< Liczb 1 >
1 PAN przemówił do Mojżesza na pustyni Synaj, w Namiocie Zgromadzenia, pierwszego [dnia] drugiego miesiąca, w drugim roku po ich wyjściu z ziemi Egiptu, tymi słowy:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 Policzcie całe zgromadzenie synów Izraela według ich rodzin i według domów ich ojców, licząc imiona wszystkich mężczyzn, głowa po głowie;
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 Od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich w Izraelu zdolnych do walki. Ty i Aaron policzycie ich według ich oddziałów.
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 I będzie z wami jeden mężczyzna z każdego pokolenia, głowa domu swoich ojców.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 A oto imiona mężczyzn, którzy będą z wami: z [pokolenia] Rubena – Elizur, syn Szedeura;
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 Z Symeona – Szelumiel, syn Suriszaddaja;
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 Z Judy – Nachszon, syn Amminadaba;
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 Z Issachara – Netaneel, syn Suara;
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 Z Zebulona – Eliab, syn Chelona;
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 Z synów Józefa: z Efraima – Eliszama, syn Ammihuda, z Manassesa – Gamliel, syn Pedahsura;
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 Z Beniamina – Abidan, syn Gideoniego;
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 Z Dana – Achiezer, syn Ammiszaddaja;
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 Z Aszera – Pagiel, syn Okrana;
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 Z Gada – Eliasaf, syn Deuela;
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 Z Neftalego – Achira, syn Enana.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 Ci powołani, [sławni] spośród zgromadzenia, byli naczelnikami pokoleń swych ojców, wodzami tysięcy w Izraelu.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 Mojżesz i Aaron przyjęli więc tych mężczyzn, którzy zostali imiennie wyznaczeni.
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 I zebrali całe zgromadzenie w pierwszym dniu drugiego miesiąca, a każdy podawał swoje pochodzenie według swych rodzin, według domów swych ojców i według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, głowa po głowie.
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 Jak PAN rozkazał Mojżeszowi, tak policzył ich na pustyni Synaj.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 Synów Rubena, pierworodnego Izraela, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, głowa po głowie, wszystkich mężczyzn od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 Naliczono z pokolenia Rubena czterdzieści sześć tysięcy pięciuset.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Synów Symeona, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, naliczonych według liczby imion, głowa po głowie, wszystkich mężczyzn od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 Naliczono z pokolenia Symeona pięćdziesiąt dziewięć tysięcy trzystu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Synów Gada, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 Naliczono z pokolenia Gada czterdzieści pięć tysięcy sześciuset pięćdziesięciu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 Synów Judy, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 Naliczono z pokolenia Judy siedemdziesiąt cztery tysiące sześciuset.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 Synów Issachara, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 Naliczono z pokolenia Issachara pięćdziesiąt cztery tysiące czterystu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 Synów Zebulona, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 Naliczono z pokolenia Zebulona pięćdziesiąt siedem tysięcy czterystu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 Synów Józefa, z synów Efraima, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 Naliczono z pokolenia Efraima czterdzieści tysięcy pięciuset.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 Synów Manassesa, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 Naliczono z pokolenia Manassesa trzydzieści dwa tysiące dwustu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 Synów Beniamina, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 Naliczono z pokolenia Beniamina trzydzieści pięć tysięcy czterystu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 Synów Dana, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 Naliczono z pokolenia Dana sześćdziesiąt dwa tysiące siedmiuset.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 Synów Aszera, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 Naliczono z pokolenia Aszera czterdzieści jeden tysięcy pięciuset.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 Synów Neftalego, ich potomków według ich rodzin, według domów ich ojców, według liczby imion, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki;
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 Naliczono z pokolenia Neftalego pięćdziesiąt trzy tysiące czterystu.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 To są ci, których policzyli Mojżesz, Aaron i książęta Izraela, dwunastu mężczyzn, po jednym z każdego domu swych ojców.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 I było wszystkich policzonych synów Izraela, według domów ich ojców, od dwudziestu lat wzwyż, wszystkich zdolnych do walki w Izraelu;
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 Wszystkich policzonych było sześćset trzy tysiące pięciuset pięćdziesięciu.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 Lecz Lewici nie zostali policzeni z nimi według pokolenia swych ojców.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 PAN rozkazał bowiem Mojżeszowi:
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 Tylko pokolenia Lewiego nie spisuj i nie licz go razem z synami Izraela;
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 Lecz ustanowisz Lewitów nad Przybytkiem Świadectwa i nad wszystkimi jego naczyniami, i nad wszystkim, co do niego należy. Oni będą nosić przybytek i wszystkie jego sprzęty; oni też będą go obsługiwać i rozbijać obóz dokoła przybytku.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 A gdy przybytek będzie miał wyruszyć, Lewici go rozbiorą; także gdy przybytek ma być wznoszony, Lewici ustawią go; a obcy, który się do niego zbliży, poniesie śmierć.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 I synowie Izraela będą rozbijać namioty, każdy w swoim obozie i każdy pod swoim sztandarem, według swych zastępów.
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 Lecz Lewici rozbiją obóz wokół Przybytku Świadectwa, aby gniew nie spadł na zgromadzenie synów Izraela. Lewici będą pełnić straż przy Przybytku Świadectwa.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 I synowie Izraela uczynili zgodnie ze wszystkim, co PAN rozkazał Mojżeszowi, tak właśnie uczynili.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.