< Psalmów 126 >

1 Pieśń stopni. Gdy PAN odwrócił niewolę Syjonu, byliśmy jak we śnie.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
2 Wtedy usta nasze napełniły się śmiechem, a nasz język radością; wtedy mówiono między narodami: PAN uczynił wielkie rzeczy dla nich.
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 PAN uczynił dla nas wielkie rzeczy i z tego się radujemy.
Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Odwróć, PANIE, naszą niewolę jak strumienie na południu.
Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
5 Ci, którzy sieją we łzach, będą żąć z radością.
Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 Kto wychodzi z płaczem, niosąc drogie ziarno, powróci z radością, przynosząc swoje snopy.
Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

< Psalmów 126 >