< Przysłów 12 >

1 Kto kocha karność, kocha wiedzę, a kto nienawidzi upomnienia, jest głupi.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 Dobry [człowiek] zdobędzie łaskę PANA, ale [PAN] potępi podstępnego.
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 Człowiek nie umocni się niegodziwością, lecz korzeń sprawiedliwych nie będzie poruszony.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 Żona cnotliwa [jest] koroną swego męża, ale ta, która go hańbi, [jest] jak zgnilizna w jego kościach.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 Myśli sprawiedliwych są prawe, a rady niegodziwych zdradliwe.
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 Słowa niegodziwych czyhają na krew, lecz usta prawych ocalą ich.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 Niegodziwi zostają powaleni i już ich nie ma, a dom sprawiedliwych się ostoi.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 Człowiek będzie chwalony za jego mądrość, a kto jest przewrotnego serca, zostanie wzgardzony.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 Lepszy [jest człowiek] wzgardzony, który ma sługę, niż ten, kto się chwali, a któremu brak chleba.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 Sprawiedliwy dba o życie swego bydła, a serce niegodziwych jest okrutne.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 Kto uprawia swoją ziemię, nasyci się chlebem, a kto naśladuje próżnujących, jest nierozumny.
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 Niegodziwy pragnie sieci złych, a korzeń sprawiedliwych wydaje [owoc].
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 Zły zostaje usidlony przez grzech swoich warg, a sprawiedliwy wyjdzie z ucisku.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 Człowiek nasyci się dobrem z owocu swoich ust, a za [dzieła] swoich rąk otrzyma zapłatę.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 Droga głupiego [wydaje się] słuszna w jego oczach, ale kto słucha rady, jest mądry.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 Gniew głupiego objawia się od razu, a roztropny skrywa hańbę.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 Kto mówi prawdę, wyraża sprawiedliwość, ale fałszywy świadek – oszustwo.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 Znajdzie się taki, którego [słowa] są jak miecz przeszywający, lecz język mądrych [jest] lekarstwem.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 Prawdomówne wargi będą trwać na wieki, ale język kłamliwy [trwa] króciutko.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 Podstęp [jest] w sercu tych, którzy knują zło, lecz u doradzających pokój [jest] radość.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 Sprawiedliwego nie spotka żadne zło, ale niegodziwi będą pełni nieszczęścia.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 Wargi kłamliwe budzą odrazę w PANU, a ci, którzy postępują w prawdzie, podobają mu się.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 Człowiek roztropny ukrywa wiedzę, a serce głupich rozgłasza głupotę.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 Ręka pracowitych będzie panowała, a leniwa będzie płaciła daninę.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 Troska w sercu człowieka przygnębia je, a dobre słowo je rozwesela.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 Sprawiedliwy jest zacniejszy od swego bliźniego, a droga niegodziwych prowadzi ich na manowce.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 Leniwy nie upiecze tego, co upolował, ale mienie człowieka pracowitego [jest] cenne.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 Na ścieżce sprawiedliwości jest życie, na jej drodze nie ma śmierci.
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Przysłów 12 >