< Przysłów 9 >
1 Mądrość zbudowała sobie dom [i] wyciosała siedem słupów;
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 Zabiła swoje bydło, zmieszała wino i zastawiła stół;
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 Rozesłała swoje służące, woła na szczytach najwyższych miejsc miasta:
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 Ktokolwiek jest prostym, niech wstąpi; [a] do nierozumnego mówi:
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Chodźcie, jedzcie mój chleb i pijcie wino, które zmieszałam.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Porzućcie głupotę, a będziecie żyli, i chodźcie drogą roztropności.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 Kto upomina szydercę, ściąga na siebie hańbę, a kto strofuje niegodziwego, ten się plami.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 Nie strofuj szydercy, aby cię nie znienawidził; strofuj mądrego, a będzie cię miłował.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Upomnij mądrego, a będzie mądrzejszy; poucz sprawiedliwego, a pomnoży swą wiedzę.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 Początkiem mądrości [jest] bojaźń PANA, a wiedza o tym, co święte, to rozum.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 Bo dzięki mnie rozmnożą się twoje dni i przedłużą się lata [twojego] życia.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 Jeśli będziesz mądry, tobie samemu będzie [służyła] twoja mądrość; a jeśli szydercą, sam poniesiesz szkodę.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 Głupia kobieta [jest] wrzaskliwa, prosta i nic nie rozumie;
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 Siedzi u drzwi swego domu, na krześle, na wysokich miejscach w mieście;
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 Aby wołać na przechodzących, którzy idą prosto swoimi ścieżkami:
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Ktokolwiek jest prosty, niech wstąpi; a do nierozumnego mówi:
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Kradzione wody są słodkie, a chleb jedzony pokątnie smaczny.
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 Ale [on] nie wie, że tam są umarli, że jej zaproszeni [są] w głębinach piekła. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )