< Psalmów 119 >

1 Alef Błogosławieni ci, których droga jest nieskalana, którzy zgodnie z prawem PANA postępują.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Błogosławieni ci, którzy strzegą jego świadectw i szukają go całym sercem;
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 [Którzy] nie czynią nieprawości, [ale] chodzą jego drogami.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Ty rozkazałeś pilnie przestrzegać twoich nakazów.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oby moje drogi były skierowane na przestrzeganie twoich praw!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Wtedy nie doznam wstydu, gdy będę zważał na wszystkie twoje przykazania.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Będę cię wysławiał w szczerości serca, gdy nauczę się twoich sprawiedliwych praw.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Będę przestrzegał twoich praw, nigdy mnie nie opuszczaj.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Bet W jaki sposób oczyści młodzieniec swoją ścieżkę? Gdy zachowuje się według twego słowa.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Z całego serca cię szukam, nie pozwól mi zboczyć od twoich przykazań.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 W swoim sercu zachowuję twoje słowa, aby nie zgrzeszyć przeciwko tobie.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Błogosławiony jesteś, PANIE; naucz mnie twoich praw.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Swoimi wargami opowiadam wszystkie nakazy twoich ust.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Cieszę się drogą twoich świadectw bardziej niż z wszelkiego bogactwa.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Rozmyślam o twoich przykazaniach i przypatruję się twoim drogom.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Rozkoszuję się twoimi prawami i nie zapominam twoich słów.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Gimel Okaż dobroć swemu słudze, [abym] żył i przestrzegał twoich słów.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Otwórz moje oczy, abym ujrzał cuda twego prawa.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Jestem obcym na ziemi, nie ukrywaj przede mną twoich przykazań.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Moja dusza omdlewa, tęskniąc cały czas za twoimi sądami.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Zgromiłeś pysznych, przeklęci [są ci], którzy odstępują od twoich przykazań.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Oddal ode mnie hańbę i wzgardę, gdyż przestrzegam twoich świadectw.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Władcy też zasiadają i mówią przeciwko mnie, lecz twój sługa rozmyśla o twoich prawach.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Twoje świadectwa też są moją rozkoszą [i] moimi doradcami.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Dalet Moja dusza przylgnęła do prochu, ożyw mnie według twego słowa.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Opowiedziałem [ci] moje drogi i wysłuchałeś mnie; naucz mnie twoich praw.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Spraw, bym zrozumiał drogę twoich nakazów, a będę rozmyślał o twoich cudownych dziełach.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Dusza moja rozpływa się [we łzach] ze smutku, umocnij mnie według twego słowa.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Oddal ode mnie drogę kłamstwa, a obdarz mnie swoim prawem.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Wybrałem drogę prawdy, a twoje nakazy stawiam [przed sobą].
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Przylgnąłem do twoich świadectw; PANIE, nie pozwól mi zaznać wstydu.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Pobiegnę drogą twoich przykazań, gdy rozszerzysz moje serce.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 He Naucz mnie, PANIE, drogi twoich praw, a będę jej strzegł [aż] do końca.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Daj mi rozum, abym zachował twoje prawo; żebym go przestrzegał z całego serca.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Spraw, bym chodził ścieżką twoich przykazań, gdyż w nich mam upodobanie.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Nakłoń moje serce do twoich świadectw, a nie do chciwości.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Odwróć moje oczy, aby nie patrzyły na marność, ożyw mnie na twojej drodze.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Utwierdź swoje słowo względem twego sługi, który się oddał twojej bojaźni.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Oddal ode mnie mą hańbę, której się boję, bo twoje sądy [są] dobre.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Oto pragnę twoich nakazów; ożyw mnie w swej sprawiedliwości.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Waw Niech zstąpi na mnie twoja łaskawość, PANIE, twoje zbawienie według twego słowa;
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Abym mógł dać odpowiedź temu, który mi urąga, bo ufam twojemu słowu.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 I nie wyjmuj z moich ust słowa prawdy, bo twoich sądów oczekuję.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 I będę zawsze strzegł twego prawa, na wieki wieków.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 A będę chodził drogą przestronną, bo szukam twoich nakazów.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Owszem, będę mówił o twoich świadectwach przed królami i nie doznam wstydu.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Będę się rozkoszował twoimi przykazaniami, które umiłowałem.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Wznoszę też swoje ręce ku twoim przykazaniom, które miłuję, i będę rozmyślał o twoich prawach.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Zain Pamiętaj o słowie danym twemu słudze, na którym [to słowie] kazałeś mi polegać.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 To jest moja pociecha w utrapieniu, bo twoje słowo mnie ożywia.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Pyszni bardzo się ze mnie naśmiewają, lecz nie odstępuję od twego prawa.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Pamiętam o twoich wiecznych sądach, PANIE, i pocieszam się nimi.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Strach mnie ogarnął z powodu niegodziwych, którzy porzucają twoje prawo.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Twoje prawa są dla mnie pieśniami w domu mego pielgrzymowania.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Nocą wspominam twoje imię, PANIE, i strzegę twego prawa.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 To mam, bo przestrzegam twoich przykazań.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Het PANIE, [ty jesteś] moim udziałem, przyrzekłem przestrzegać twoich słów.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Modliłem się przed twoim obliczem z całego serca, zlituj się nade mną według twego słowa.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Rozmyślałem nad moimi drogami i zwracałem kroki ku twoim świadectwom.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Spieszyłem się i nie zwlekałem z przestrzeganiem twoich przykazań.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Hufce niegodziwych złupiły mnie, [ale] nie zapominam twojego prawa.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 O północy wstaję, aby wysławiać cię za twoje sprawiedliwe sądy.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Jestem przyjacielem wszystkich, którzy boją się ciebie, i tych, którzy przestrzegają twoich przykazań.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 PANIE, ziemia jest pełna twego miłosierdzia; naucz mnie twoich praw.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Tet Wyświadczyłeś dobro twemu słudze, PANIE, według twego słowa.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Naucz mnie trafnego sądu i wiedzy, bo uwierzyłem twoim przykazaniom.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Zanim doznałem utrapienia, błądziłem; lecz teraz przestrzegam twego słowa.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Jesteś dobry i czynisz dobro; naucz mnie twoich praw.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Zuchwali zmyślili przeciwko mnie kłamstwo, [ale] ja całym sercem strzegę twoich przykazań.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Serce ich utyło jak sadło, [ale] ja rozkoszuję się twoim prawem.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Dobrze to dla mnie, że zostałem uciśniony, abym się nauczył twoich praw.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Prawo twoich ust [jest] lepsze dla mnie niż tysiące [sztuk] złota i srebra.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Jod Twoje ręce mnie uczyniły i ukształtowały; daj mi rozum, abym się nauczył twoich przykazań;
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Bojący się ciebie, widząc mnie, będą się radować, że pokładam nadzieję w twoim słowie.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Wiem, PANIE, że twoje sądy [są] sprawiedliwe i [że] słusznie mnie trapiłeś.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Proszę cię, niech mnie ucieszy twoje miłosierdzie według twego słowa do twego sługi.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Niech przyjdzie na mnie twoje miłosierdzie, abym żył; bo twoje prawo jest moją rozkoszą.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Niech się zawstydzą zuchwali, bo niesłusznie znieważali mnie, ale ja będę rozmyślać o twoich przykazaniach.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Niech się zwrócą do mnie ci, którzy się boją ciebie, i ci, którzy znają twoje świadectwa.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Niech moje serce będzie nienaganne w twoich prawach, abym nie doznał wstydu.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Kaf Moja dusza tęskni do twego zbawienia, pokładam nadzieję w twoim słowie.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Moje oczy słabną, [czekając] na twoje słowo, gdy mówię: Kiedy mnie pocieszysz?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Chociaż jestem jak bukłak w dymie, [jednak] nie zapomniałem twoich praw.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Ile będzie dni twego sługi? Kiedy wykonasz wyrok na tych, którzy mnie prześladują?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Doły wykopali dla mnie zuchwali, którzy nie postępują według twego prawa.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Wszystkie twoje przykazania są prawdą; bez powodu mnie prześladują; pomóż mi.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Omal nie zgładzili mnie na ziemi; ja zaś nie porzuciłem twoich przykazań.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Według twego miłosierdzia ożyw mnie, abym strzegł świadectwa twoich ust.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Lamed Na wieki, o PANIE, twoje słowo trwa w niebie.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Z pokolenia na pokolenie twoja prawda; ugruntowałeś ziemię i trwa.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 [Wszystko] trwa do dziś według twego rozporządzenia; to wszystko służy tobie.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Gdyby twoje prawo nie było moją rozkoszą, dawno zginąłbym w moim utrapieniu.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Nigdy nie zapomnę twoich przykazań, bo nimi mnie ożywiłeś.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Twoim jestem, wybaw mnie, bo szukam twoich przykazań.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Czyhają na mnie niegodziwi, aby mnie stracić, [ale ja] rozważam twoje świadectwa.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Widziałem koniec wszelkiej doskonałości, [ale] twoje przykazanie jest bezkresne.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Mem O, jakże miłuję twoje prawo! Przez cały dzień o nim rozmyślam.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Czynisz mnie mądrzejszym od moich nieprzyjaciół dzięki twoim przykazaniom, bo mam je zawsze przed sobą.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Stałem się rozumniejszy od wszystkich moich nauczycieli, bo rozmyślam o twoich świadectwach.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Jestem roztropniejszy od starszych, bo przestrzegam twoich przykazań.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Powstrzymuję swoje nogi od wszelkiej drogi złej, abym strzegł twego słowa.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Nie odstępuję od twoich nakazów, bo ty mnie uczysz.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 O, jakże słodkie są twoje słowa dla mego podniebienia! [Są słodsze] niż miód dla moich ust.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Dzięki twoim przykazaniom nabywam rozumu; dlatego nienawidzę wszelkiej ścieżki fałszywej.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Nun Twoje słowo jest pochodnią dla moich nóg i światłością na mojej ścieżce.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Złożyłem przysięgę i wypełnię ją, będę przestrzegał twoich sprawiedliwych nakazów.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Jestem bardzo strapiony; PANIE, ożyw mnie według słowa twego.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 PANIE, przyjmij dobrowolne ofiary moich ust i naucz mnie twoich nakazów.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Moja dusza jest stale w niebezpieczeństwie, ale nie zapominam twojego prawa.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Niegodziwi zastawili na mnie sidła, lecz [ja] nie odstępuję od twoich przykazań.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Wziąłem twoje świadectwa jako wieczne dziedzictwo, bo są radością mego serca.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Nakłoniłem moje serce, by zawsze wykonywać twoje prawa, aż do końca.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Samech Nienawidzę [chwiejnych] myśli, ale miłuję twoje prawo.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Ty jesteś moją ucieczką i tarczą, pokładam nadzieję w twoim słowie.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Odstąpcie ode mnie, złoczyńcy, będę strzegł przykazania mojego Boga.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Wesprzyj mnie według słowa twego, abym żył, i niech nie doznam wstydu ze względu na moją nadzieję.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Podtrzymaj mnie, a będę wybawiony i będę rozmyślał zawsze o twoich prawach.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Podeptałeś wszystkich, którzy odstępują od twoich praw, bo ich zdrada to fałsz.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Odrzucasz [jak] żużel wszystkich niegodziwych ziemi; dlatego miłuję twoje świadectwa.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Moje ciało drży ze strachu przed tobą, bo lękam się twoich sądów.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Ajin Sprawowałem sąd i sprawiedliwość; nie wydawaj mnie moim ciemięzcom.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Bądź poręczycielem dla twego sługi ku dobremu, aby nie uciskali mnie zuchwalcy.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Moje oczy słabną, [czekając] na twoje zbawienie i na słowo twojej sprawiedliwości.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Postąp ze swoim sługą według twego miłosierdzia i naucz mnie twoich praw.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Jestem twoim sługą, daj mi rozum, abym poznał twoje świadectwa.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Już czas, PANIE, abyś działał, [bo] naruszono twoje prawo.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Dlatego umiłowałem twoje przykazania nad złoto, nad szczere złoto.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Bo wszystkie [twoje] przykazania uznaję za prawdziwe, [a] nienawidzę wszelkiej fałszywej drogi.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Pe Twoje świadectwa są przedziwne, dlatego moja dusza ich strzeże.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Początek twoich słów oświeca [i] daje rozum prostym.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Otwieram usta i wzdycham, bo pragnąłem twoich przykazań.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Spójrz na mnie i zmiłuj się nade mną, jak postępujesz z tymi, którzy miłują twoje imię.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Utwierdź moje kroki w twoim słowie, niech nie panuje nade mną żadna nieprawość.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Wybaw mnie z ludzkiego ucisku, abym strzegł twoich nakazów.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Rozjaśnij swe oblicze nad twoim sługą i naucz mnie twoich praw.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Strumienie wód płyną z mych oczu, bo nie strzegą twego prawa.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Cade Sprawiedliwy jesteś, PANIE, i słuszne [są] twoje sądy.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Twoje świadectwa, które nadałeś, są sprawiedliwe i bardzo wierne.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Gorliwość pożarła mnie, bo moi nieprzyjaciele zapominają twoje słowa.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Twoje słowo jest w pełni wypróbowane, dlatego twój sługa je kocha.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Ja jestem mały i wzgardzony, [lecz] nie zapominam twoich przykazań.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Twoja sprawiedliwość jest sprawiedliwością wieczną, a twoje prawo jest prawdą.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Ucisk i utrapienie spadły na mnie, lecz twoje przykazania są moją rozkoszą.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Sprawiedliwość twoich świadectw [trwa] na wieki; daj mi rozum, a będę żył.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Kof Wołam z całego serca, wysłuchaj mnie, o PANIE, a będę strzegł twoich praw.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Wołam do ciebie, wybaw mnie, a będę strzegł twoich świadectw.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Wstaję przed świtem i wołam, oczekuję na twoje słowo.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Moje oczy wyprzedzają straże nocne, abym mógł rozmyślać o twoim słowie.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 PANIE, usłysz mój głos według twego miłosierdzia; ożyw mnie według twego wyroku.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Zbliżają się niegodziwi prześladowcy, są daleko od twego prawa.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Blisko [jesteś], PANIE, i wszystkie twoje przykazania [są] prawdą.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Od dawna wiem o twoich świadectwach, że ugruntowałeś je na wieki.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Resz Wejrzyj na moje utrapienie i wyzwól mnie, bo nie zapomniałem twojego prawa.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Broń mojej sprawy i wybaw mnie; ożyw mnie według twego słowa.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Zbawienie [jest] daleko od niegodziwych, bo nie szukają twoich praw.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Wielka jest twoja litość, PANIE; ożyw mnie według twoich wyroków.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Liczni są moi prześladowcy i nieprzyjaciele; [lecz] nie uchylam się od twoich świadectw.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Widziałem przestępców i czułem odrazę, że nie przestrzegali twego słowa.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Patrz, jak miłuję twoje nakazy, PANIE; ożyw mnie według twego miłosierdzia.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Podstawą twego słowa [jest] prawda, a wszelki wyrok twojej sprawiedliwości [trwa] na wieki.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Szin Władcy prześladują mnie bez przyczyny; moje serce zaś boi się twoich słów.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Raduję się z twego słowa jak ten, który znajduje wielki łup.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Nienawidzę kłamstwa i brzydzę się [nim, ale] miłuję twoje prawo.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Chwalę cię siedem razy dziennie za twoje sprawiedliwe sądy.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Wielki pokój dla tych, którzy miłują twoje prawo, a nie doznają żadnego zgorszenia.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 PANIE, oczekuję na twoje zbawienie i zachowuję twoje przykazania.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Moja dusza przestrzega twoich świadectw, bo bardzo je miłuję.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Przestrzegam twoich przykazań i świadectw, bo wszystkie moje drogi są przed tobą.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Taw PANIE, niech dotrze moje wołanie przed twoje oblicze, daj mi zrozumienie według słowa twego.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Niech dojdzie moja prośba przed twoje oblicze, ocal mnie według twojej obietnicy.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Moje wargi wygłoszą chwałę, gdy nauczysz mnie twoich praw.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Mój język będzie głosił twoje słowo, bo wszystkie twoje przykazania są sprawiedliwością.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Niech twoja ręka będzie mi pomocą, [bo] wybrałem twoje przykazania.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 PANIE, pragnę twego zbawienia, a twoje prawo [jest] moją rozkoszą.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Pozwól mojej duszy żyć, a będzie cię chwalić; niech twoje nakazy będą dla mnie pomocą.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Błądzę jak zgubiona owca; szukaj twego sługi, bo nie zapominam twoich przykazań.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalmów 119 >