< Psalmów 32 >

1 Psalm Dawida. Pieśń pouczająca. Błogosławiony [ten], komu przebaczono występek, komu grzech zakryto.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Błogosławiony człowiek, któremu PAN nie poczytuje nieprawości i w którego duchu nie ma podstępu.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Gdy milczałem, moje kości schły od moich całodziennych narzekań.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 We dnie i w nocy bowiem ciążyła na mnie twoja ręka, usychałem jak podczas letniej suszy. (Sela)
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Wyznałem ci swój grzech i nie kryłem mojej nieprawości. Powiedziałem: Wyznam moje występki PANU, a ty przebaczyłeś nieprawość mego grzechu. (Sela)
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 Dlatego do ciebie będzie się modlił każdy pobożny w czasie, gdy można cię znaleźć; nawet w czasie powodzi wielkich wód, one go nie dosięgną.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Ty jesteś moim schronieniem, zachowasz mnie od ucisku; otaczasz [mnie] pieśniami wybawienia. (Sela)
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Pouczę cię i nauczę cię drogi, którą masz kroczyć, poprowadzę cię swoim okiem.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Nie bądźcie bezrozumni jak koń [czy] jak muł, których pyski trzeba okiełznać uzdą i wędzidłem, aby się na ciebie nie porywały.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Wiele cierpień [spada] na niegodziwego, lecz ufającego PANU otoczy miłosierdzie.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Weselcie się w PANU i radujcie się sprawiedliwi, wykrzykujcie [radośnie], wszyscy prawego serca.
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Psalmów 32 >