< Łukasza 7 >

1 Gdy skończył [mówić] wszystkie te słowa w obecności ludzi, wszedł do Kafarnaum.
Yesu atamaliza kunena zonsezi pamaso pa anthu amene ankamvetsera, analowa mu Kaperenawo.
2 A sługa pewnego setnika, bardzo przez niego ceniony, chorował i był bliski śmierci.
Kumeneko wantchito wa Kenturiyo, amene amamukhulupirira kwambiri, anadwala ndipo anali pafupi kufa.
3 Kiedy [setnik] usłyszał o Jezusie, posłał do niego starszych spośród Żydów, prosząc, aby przyszedł i uzdrowił jego sługę.
Kenturiyo anamva za Yesu ndipo anatumiza ena a akulu Ayuda kwa Iye kuti abwere adzachiritse wantchito wakeyo.
4 A oni przyszli do Jezusa i prosili go usilnie: Godny jest, abyś mu to uczynił.
Iwo atafika kwa Yesu, anamudandaulira kwambiri, nati, “Munthuyu ayenera kuthandizidwa
5 Miłuje bowiem nasz naród i zbudował nam synagogę.
chifukwa amakonda mtundu wathu ndipo anatimangira sunagoge wathu.”
6 Wtedy Jezus poszedł z nimi. Ale gdy był [już] niedaleko domu, setnik posłał do niego przyjaciół ze słowami: Panie, nie trudź się, bo nie jestem godny, abyś wszedł pod mój dach.
Pamenepo Yesu anapita nawo. Iye sanali patali ndi nyumba pamene Kenturiyo anatumiza anzake kuti akamuwuze kuti, “Ambuye, musadzivutitse, pakuti ndine wosayenera kuti mulowe mʼnyumba mwanga.
7 Dlatego i samego siebie nie uważałem za godnego przyjść do ciebie. Lecz powiedz słowo, a mój sługa zostanie uzdrowiony.
Nʼchifukwa chake sindinadziyenereze ndi pangʼono pomwe kuti ndibwere kwa inu. Koma nenani mawu, ndipo wantchito wanga adzachira.
8 Bo i ja jestem człowiekiem podległym władzy i mam pod sobą żołnierzy, i mówię jednemu: Idź, a idzie, a drugiemu: Chodź tu, a przychodzi, a mojemu słudze: Zrób to, a robi.
Pakuti ndili pansi paulamuliro, ndiponso ndili ndi asilikali pansi panga. Ndikamuwuza uyu kuti, ‘Pita,’ iye amapita; ndi uyo kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikamuwuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ amachita.”
9 Gdy Jezus to usłyszał, zdziwił się i odwróciwszy się, powiedział do ludzi, którzy szli za nim: Mówię wam, nawet w Izraelu nie znalazłem tak wielkiej wiary.
Yesu atamva izi, anadabwa naye, ndipo anatembenukira gulu la anthu limene limamutsatira nati, “Ndikukuwuzani kuti, sindinapeze chikhulupiriro chachikulu ngati ichi mu Israeli.”
10 Ci zaś, którzy byli posłani, po powrocie do domu zastali zdrowym sługę, który chorował.
Kenaka anthu amene anatumidwawo anabwerera ku nyumba ndipo anakamupeza wantchitoyo atachira.
11 A nazajutrz udał się do miasta zwanego Nain. I szło z nim wielu jego uczniów i mnóstwo ludzi.
Zitangotha izi, Yesu anapita ku mudzi wa Naini ndipo ophunzira ake ndi gulu lalikulu la anthu linapita naye pamodzi.
12 A gdy zbliżył się do bramy miasta, właśnie wynoszono zmarłego, jedynego syna matki, która [była] wdową. Towarzyszyło jej mnóstwo ludzi z miasta.
Akufika pa chipata cha mudziwo, anakumana ndi anthu amene ankatuluka ndi munthu wakufa amene anali mwana yekhayo wa mkazi wamasiye. Gulu lalikulu la anthu a mʼmudziwo linali naye.
13 Kiedy Pan ją zobaczył, ulitował się nad nią i powiedział do niej: Nie płacz.
Ambuye atamuona mayiyo, mtima wawo unagwidwa naye chifundo ndipo anati, “Usalire.”
14 Potem podszedł i dotknął mar, a ci, którzy [je] nieśli, stanęli. I powiedział: Młodzieńcze, mówię ci, wstań!
Kenaka anapita nakakhudza chithatha cha maliro ndipo amene anachinyamulawo anayima. Iye anati, “Mnyamata, ndikukuwuza kuti, dzuka!”
15 A ten, który był martwy, usiadł i zaczął mówić. I oddał go jego matce.
Wakufayo anakhala tsonga ndi kuyamba kuyankhula, ndipo Yesu anamupereka mnyamatayo kwa amayi ake.
16 Wtedy wszystkich ogarnął strach i wielbili Boga, mówiąc: Wielki prorok powstał wśród nas, oraz: Bóg nawiedził swój lud.
Onse anachita mantha kwambiri nalemekeza Mulungu. Iwo anati, “Mneneri wamkulu waonekera pakati pathu. Mulungu wabwera kudzathandiza anthu ake.”
17 I rozeszła się ta wieść o nim po całej Judei i po całej okolicznej krainie.
Mbiriyi inafalikira ku Yudeya konse ndi ku madera ozungulira.
18 O tym wszystkim oznajmili Janowi jego uczniowie.
Ndipo ophunzira a Yohane anamuwuza Yohaneyo zinthu zonsezi. Atayitana awiri a ophunzirawo,
19 A [Jan], wezwawszy dwóch spośród swoich uczniów, posłał ich do Jezusa z zapytaniem: Czy ty jesteś tym, który ma przyjść, czy mamy oczekiwać innego?
anawatumiza kwa Ambuye kukafunsa kuti, “Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?”
20 A gdy ci mężczyźni przyszli do niego, powiedzieli: Jan Chrzciciel przysłał nas do ciebie z zapytaniem: Czy ty jesteś tym, który ma przyjść, czy mamy oczekiwać innego?
Anthuwo atafika kwa Yesu anati, “Yohane Mʼbatizi watituma kwa Inu kuti tidzafunse kuti, ‘Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?’”
21 A w tym właśnie czasie wielu uzdrowił z chorób i dolegliwości i [uwolnił] od złych duchów, a wielu ślepych obdarzył wzrokiem.
Pa nthawi yomweyo, Yesu anachiritsa ambiri amene ankavutika, odwala ndi amene anali mizimu yoyipa, ndiponso anapenyetsa anthu osaona.
22 Jezus więc odpowiedział im: Idźcie i oznajmijcie Janowi to, co widzieliście i słyszeliście: Ślepi widzą, chromi chodzą, trędowaci zostają oczyszczeni, głusi słyszą, umarli zmartwychwstają, a ubogim głoszona jest ewangelia.
Ndipo Iye anawayankha otumidwawo kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwaona ndi kumva: Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa, ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka.
23 A błogosławiony jest ten, kto się nie zgorszy z mojego powodu.
Odala munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”
24 Gdy zaś posłańcy Jana odeszli, zaczął mówić do ludzi o Janie: Co wyszliście zobaczyć na pustyni? Trzcinę kołyszącą się na wietrze?
Anthu otumidwa ndi Yohane aja atachoka, Yesu anayamba kuyankhula ndi gulu la anthu za Yohaneyo kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kukaona chiyani? Bango logwedezeka ndi mphepo?
25 Ale co wyszliście zobaczyć? Człowieka ubranego w miękkie szaty? Oto ci, którzy [noszą] kosztowne szaty i żyją w rozkoszach, są w domach królewskich.
Ngati si choncho, munkapita kukaona chiyani? Munthu wovala zovala zabwino? Ayi, ovala zovala zodula ndi okhala moyo wapamwamba ali mʼnyumba zaufumu.
26 Ale co wyszliście zobaczyć? Proroka? Tak, mówię wam, nawet więcej niż proroka.
Koma inu munkapita kukaona chiyani? Mneneri? Inde, Ine ndikukuwuzani, woposa mneneri.
27 On jest tym, o którym jest napisane: Oto posyłam mego posłańca przed twoim obliczem, który przygotuje twoją drogę przed tobą.
Uyu ndi amene malemba akunena za Iye kuti, “‘Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu.’
28 Mówię wam bowiem: Nie ma wśród narodzonych z kobiet większego proroka od Jana Chrzciciela. Lecz ten, kto jest najmniejszy w królestwie Bożym, jest większy niż on.
Ine ndikukuwuzani kuti pakati pa obadwa kuchokera mwa mkazi palibe wina wamkulu kuposa Yohane; komabe amene ali wamngʼono mu ufumu wa Mulungu ndi wamkulu kuposa iye.”
29 Słysząc to, wszyscy ludzie, jak również celnicy, przyznawali słuszność Bogu, będąc ochrzczeni chrztem Jana.
Anthu onse, ngakhale amisonkho, atamva mawu a Yesu, anavomereza kuti njira ya Mulungu ndi yolondola, chifukwa anabatizidwa ndi Yohane.
30 Ale faryzeusze i znawcy prawa odrzucili radę Boga sami przeciwko sobie, nie dając się przez niego ochrzcić.
Koma Afarisi ndi akatswiri amalamulo anakana cholinga cha Mulungu kwa iwo okha, chifukwa sanabatizidwe ndi Yohane.
31 I powiedział Pan: Do kogo więc przyrównam ludzi tego pokolenia? Do kogo są podobni?
“Kodi ndingawafanizire chiyani anthu a mʼbado uno? Ali ngati chiyani?
32 Podobni są do dzieci, które siedzą na rynku i wołają jedne na drugie: Graliśmy wam na flecie, a nie tańczyliście, śpiewaliśmy pieśni żałobne, a nie płakaliście.
Ali ngati ana amene akukangana pa msika, ena akufunsa anzawo kuti, “‘Ife tinakuyimbirani chitoliro, koma inu simunavine. Tinakuyimbirani nyimbo zamaliro, koma inu simunalire.’
33 Przyszedł bowiem Jan Chrzciciel, nie jadł chleba i nie pił wina, a mówicie: Ma demona.
Pakuti Yohane Mʼbatizi sanabwere kudzadya buledi kapena kumwa vinyo, koma inu mumati, ‘Ali ndi chiwanda.’
34 Przyszedł Syn Człowieczy, jedząc i pijąc, a mówicie: Oto żarłok i pijak, przyjaciel celników i grzeszników.
Mwana wa Munthu anabwera nadya ndi kumwa, ndipo inu mukuti, ‘Ali ndi dyera komanso ndi woledzera, bwenzi la amisonkho ndi ochimwa.’
35 Lecz usprawiedliwiona jest mądrość przez wszystkie swoje dzieci.
Ndipo nzeru zimaoneka zolondola mwa ana ake onse.”
36 I zaprosił go jeden z faryzeuszy na wspólny posiłek. Wszedł więc do domu faryzeusza i usiadł [przy stole].
Tsopano mmodzi mwa Afarisi anayitana Yesu kuti akadye naye ku nyumba kwake ndipo anapita nakakhala pa tebulo.
37 A oto kobieta, grzesznica, która była w [tym] mieście, dowiedziawszy się, że siedzi [przy stole] w domu faryzeusza, przyniosła alabastrowe naczynie olejku;
Mayi amene amakhala moyo wauchimo mu mzindawo atadziwa kuti Yesu akudya ku nyumba ya Mfarisiyo, anabweretsa botolo la mafuta onunkhira a alabasta.
38 I stanąwszy z tyłu u jego nóg, płacząc, zaczęła łzami obmywać jego nogi, wycierała je włosami swojej głowy, całowała i namaszczała olejkiem.
Iye anayimirira kumbuyo kwa Yesu pa mapazi ake akulira, nayamba kumadontheza misozi pa mapazi ake. Ndipo iye anapukuta mapaziwo ndi tsitsi lake, nawapsompsona ndi kuwathira mafuta onunkhirawo.
39 A widząc to, faryzeusz, który go zaprosił, pomyślał sobie: Gdyby on był prorokiem, wiedziałby, kim i jaka jest ta kobieta, która go dotyka. Jest bowiem grzesznicą.
Mfarisiyo anamuyitanayo ataona izi, anati mu mtima mwake, “Ngati munthuyu akanakhala mneneri, akanadziwa kuti akumukhudzayo ndi mayi otani, kuti ndi wochimwa.”
40 A Jezus odezwał się do niego: Szymonie, mam ci coś do powiedzenia. A on odrzekł: Powiedz, Nauczycielu.
Yesu anamuyankha iye kuti, “Simoni, ndili ndi kanthu koti ndikuwuze.” Iye anati, “Ndiwuzeni Aphunzitsi.”
41 Pewien wierzyciel miał dwóch dłużników. Jeden był winien pięćset groszy, a drugi pięćdziesiąt.
“Anthu awiri anakongola ndalama kwa munthu wina wokongoletsa ndalama: mmodzi ndalama zokwana 500 ndi winayo ndalama makumi asanu.
42 A gdy nie mieli z czego oddać, darował obydwóm. Powiedz więc, który z nich będzie go bardziej miłował?
Panalibe mmodzi mwa iwo anali ndi ndalama zobwezera, ndipo iye anawakhululukira ngongole zawo. Tsopano ndi ndani mwa awiriwa adzamukonde koposa?”
43 Szymon odpowiedział: Sądzę, że ten, któremu więcej darował. A on mu powiedział: Słusznie osądziłeś.
Simoni anayankha kuti, “Ndikuganiza kuti ndi amene anamukhululukira ngongole yayikulu.” Yesu anati, “Wayankha molondola.”
44 I odwróciwszy się do kobiety, powiedział do Szymona: Widzisz tę kobietę? Wszedłem do twego domu, a nie podałeś mi wody do nóg, ona zaś łzami obmyła moje nogi i otarła je swoimi włosami.
Kenaka anatembenukira kwa mayiyo nati kwa Simoni, “Ukumuona mayiyu? Ine ndabwera mʼnyumba yako. Iwe sunandipatse madzi otsukira mapazi anga, koma iyeyu wanyowetsa mapazi anga ndi misozi yake ndi kuwapukuta ndi tsitsi lake.
45 Nie pocałowałeś mnie, a ona, odkąd wszedłem, nie przestała całować moich nóg.
Iwe sunandipsompsone, koma mayiyu, kuyambira pamene Ine ndalowa, sanaleke kupsompsona mapazi anga.
46 Nie namaściłeś mi głowy oliwą, a ona olejkiem namaściła moje nogi.
Iwe sunadzoze mutu wanga mafuta, koma iye wadzoza mapazi anga mafuta onunkhira.
47 Dlatego mówię ci: Przebaczono jej wiele grzechów, gdyż bardzo umiłowała. A komu mało przebaczono, mało miłuje.
Tsono, ndikukuwuza iwe, machimo ake amene ndi ambiri akhululukidwa, monga chaonetsera chikondi chake chachikulu. Koma iye amene wakhululukidwa zochepa amakonda pangʼono.”
48 Do niej zaś powiedział: Twoje grzechy są przebaczone.
Kenaka anati kwa mayiyo, “Machimo ako akhululukidwa.”
49 Wtedy współbiesiadnicy zaczęli mówić między sobą: Kim jest ten, który i grzechy przebacza?
Alendo enawo anayamba kumanena mʼmitima mwawo kuti, “Uyu ndi ndani amene akhululukiranso machimo?”
50 I powiedział do kobiety: Twoja wiara cię zbawiła. Idź w pokoju.
Yesu anati kwa mayiyo, “Chikhulupiriro chako chakupulumutsa. Pita mu mtendere.”

< Łukasza 7 >