< Psalmów 26 >
1 Psalm Dawida. Osądź mnie, PANIE, bo postępuję uczciwie, zaufałem PANU i nie zachwieję się.
Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
2 Zbadaj mnie, PANIE, i doświadcz mnie; poddaj próbie moje nerki i serce.
Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
3 Mam bowiem twoje miłosierdzie przed oczyma i postępuję w twojej prawdzie.
pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
4 Nie zasiadałem z ludźmi próżnymi i nie zadaję się z obłudnikami.
Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
5 Nienawidzę zgromadzenia złoczyńców i z niegodziwymi nie usiądę.
Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
6 Umyję w niewinności swoje ręce i obejdę twój ołtarz, PANIE;
Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
7 Aby wznosić głos dziękczynienia i opowiadać o wszystkich twoich cudach.
kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
8 PANIE, miłuję dom, w którym mieszkasz, i miejsce, gdzie przebywa twoja chwała.
Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
9 Nie zabieraj mojej duszy z grzesznikami ani mojego życia z krwawymi ludźmi;
Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10 W ich rękach jest przewrotność, a ich prawica pełna [jest] przekupstwa.
amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11 Lecz ja będę postępować uczciwie, odkup mnie i zmiłuj się nade mną.
Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
12 Moja noga stoi na równej drodze, będę błogosławił PANA w zgromadzeniach.
Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.