< Księga Sędziów 8 >
1 I mężczyźni z Efraima powiedzieli do niego: Dlaczego tak z nami postąpiłeś, że nie wezwałeś nas, gdy wyruszyłeś do walki z Midianitami? I mocno się z nim spierali.
Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
2 A [on] powiedział: Cóż takiego uczyniłem w porównaniu z wami? Czyż nie lepszy jest ostatni zbiór winogron Efraima niż pierwszy zbiór Abiezera?
Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
3 Bóg wydał w wasze ręce książąt Midianu – Oreba i Zeeba. Cóż mogłem takiego uczynić w porównaniu z wami? Gdy to powiedział, ich duch uspokoił się wobec niego.
Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
4 A gdy Gedeon przybył do Jordanu, przeprawił się przez niego wraz z trzystoma mężczyznami, którzy z nim byli, znużonymi i w pościgu.
Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
5 I powiedział do mieszkańców Sukkot: Dajcie, proszę, po bochenku chleba ludowi, który idzie za mną, bo jest znużony, a ja ścigam Zebacha i Salmunnę, królów Midianu.
Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
6 Lecz książęta Sukkot odpowiedzieli mu: Czy dłonie Zebacha i Salmunny są już w twoich rękach, żebyśmy mieli dać twemu wojsku chleba?
Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
7 Gedeon odpowiedział: Kiedy PAN wyda Zebacha i Salmunnę w moje ręce, wtedy wymłócę wasze ciała cierniem pustyni i ostami.
Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
8 Potem wyruszył stamtąd do Penuel i mówił do nich podobnie, ale ludzie z Penuel odpowiedzieli mu [tak samo] jak odpowiedzieli mieszkańcy Sukkot.
Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
9 Powiedział więc też mężczyznom z Penuel: Gdy wrócę w pokoju, zburzę tę wieżę.
Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
10 A Zebach i Salmunna byli w Karkor, a z nimi ich wojsko w liczbie około piętnastu tysięcy, wszyscy, którzy pozostali z całego wojska ludzi ze wschodu; a poległo sto dwadzieścia tysięcy mężczyzn dobywających miecz.
Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
11 Wtedy Gedeon ciągnął drogą tych, którzy mieszkali w namiotach, na wschód od Nobach i Jogbeha, i uderzył na obóz, który czuł się bezpieczny.
Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
12 A gdy Zebach i Salmunna uciekli, ścigał ich i pojmał obu królów Midianu, Zebecha i Salmunnę, całe zaś wojsko rozgromił.
Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
13 Potem Gedeon, syn Joasza, wrócił z bitwy, zanim wzeszło słońce;
Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
14 I schwytał młodzieńca spośród mieszkańców Sukkot, i wypytał go, a ten spisał mu książąt Sukkot i jego starszych, siedemdziesięciu siedmiu mężczyzn.
Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
15 Wtedy przyszedł do mężczyzn Sukkot i powiedział: Oto Zebach i Salmunna, z powodu których mi urągaliście, mówiąc: Czy dłonie Zebacha i Salmunny są już w twoich rękach, abyśmy mieli dać chleba twoim znużonym mężczyznom?
Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
16 Wziął więc starszych tego miasta oraz ciernie z pustyni i osty i wysmagał nimi mężczyzn Sukkot.
Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
17 Zburzył także wieżę Penuel i zabił mężczyzn tego miasta.
Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
18 Potem powiedział do Zebacha i Salmunny: Co to byli za mężczyźni, których zabiliście w Tabor? A oni odpowiedzieli: Byli tacy jak ty; każdy z nich z wyglądu jak syn króla.
Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
19 I powiedział: [To byli] moi bracia, synowie mojej matki. Jak żyje PAN, gdybyście zachowali ich przy życiu, nie zabiłbym was.
Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
20 Potem powiedział do Jetera, swego pierworodnego: Wstań i zabij ich. Lecz młodzieniec nie dobył swego miecza, ponieważ bał się, gdyż był jeszcze chłopcem.
Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
21 Wtedy Zebach i Salmunna powiedzieli: Ty wstań i rzuć się na nas, jaki bowiem mężczyzna, taka jego siła. Wstał więc Gedeon, zabił Zebacha i Salmunnę i zabrał klejnoty, które były na szyjach ich wielbłądów.
Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
22 I powiedzieli Izraelici do Gedeona: Panuj nad nami, ty i twój syn, i syn twego syna. Wybawiłeś nas bowiem z rąk Midianitów.
Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
23 Lecz Gedeon odpowiedział im: Nie ja będę panował nad wami ani nie mój syn będzie panował nad wami. PAN będzie panował nad wami.
Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
24 Gedeon powiedział jeszcze do nich: Będę was prosił o jedną rzecz, aby każdy z was dał mi kolczyki ze swego łupu. Mieli bowiem złote kolczyki, bo byli Izmaelitami.
Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
25 I powiedzieli: Chętnie damy. Rozpostarli szatę i każdy rzucał na nią kolczyki ze swoich łupów.
Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
26 I waga [tych] złotych kolczyków, o które poprosił, wyniosła tysiąc siedemset syklów złota, nie licząc klejnotów i wisiorków, i szkarłatnych szat, które nosili królowie Midianu, i nie licząc łańcuchów, które były na szyjach ich wielbłądów.
Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
27 A Gedeon zrobił z tego efod i umieścił go w swoim mieście, w Ofra. Tam cały Izrael, chodząc za nim, uprawiał nierząd, a stało się to sidłem dla Gedeona i jego domu.
Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
28 Tak Midianici zostali poniżeni przed synami Izraela i nie podnieśli już swoich głów. A ziemia żyła w pokoju przez czterdzieści lat za dni Gedeona.
Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
29 Wrócił więc Jerubbaal, syn Joasza, i mieszkał w swoim domu.
Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
30 A Gedeon miał siedemdziesięciu synów, którzy wyszli z jego bioder. Miał bowiem wiele żon.
Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
31 Również jego nałożnica, która była w Sychem, urodziła mu syna i nadała mu imię Abimelek.
Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
32 Potem Gedeon, syn Joasza, umarł w szczęśliwej starości i został pogrzebany w grobie swego ojca Joasza, w Ofra Abiezerytów.
Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
33 A gdy Gedeon umarł, synowie Izraela odwrócili się i uprawiali nierząd, idąc za Baalami, i ustanowili sobie Baal-Berita swoim bogiem.
Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
34 I synowie Izraela nie pamiętali o PANU, swym Bogu, który ich wyrwał z rąk wszystkich okolicznych wrogów;
Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
35 I nie okazali miłosierdzia domowi Jerubbaala, Gedeona, za wszystkie dobrodziejstwa, jakie wyświadczył on Izraelowi.
Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.