< Przysłów 30 >

1 Słowa Agura, syna Jake, proroctwo tego człowieka do Itiela, do Itiela i Ukala.
Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 Zaprawdę jestem najgłupszym z ludzi i nie mam ludzkiego rozumu.
“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 Ani nie nauczyłem się mądrości, ani nie mam wiedzy o tym, co święty.
Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 Któż wstąpił do nieba i zstąpił? Któż zebrał wiatr w swoje garście? Któż zgarnął wody do [swej] szaty? Któż utwierdził wszystkie krańce ziemi? Jakie [jest] jego imię? A jakie [jest] imię jego syna? Czy wiesz?
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 Każde słowo Boga jest czyste; on [jest] tarczą dla tych, którzy mu ufają.
“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 Nie dodawaj nic do jego słów, aby cię nie strofował i abyś nie okazał się kłamcą.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 Proszę cię o dwie rzeczy; nie odmawiaj mi [ich], zanim umrę.
“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
8 Oddal ode mnie marność i słowo kłamliwe; nie dawaj mi ani ubóstwa, ani bogactwa; żyw mnie odpowiednim dla mnie pokarmem;
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 Abym będąc syty, nie zaparł się [ciebie] i nie mówił: Kim jest PAN? Albo zubożawszy, nie kradł i nie brał imienia mego Boga [nadaremnie].
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 Nie oczerniaj sługi przed jego panem, aby ci nie złorzeczył i byś nie okazał się winny.
“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 [Jest] pokolenie, które złorzeczy swemu ojcu i nie błogosławi swojej matce.
“Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
12 [Jest] pokolenie, które we własnych oczach jest czyste, lecz nie jest obmyte ze swego plugastwa.
Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 [Jest] pokolenie, którego oczy są wyniosłe i powieki wzniesione.
Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
14 [Jest] pokolenie, którego zęby [są jak] miecze, a zęby trzonowe [jak] noże, by pożreć ubogich na ziemi i nędzarzy spośród ludzi.
Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 Pijawka ma dwie córki, [które mówią]: Daj, daj. Trzy są rzeczy, które nie mogą się nasycić; cztery, które nie mówią: Dość.
“Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 Grób, niepłodne łono, ziemia niesyta wody i ogień, [który] nie mówi: Dość. (Sheol h7585)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
17 Oko, [które] wyśmiewa ojca i gardzi posłuszeństwem matce, wydziobią kruki [nad] potokami i wyjedzą orlęta.
Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 Trzy [są] rzeczy dla mnie zbyt zdumiewające, czterech nie znam:
Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 Drogi orła w powietrzu, drogi węża na skale, drogi okrętu na środku morza i drogi mężczyzny z młodą kobietą.
Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 Taka [jest] droga kobiety cudzołożnej: je i obciera swoje usta, i mówi: Nie zrobiłam nic złego.
Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 Pod trzema rzeczami drży ziemia, czterech nie może znieść:
Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 Sługi, kiedy panuje, głupca, kiedy syci się chlebem;
Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
23 Obmierzłej [kobiety], kiedy wychodzi za mąż, [i] służącej, kiedy dziedziczy po swojej pani.
mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 Cztery są rzeczy najmniejsze na ziemi, jednak mędrsze nad mędrców:
Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Mrówki, lud słaby, a jednak w lecie przygotowują pokarm;
Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 Króliki, lud słaby, a jednak budują swój dom w skale;
mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 Szarańcze nie mają króla, a jednak wszystkie wyruszają chmarą;
dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Pająk pracuje rękoma, a bywa w pałacach królewskich.
Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 Trzy są rzeczy, które poruszają się wspaniale, cztery kroczą dostojnie:
“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 Lew, najsilniejszy wśród zwierząt, który przed nikim nie ustępuje;
Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 Chart i kozioł, i król, przeciw któremu nikt nie powstaje.
Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 Jeśli głupio postąpiłeś, wynosząc się, albo jeśli pomyślałeś źle, [połóż] rękę na ustach.
“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Jak ubijanie mleka daje masło i wycieranie nosa wywołuje krew, tak kto wzbudza gniew, wszczyna kłótnię.
Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

< Przysłów 30 >