< Księga Sędziów 16 >
1 Potem Samson poszedł do Gazy i gdy zobaczył tam nierządnicę, obcował z nią.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 I powiadomiono mieszkańców Gazy: Przybył tu Samson. Otoczyli go więc i czyhali na niego przez całą noc w bramie miasta. Zachowywali się cicho przez całą noc, mówiąc: Gdy zacznie świtać, zabijemy go.
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 Ale Samson spał do północy, a o północy wstał, chwycił wrota bramy miejskiej z dwoma słupami i wyrwał je z zasuwą, potem włożył na swoje ramiona i zaniósł je na szczyt góry, która była naprzeciw Hebronu.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 Potem w dolinie Sorek zakochał się w kobiecie, która miała na imię Dalila.
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 I przyszli do niej książęta Filistynów i powiedzieli jej: Oszukaj go i dowiedz się, w czym [tkwi] jego wielka siła i jak moglibyśmy go pokonać, by go związać i gnębić, a każdy z nas da ci tysiąc sto srebrników.
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 Powiedziała więc Dalila do Samsona: Powiedz mi, proszę, w czym tkwi twoja wielka siła i czym można by cię związać, by cię gnębić?
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 Samson jej odpowiedział: Gdyby mnie związano siedmioma świeżymi witkami, które jeszcze nie wyschły, wtedy osłabnę i będę jak każdy inny człowiek.
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 I książęta Filistynów przynieśli jej siedem świeżych witek, które jeszcze nie wyschły, i związała go nimi.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Tymczasem czyhający na niego siedzieli u niej w komorze. Wtedy powiedziała mu: Filistyni nad tobą, Samsonie! Lecz [on] zerwał witki, jakby ktoś zerwał zgrzebną nić, gdy dotknie jej ogień. Nie poznano więc, [w czym tkwiła] jego siła.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 Potem Dalila powiedziała do Samsona: Oszukałeś mnie i skłamałeś mi. Teraz powiedz mi, proszę, czym można by cię związać?
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 A on jej odpowiedział: Gdyby mnie związano nowymi powrozami, których [jeszcze] nie używano, wtedy osłabnę i będę jak każdy inny człowiek.
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 Dalila wzięła więc nowe powrozy i związała go nimi, i powiedziała do niego: Filistyni nad tobą, Samsonie! A czyhający na niego siedzieli w komorze, lecz [on] porwał je ze swych ramion jak nici.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 Wtedy Dalila powiedziała do Samsona: Aż dotąd szydziłeś ze mnie i okłamywałeś mnie. Powiedz mi, czym można by cię związać? I powiedział jej: Jeśli spleciesz siedem pasm z mojej głowy w osnowę przędzy.
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 Ona wtedy przybiła [je] kołkiem i powiedziała do niego: Filistyni nad tobą, Samsonie! Lecz [on] obudził się ze snu i wyrwał kołek z osnową i z wałkiem.
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Znowu powiedziała do niego: Jak możesz mówić: Kocham cię, skoro twoje serce nie jest ze mną. Już trzykrotnie mnie oszukałeś i nie powiedziałeś mi, w czym tkwi twoja wielka siła.
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 A gdy mu się tak naprzykrzała słowami każdego dnia i naciskała na niego tak, że jego dusza zmęczyła się na śmierć;
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 Wtedy otworzył przed nią całe swoje serce i powiedział jej: Brzytwa nigdy nie dotknęła mojej głowy, bo jestem nazirejczykiem dla Boga [już] z łona mojej matki. Jeśli zostanę ogolony, odejdzie ode mnie moja siła, osłabnę i będę jak każdy inny człowiek.
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 A gdy Dalila spostrzegła, że otworzył przed nią całe swoje serce, wezwała książąt Filistynów, mówiąc: Przyjdźcie raz [jeszcze], gdyż otworzył przede mną całe swoje serce. Przyszli więc do niej książęta Filistynów, niosąc srebro w rękach.
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 Wtedy uśpiła go na swoich kolanach, przywołała [pewnego] człowieka i kazała zgolić siedem pasm jego głowy; potem zaczęła go gnębić, a jego siła odeszła od niego.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 I powiedziała: Filistyni nad tobą, Samsonie! A gdy się obudził ze snu, powiedział: Wyjdę jak poprzednio i otrząsnę się. Lecz nie wiedział, że PAN odstąpił od niego.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 Wtedy Filistyni pojmali go, wyłupili mu oczy i zaprowadzili do Gazy, a tam związali go dwoma spiżowymi łańcuchami i musiał mleć w domu więźniów.
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 Potem włosy na jego głowie zaczęły odrastać po ogoleniu.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 A książęta Filistynów zebrali się, aby złożyć swemu bogu Dagonowi wielką ofiarę i radować się. Mówili bowiem: Nasz bóg wydał w nasze ręce Samsona, naszego wroga.
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 Kiedy ludzie widzieli go, chwalili swego boga, bo mówili: Nasz bóg wydał w nasze ręce naszego wroga, tego, który pustoszył naszą ziemię i który wielu z naszych pozabijał.
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 A gdy ich serca się rozweseliły, powiedzieli: Zawołajcie Samsona, aby nas zabawiał. Przywołano więc Samsona z domu więźniów, aby ich zabawiał. I postawili go między dwiema kolumnami.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 Wtedy Samson powiedział do chłopca, który go trzymał za rękę: Poprowadź mnie, abym mógł dotknąć kolumn, na których stoi dom, abym się o nie oparł.
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 A dom był pełen mężczyzn i kobiet, [byli] tam wszyscy książęta Filistynów, na dachu zaś [było] około trzech tysięcy mężczyzn i kobiet, którzy się przyglądali, gdy Samson [ich] zabawiał.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 Wówczas Samson wezwał PANA i powiedział: Panie BOŻE, wspomnij na mnie, proszę, i wzmocnij mnie tylko ten jeden raz, Boże, abym mógł się zemścić już na Filistynach za dwoje moich oczu.
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 Ujął więc Samson obie środkowe kolumny, na których stał dom i o które się wsparł, jedną swoją prawą ręką, a drugą swoją lewą ręką.
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 Potem Samson powiedział: Niech umrę z Filistynami. A gdy się o nie mocno oparł, dom upadł na książąt i na cały lud, który w nim był. A martwych, których zabił przy swojej śmierci, było więcej niż tych, których zabił za swego życia.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 I przyszli jego bracia i cały dom jego ojca, wzięli go, wrócili i pogrzebali go między Sorea a Esztaol, w grobie Manoacha, jego ojca. A sądził on Izraela przez dwadzieścia lat.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.