< Przysłów 17 >

1 Lepszy [jest] kęs suchego [chleba], a przy tym spokój, niż dom pełen bydła ofiarnego z kłótnią.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 Sługa roztropny będzie panował nad synem, który przynosi hańbę, i wraz z [jego] braćmi będzie miał udział w dziedzictwie.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 Tygiel dla srebra, piec dla złota, ale serca bada PAN.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 Zły zważa na wargi fałszywe, a kłamca słucha przewrotnego języka.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Kto naśmiewa się z ubogiego, uwłacza jego Stwórcy, a kto się cieszy z nieszczęścia, nie uniknie kary.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Koroną starców są synowie synów, a chlubą synów są ich ojcowie.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Poważna mowa nie przystoi głupiemu, tym mniej kłamliwe usta dostojnikowi.
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 Dar jest [jak] drogocenny kamień w oczach tego, kto go posiada; gdziekolwiek [z nim] zmierza, ma powodzenie.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 Kto kryje grzech, szuka miłości, a kto wyjawia sprawę, rozdziela przyjaciół.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 Nagana lepiej działa na rozumnego niż sto razów na głupiego.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 Zły szuka jedynie buntu; dlatego zostanie wysłany przeciw niemu okrutny posłaniec.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 [Lepiej] człowiekowi spotkać się z niedźwiedzicą, której zabrano młode, niż z głupim w jego głupocie.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Kto odpłaca złem za dobro, temu zło z domu nie ustąpi.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 Kto zaczyna kłótnię, [jest jak] ten, co puszcza wodę; [dlatego] zaniechaj sporu, zanim wybuchnie.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 Kto usprawiedliwia niegodziwego i kto potępia sprawiedliwego, obaj budzą odrazę w PANU.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 Na cóż w ręku głupiego pieniądze, by zdobyć mądrość, [skoro] nie ma rozumu?
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 Przyjaciel kocha w każdym czasie, a brat rodzi się w nieszczęściu.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 Nierozumny człowiek daje porękę i ręczy na oczach przyjaciela.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 Kto kocha grzech, kocha spór, a kto podwyższa swoją bramę, szuka zagłady.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 Przewrotny w sercu nie znajduje dobra, a kto ma przewrotny język, wpadnie w zło.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 Kto spłodzi głupca, [zrobi to] na swój smutek, a ojciec głupiego nie doznaje radości.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 Wesołe serce działa dobrze [jak] lekarstwo, a przygnębiony duch wysusza kości.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 Niegodziwy bierze dar z zanadrza, aby wypaczać ścieżki sądu.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Mądrość [jest] przed obliczem rozumnego, a oczy głupca są aż na krańcu ziemi.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 Głupi syn jest zmartwieniem dla ojca i goryczą dla rodzicielki.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 Zaprawdę to niedobrze wymierzyć karę sprawiedliwemu ani bić władców za prawość.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 Kto ma wiedzę, powściąga swoje słowa, człowiek roztropny [jest] zacnego ducha.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Nawet głupi, gdy milczy, uchodzi za mądrego, [a] kto zamyka swoje wargi – za rozumnego.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< Przysłów 17 >