< Psalmów 108 >

1 Pieśń. Psalm Dawida. Boże, moje serce jest gotowe; będę ci śpiewać i wysławiać cię, także i moja chwała.
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 Obudź się, cytro i harfo, gdy o świcie powstanę.
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 Będę cię wysławiać wśród ludu, PANIE, będę ci śpiewał wśród narodów.
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 Twoje miłosierdzie bowiem jest wielkie, [sięga] ponad niebiosa, a twoja prawda aż pod obłoki.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Bądź wywyższony ponad niebiosa, Boże, a twoja chwała ponad całą ziemię;
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 Aby twoi umiłowani byli ocaleni, wybaw ich swoją prawicą i wysłuchaj mnie.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 Bóg przemówił w swej świętości: Będę się weselić, rozdzielę Sychem, a dolinę Sukkot wymierzę.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 Mój [jest] Gilead, mój i Manasses, Efraim mocą mojej głowy, Juda moim prawodawcą.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 Moab jest moją miednicą do mycia, na Edom rzucę moje obuwie, nad Filisteą zatriumfuję.
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 Kto mnie wprowadzi do miasta warownego? Kto mnie doprowadzi aż do Edomu?
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Czy nie [ty], Boże, [który] nas odrzuciłeś? Czy nie wyruszysz, Boże, z naszymi wojskami?
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 Udziel nam pomocy w ucisku, bo próżna jest pomoc ludzka.
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 W Bogu będziemy mężni, on podepcze naszych wrogów.
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< Psalmów 108 >