< Łukasza 16 >

1 Mówił też do swoich uczniów: Pewien bogaty człowiek miał szafarza, którego oskarżono przed nim, że trwoni jego dobra.
Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
2 Zawołał go i powiedział: Cóż to słyszę o tobie? Zdaj sprawę z twego zarządzania, bo już więcej nie będziesz mógł zarządzać.
Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
3 Wtedy szafarz powiedział sobie: Co ja zrobię, skoro mój pan pozbawia mnie zarządu? Kopać nie mogę, żebrać się wstydzę.
“Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
4 Wiem, co zrobię, żeby [ludzie] przyjęli mnie do swoich domów, gdy zostanę odsunięty od zarządzania.
Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
5 Przywołał więc do siebie każdego z dłużników swego pana i zapytał pierwszego: Ile jesteś winien memu panu?
“Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
6 A on odpowiedział: Sto baryłek oliwy. I powiedział mu: Weź swój zapis, siadaj szybko i napisz pięćdziesiąt.
“Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
7 Potem zapytał drugiego: A ty ile jesteś winien? A on mu odpowiedział: Sto korców pszenicy. I powiedział mu: Weź swój zapis i napisz osiemdziesiąt.
“Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
8 I pochwalił pan niesprawiedliwego szafarza, że roztropnie postąpił. Bo synowie tego świata w swoim pokoleniu są roztropniejsi od synów światłości. (aiōn g165)
“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
9 I ja wam mówię: Zyskujcie sobie przyjaciół mamoną niesprawiedliwości, aby, gdy ustaniecie, przyjęto was do wiecznych przybytków. (aiōnios g166)
Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
10 Kto jest wierny w najmniejszym, i w wielkim jest wierny, a kto w najmniejszym jest niesprawiedliwy, i w wielkim jest niesprawiedliwy.
“Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
11 Jeśli więc w niesprawiedliwej mamonie nie byliście wierni, któż wam powierzy to, co prawdziwe?
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
12 A jeśli w cudzym nie byliście wierni, któż wam da wasze [własne]?
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
13 Żaden sługa nie może dwom panom służyć, gdyż albo jednego będzie nienawidził, a drugiego miłował, albo jednego będzie się trzymał, a drugim wzgardzi. Nie możecie służyć Bogu i mamonie.
“Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
14 Słuchali tego wszystkiego również faryzeusze, którzy byli chciwi, i naśmiewali się z niego.
Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
15 I powiedział im: Wy sami siebie usprawiedliwiacie przed ludźmi, ale Bóg zna wasze serca. To bowiem, co ludzie poważają, obrzydliwością jest w oczach Boga.
Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
16 Prawo i Prorocy [byli] do Jana. Odtąd jest głoszone królestwo Boże i każdy się do niego gwałtem wdziera.
“Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
17 I łatwiej jest niebu i ziemi przeminąć, niż przepaść jednej kresce prawa.
Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
18 Każdy, kto oddala swoją żonę i żeni się z inną, cudzołoży, a kto żeni się z oddaloną przez męża, cudzołoży.
“Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
19 Był pewien bogaty człowiek, który ubierał się w purpurę i bisior i wystawnie ucztował każdego dnia.
“Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
20 Był też pewien żebrak, imieniem Łazarz, który leżał u jego wrót owrzodziały;
Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
21 Pragnął on nasycić się okruchami, które spadały ze stołu bogacza. Nadto i psy przychodziły i lizały jego wrzody.
ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
22 I umarł żebrak, i został zaniesiony przez aniołów na łono Abrahama. Umarł też bogacz i został pogrzebany.
“Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
23 A [będąc] w piekle i cierpiąc męki, podniósł oczy i ujrzał z daleka Abrahama i Łazarza na jego łonie. (Hadēs g86)
Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
24 Wtedy zawołał: Ojcze Abrahamie, zmiłuj się nade mną i poślij Łazarza, aby umoczył koniec swego palca w wodzie i ochłodził mi język, bo cierpię męki w tym płomieniu.
Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
25 I powiedział Abraham: Synu, wspomnij, że za życia odebrałeś swoje dobro, podobnie jak Łazarz zło. A teraz on doznaje pociechy, a ty cierpisz męki.
“Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
26 I oprócz tego wszystkiego między nami a wami jest utwierdzona wielka przepaść, aby ci, którzy chcą stąd przejść do was, nie mogli, ani stamtąd przejść do nas.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
27 A on powiedział: Proszę cię więc, ojcze, abyś posłał [go] do domu mego ojca.
“Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
28 Mam bowiem pięciu braci – niech im da świadectwo, żeby i oni nie przyszli na to miejsce męki.
pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
29 Lecz Abraham mu powiedział: Mają Mojżesza i Proroków, niech ich słuchają.
“Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
30 A on odpowiedział: Nie, ojcze Abrahamie, lecz jeśli ktoś z umarłych przyjdzie do nich, będą pokutować.
“Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
31 I powiedział do niego: Jeśli Mojżesza i Proroków nie słuchają, to choćby ktoś zmartwychwstał, nie uwierzą.
“Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”

< Łukasza 16 >