< Psalmów 102 >

1 Modlitwa strapionego, gdy uciśniony wylewa przed PANEM swoją skargę. PANIE, wysłuchaj mojej modlitwy i niech przyjdzie do ciebie moje wołanie.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Nie ukrywaj przede mną swego oblicza, w dniu mego ucisku nakłoń ku mnie swego ucha; w dniu, w którym cię wzywam, szybko mnie wysłuchaj.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Moje dni bowiem nikną jak dym, a moje kości są rozpalone jak ognisko.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Moje serce jest porażone i usycha jak trawa, [tak] że zapomniałem jeść chleb.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Od głosu mego wołania moje kości przylgnęły mi do ciała.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Jestem podobny do pelikana na pustyni, jestem jak sowa na pustkowiu.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Czuwam i jestem jak samotny wróbel na dachu.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Przez cały dzień znieważają mnie moi wrogowie i przeklinają mnie ci, którzy szaleją przeciwko mnie.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Jadam bowiem popiół jak chleb, a mój napój mieszam ze łzami;
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 Z powodu twego gniewu i zapalczywości, bo podniosłeś mnie i strąciłeś.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Moje dni są jak chylący się cień, a ja usycham jak trawa.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Ale ty, PANIE, trwasz na wieki, a twoja pamięć z pokolenia na pokolenie.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Powstaniesz i zmiłujesz się nad Syjonem, bo czas, byś się nad nim zlitował, gdyż nadszedł czas wyznaczony.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Twoi słudzy bowiem miłują jego kamienie i litują się nad jego prochem;
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 A poganie będą się bać imienia PANA i wszyscy królowie ziemi – twojej chwały;
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Gdy PAN odbuduje Syjon i ukaże się w swojej chwale;
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Przychyli się do modlitwy opuszczonych i nie pogardzi ich modlitwą.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Zapiszą to dla przyszłego pokolenia, a lud, który ma być stworzony, będzie chwalić PANA.
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 Spojrzał bowiem z wysokości swojej świątyni; PAN popatrzył z nieba na ziemię;
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 Aby wysłuchać jęku więźniów i uwolnić skazanych na śmierć;
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Aby głosili na Syjonie imię PANA i jego chwałę w Jeruzalem;
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 Gdy się zgromadzą razem narody i królestwa, aby służyć PANU.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Osłabił w drodze moją siłę, skrócił moje dni.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Powiedziałem: Mój Boże, nie zabieraj mnie w połowie moich dni; twoje lata bowiem [trwają] z pokolenia na pokolenie.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Ty dawno założyłeś [fundamenty] ziemi i niebiosa są dziełem twoich rąk.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 One przeminą, ale ty pozostajesz; wszystkie jak szata się zestarzeją, zmienisz je jak płaszcz i będą odmienione.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Ale ty [zawsze jesteś] ten sam, a twoje lata nigdy się nie skończą.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Synowie twoich sług będą trwać [u ciebie], a ich potomstwo zostanie przed tobą utwierdzone.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Psalmów 102 >