< Micheasza 5 >
1 Zbierz się teraz w oddziały, córko oddziałów! Obległ nas. Laską będą bić w policzek sędziego Izraela.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 Ale ty, Betlejem Efrata, [choć] jesteś najmniejsze wśród tysięcy w Judzie, z ciebie [jednak] wyjdzie mi ten, który będzie władcą w Izraelu, a jego wyjścia [są] od dawna, od dni wiecznych.
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 Dlatego wyda ich aż do czasu, [kiedy] rodząca porodzi. Wtedy resztka jego braci wróci do synów Izraela.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 Powstanie i będzie paść w mocy PANA i w majestacie imienia PANA, swego Boga. I będą mieszkać [spokojnie], bo już będzie [on] wielki aż po krańce ziemi.
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 I będzie [on] pokojem, gdy Asyryjczyk wtargnie do naszej ziemi. I gdy podepcze nasze pałace, wtedy wystawimy przeciw niemu siedmiu pasterzy i ośmiu książąt z ludu.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 Ci ogołocą ziemię Asyrii mieczem i ziemię Nimroda na jej granicach. W ten sposób wybawi [nas] od Asyryjczyka, gdy nadciągnie do naszej ziemi i gdy będzie stąpał w naszych granicach.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 Dlatego resztka Jakuba będzie pośród wielu narodów jak rosa od PANA, jak deszcze skrapiające trawę, które nie czekają na człowieka ani nie polegają na synach ludzkich.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 Resztka Jakuba będzie też pośród pogan, wśród wielu narodów, jak lew między leśnymi zwierzętami i jak lwiątko między trzodami owiec, które – gdy przechodzi – depcze i szarpie, a nie ma nikogo, kto by [je] ocalił.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 Wywyższy się twoja ręka nad twoimi wrogami, a wszyscy twoi przeciwnicy będą wykorzenieni.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 I stanie się w tym dniu, mówi PAN, że wytracę twoje konie spośród ciebie i zniszczę twoje rydwany.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 Wygubię miasta twojej ziemi i zburzę wszystkie twoje twierdze.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 Wytracę czary z twojej ręki i nie będzie już u ciebie wróżbitów.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 Wyniszczę też twoje rzeźbione bożki i twoje obrazy spośród ciebie i nie będziesz już oddawać pokłonu dziełu swoich rąk.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 Wykorzenię twoje gaje spośród ciebie i zgładzę twoich wrogów.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 [Tak] w gniewie i zapalczywości dokonam zemsty nad narodami, które nie były posłuszne.
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”