< Przysłów 23 >
1 Gdy usiądziesz do posiłku z władcą, zważaj pilnie, co jest przed tobą;
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 I przyłóż nóż do gardła, jeśli jesteś łakomy.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Nie pragnij jego przysmaków, bo to pokarm zwodniczy.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Nie zabiegaj o bogactwo, porzuć swoją mądrość.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Czy obrócisz swoje oczy na to, co jest niczym? Bo bogactwa robią sobie skrzydła i ulatują do nieba jak orzeł.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Nie jedz chleba człowieka, który ma złe oko, ani nie pożądaj jego przysmaków.
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 Bo jak myśli w swym sercu, taki [on jest]. Jedz i pij – mówi do ciebie, ale jego serce nie jest z tobą.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Kęs, który zjadłeś, zwrócisz i utracisz swoje wdzięczne słowa.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Nie mów do uszu głupca, bo wzgardzi mądrością twoich słów.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Nie przesuwaj dawnej granicy i nie wchodź na pole sierot.
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 Bo ich obrońca jest mocny, przeprowadzi ich sprawę przeciwko tobie.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Nakłoń swoje serce na pouczenie, a swe uszy na słowa rozumne.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Nie szczędź dziecku karcenia, [bo] jeśli je bijesz rózgą, nie umrze.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Będziesz je bił rózgą, a jego duszę ocalisz od piekła. (Sheol )
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
15 Synu mój, jeśli twoje serce będzie mądre, moje serce będzie się radowało, właśnie moje;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 I moje nerki będą się weselić, gdy twoje usta będą mówiły to, co jest prawe.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Niech twoje serce nie zazdrości grzesznikom, lecz każdego dnia [postępuj] w bojaźni PANA;
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Bo koniec jest pewny i twoja nadzieja nie będzie zawiedziona.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Słuchaj, synu mój, i bądź mądry, i skieruj swoje serce na drogę.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Nie bywaj wśród pijaków ani wśród obżerających się mięsem;
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Bo pijak i żarłok zubożeją, a ospały będzie chodził w łachmanach.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Słuchaj ojca, który cię spłodził, a nie gardź matką, gdy się zestarzeje.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Kupuj prawdę i nie sprzedawaj [jej]; [kupuj] mądrość, karność i rozum.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Ojciec sprawiedliwego będzie się wielce radował, a kto spłodzi mądrego, będzie się z niego cieszył.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Niech się weseli twój ojciec i matka i niech się raduje ta, która cię rodziła.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Synu mój, daj mi swoje serce, a niech twoje oczy strzegą moich dróg.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Bo nierządnica [jest] głębokim dołem, a cudza [kobieta jest] ciasną studnią.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Ona też czyha jak zbój i pomnaża przewrotnych wśród ludzi.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 U kogo biada? U kogo żal? U kogo kłótnie? U kogo szemranie? Kto ma rany bez powodu? Kto ma zaczerwienione oczy?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Ci, którzy przesiadują przy winie; ci, którzy idą szukać zmieszanego wina.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Nie patrz na wino, gdy się czerwieni; gdy wydaje łunę swą w kielichu, a samo się przesuwa.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 Na koniec ugryzie jak wąż i ukąsi jak żmija;
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Twoje oczy będą patrzeć na cudze kobiety, a twoje serce będzie mówiło rzeczy przewrotne;
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 I będziesz jak ten, który leży na środku morza, i jak ten, który śpi na szczycie masztu;
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 [Powiesz]: Bili mnie, a nie bolało, uderzyli mnie, a [nic] nie czułem. Gdy się obudzę, znów go poszukam.
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”