< Psalmów 54 >
1 i powiedzieli do Saula: [Dawid się u nas ukrywa. ] Boże, wybaw mnie twoim imieniem i twoją mocą broń mojej sprawy.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Boże, wysłuchaj mojej modlitwy, nakłoń ucha ku słowom moich ust.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Gdyż obcy powstali przeciwko mnie, a okrutnicy czyhają na moją duszę; nie mają Boga przed oczami. (Sela)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Oto Bóg jest moim pomocnikiem; Pan jest z tymi, którzy podtrzymują moje życie.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Odpłaci złem moim wrogom; w twojej prawdzie wytrać ich.
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Będę ci dobrowolnie składał ofiary, będę wysławiał twoje imię, PANIE, bo jest dobre.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 Uwolniłeś mnie bowiem z każdego utrapienia, a moje oko widziało [zemstę] nad moimi wrogami.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.