< Psalmów 27 >

1 Psalm Dawida. PAN jest moją światłością i moim zbawieniem, kogóż będę się bać? PAN jest mocą mego życia, kogóż mam się lękać?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 Gdy złoczyńcy, moi przeciwnicy i wrogowie, wystąpili przeciwko mnie, aby pożreć moje ciało, potknęli się i upadli.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Choćby wojsko rozbiło naprzeciw mnie obóz, moje serce się nie ulęknie; choćby wojna wybuchła przeciw mnie, nawet wtedy będę ufał.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 O jedno proszę PANA i o to będę zabiegał: abym mieszkał w domu PANA po wszystkie dni mego życia, abym oglądał piękno PANA i dowiadywał się w jego świątyni.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 Skryje mnie bowiem w dniu niedoli w swoim przybytku, schowa mnie w ukryciu swego namiotu [i] wyniesie mnie na skałę.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 A teraz moja głowa będzie wzniesiona nad moimi nieprzyjaciółmi, którzy mnie otaczają; będę składał w jego przybytku ofiary radości, będę śpiewał i oddawał PANU chwałę.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Usłysz, PANIE, mój głos, [gdy] wołam; zmiłuj się nade mną i wysłuchaj mnie.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 [Gdy mówiłeś]: Szukajcie mojego oblicza, moje serce mówiło do ciebie: Twojego oblicza, PANIE, będę szukać.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Nie ukrywaj przede mną twojego oblicza ani nie odtrącaj w gniewie swego sługi; ty jesteś moją pomocą, nie opuszczaj mnie i nie odchodź, Boże mego zbawienia.
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Choćby ojciec i matka opuścili mnie, to PAN mnie przygarnie.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Naucz mnie, PANIE, twojej drogi i prowadź mnie ścieżką prostą ze względu na moich wrogów.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Nie wydawaj mnie na pastwę moich nieprzyjaciół, bo powstali przeciwko mnie fałszywi świadkowie i ci, którzy dyszą okrucieństwem.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 [Zniechęciłbym się], gdybym nie wierzył, że będę oglądał dobroć PANA w ziemi żyjących.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Oczekuj PANA, bądź dzielny, [a on] umocni twoje serce; oczekuj więc PANA.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.

< Psalmów 27 >