< Kapłańska 7 >

1 Takie jest prawo ofiary za przewinienie: jest to rzecz najświętsza.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 Na miejscu, gdzie zabijają ofiarę całopalną, zabiją ofiarę za przewinienie, a pokropią jej krwią z wierzchu dokoła ołtarz.
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 I [kapłan] złoży w ofierze cały jej tłuszcz, ogon i tłuszcz pokrywający wnętrzności;
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 Obie nerki z tłuszczem, który jest na nich i na lędźwiach, i płat tłuszczu na wątrobie, który oddzieli wraz z nerkami.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 I kapłan spali to na ołtarzu jako ofiarę ogniową dla PANA. To jest ofiara za przewinienie.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 Każdy mężczyzna spośród kapłanów będzie z niej jeść, będzie spożywana na miejscu świętym. Jest to rzecz najświętsza.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 Zarówno do ofiary za grzech, jak i do ofiary za przewinienie odnosi się jednakowe prawo: będą one [należeć] do tego kapłana, który dokonuje przebłagania.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Do kapłana, który składa czyjąś ofiarę całopalną, będzie [należeć] skóra tej ofiary, którą złożył.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 Także każda ofiara pokarmowa upieczona w piecu i wszystko, co przyrządzone w rondlu albo na patelni, będzie [należeć] do kapłana, który je składa.
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 Lecz każda ofiara pokarmowa zmieszana z oliwą albo sucha będzie należeć do wszystkich synów Aarona, do każdego w równej części.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 A takie jest prawo ofiary pojednawczej, którą będzie się składać PANU.
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 Jeśli [ktoś] składa ją jako ofiarę dziękczynną, złoży z ofiarą dziękczynną przaśne placki zmieszane z oliwą, przaśne podpłomyki pomazane oliwą i placki z mąki pszennej zmieszane z oliwą i smażone.
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 Oprócz tych placków złoży jako ofiarę chleb zakwaszony wraz z ofiarą dziękczynną ze swoich ofiar pojednawczych.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 I z niego będzie składał PANU po jednym [chlebie] z każdej ofiary jako ofiarę wzniesienia. Będzie to [należeć] do kapłana, który kropi krwią [ofiar] pojednawczych.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Mięso z dziękczynnej ofiary pojednawczej należy spożyć w dniu składania jego ofiary; nic z niego nie zostawią do rana.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 A jeśli jego ofiara jest darem ślubowanym lub dobrowolnym, należy ją spożyć w dniu jej złożenia; a to, co z niej zostanie, spożyją nazajutrz.
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 Lecz jeśli coś z mięsa tej ofiary zostanie do trzeciego dnia, będzie spalone w ogniu.
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 A jeśli ktoś zje mięso tej ofiary pojednawczej trzeciego dnia, nie zostanie przyjęta ani nie zostanie policzona temu, który ją złożył. Będzie to obrzydliwością, a kto ją spożyje, będzie obciążony nieprawością.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 Mięso, które dotknie czegoś nieczystego, nie będzie spożywane, ale zostanie spalone w ogniu. Inne mięso zaś może jeść każdy, kto jest czysty.
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 A ktokolwiek spożyje mięso z ofiary pojednawczej, która należy do PANA, będąc nieczysty, to taki człowiek zostanie wykluczony ze swego ludu.
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 A kto dotknie czegoś nieczystego: nieczystości ludzkiej [lub] nieczystego zwierzęcia lub jakiejkolwiek nieczystej obrzydliwości, a spożyje mięso z ofiary pojednawczej, która należy do PANA, to taki człowiek zostanie wykluczony ze swego ludu.
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 PAN powiedział jeszcze do Mojżesza:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 Powiedz synom Izraela: Nie będziecie jedli żadnego tłuszczu wołu, owcy ani kozy;
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Tłuszcz [zwierzęcia] padłego lub tłuszcz rozszarpanego może być używany do wszelkich celów, ale spożywać go nie wolno.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 Ktokolwiek bowiem spożyje tłuszcz zwierzęcia złożonego PANU jako ofiarę ogniową, ten zostanie wykluczony ze swego ludu.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Żadnej krwi nie będziecie jeść we wszystkich waszych mieszkaniach – ani z ptaków, ani ze zwierząt.
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 Każdy człowiek, który spożyje jakąkolwiek krew, zostanie wykluczony ze swego ludu.
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 PAN powiedział jeszcze do Mojżesza:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 Powiedz synom Izraela: Kto będzie składał PANU ofiarę pojednawczą, niech przyniesie PANU swoją ofiarę ze swoich ofiar pojednawczych.
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 Własnoręcznie przyniesie PANU ofiarę ogniową; przyniesie tłuszcz wraz z mostkiem, aby kołysać nim jako ofiarą kołysaną przed PANEM.
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 Potem kapłan spali tłuszcz na ołtarzu, a mostek będzie należał do Aarona i jego synów.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 A prawą łopatkę oddacie kapłanowi jako ofiarę wzniesienia z waszych ofiar pojednawczych.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 Kto spośród synów Aarona będzie składał krew ofiar pojednawczych i tłuszcz, weźmie jako swoją część prawą łopatkę.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 Gdyż mostek kołysania i łopatkę wzniesienia wziąłem od synów Izraela z ich ofiar pojednawczych i dałem je kapłanowi Aaronowi oraz jego synom od synów Izraela na mocy wiecznej ustawy.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 To jest część z ofiar ogniowych PANA [z powodu] namaszczenia Aarona i jego synów od dnia, kiedy przyprowadził ich, aby pełnili służbę kapłańską dla PANA;
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 O którym PAN rozkazał, aby im dawano od synów Izraela w dniu, w którym ich namaścił, na mocy wiecznej ustawy dla ich pokoleń.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 Takie jest prawo całopalenia, ofiary pokarmowej, ofiary za grzech, ofiary za przewinienie, ofiary poświęcenia i ofiary pojednawczej;
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 Które PAN nadał Mojżeszowi na górze Synaj w dniu, kiedy nakazał synom Izraela, aby składali swoje ofiary PANU na pustyni Synaj.
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.

< Kapłańska 7 >