< Jozuego 6 >
1 A Jerycho było szczelnie zamknięte z powodu synów Izraela. Nikt z niego nie wychodził i nikt do niego nie wchodził.
Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
2 Wtedy PAN powiedział do Jozuego: Oto dałem w twoje ręce Jerycho, jego króla i [jego] dzielnych wojowników.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
3 I wy, wszyscy wojownicy, będziecie obchodzić miasto, okrążając je raz. Uczynicie tak przez sześć dni.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
4 A siedmiu kapłanów będzie niosło przed arką siedem trąb [z rogów] baranich. Siódmego zaś dnia obejdziecie miasto siedem razy, a kapłani będą dąć w trąby.
Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
5 A gdy przeciągle będą [trąbić] w baranie rogi i usłyszycie głos trąby, cały lud wzniesie wielki okrzyk, a mury miasta runą i lud wejdzie [do miasta], każdy wprost przed siebie.
Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
6 Wtedy Jozue, syn Nuna, wezwał kapłanów i powiedział im: Weźcie arkę przymierza i niech siedmiu kapłanów niesie siedem trąb z baranich [rogów] przed arką PANA.
Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
7 Potem powiedział do ludu: Idźcie i obejdźcie miasto, a uzbrojeni wojownicy niech idą przed arką PANA.
Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
8 A gdy Jozue powiedział [to] ludowi, siedmiu kapłanów niosących siedem trąb [z] baranich [rogów] wyruszyło przed arką PANA i dęli w trąby. A arka przymierza PANA szła za nimi.
Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
9 Uzbrojeni wojownicy zaś szli przed kapłanami, którzy dęli w trąby, a pozostałe oddziały szły za arką. Gdy szli, dęto w trąby.
Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
10 A Jozue nakazał ludowi: Nie krzyczcie, niech nie będzie słychać waszego głosu ani niech żadne słowo nie wyjdzie z waszych ust aż do dnia, w którym wam powiem: Wznieście okrzyk! Wtedy wydacie okrzyk.
Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
11 Tak więc arka PANA okrążyła miasto raz, po czym wrócili do obozu i przenocowali w nim.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
12 Jozue wstał wcześnie rano, a kapłani wzięli arkę PANA.
Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
13 A siedmiu kapłanów niosących siedem trąb z [rogów] baranich szło nieprzerwanie przed arką PANA, dmąc w trąby. Uzbrojeni wojownicy szli przed nimi, a pozostałe oddziały szły za arką PANA. Gdy szli, dęto w trąby.
Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
14 Na drugi dzień okrążyli miasto raz i wrócili do obozu. Tak czynili przez sześć dni.
Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
15 Lecz dnia siódmego wstali rano o świcie i okrążyli miasto w ten sam sposób siedem razy. Tylko tego dnia okrążyli miasto siedem razy.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
16 A za siódmym razem, gdy kapłani zadęli w trąby, Jozue powiedział do ludu: Wznieście [teraz] okrzyk, bo PAN wydaje wam miasto.
Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
17 I miasto będzie przeklęte dla PANA, ono samo i wszystko, co się w nim znajduje. Tylko nierządnica Rachab zostanie przy życiu, ona i wszyscy, którzy są z nią w domu, gdyż ukryła posłańców, których wysłaliśmy.
Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
18 Wy jednak strzeżcie się tego, co przeklęte, abyście sami nie stali się przekleństwem, gdy weźmiecie z obłożonego przekleństwem, i byście nie ściągnęli przekleństwa na obóz Izraela, i nie sprowadzili na niego nieszczęścia.
Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
19 Wszelkie srebro i złoto oraz przedmioty miedziane i żelazne będą poświęcone PANU. Zostaną złożone do skarbca PANA.
Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
20 Wtedy lud wydał okrzyk, gdy zadęto w trąby. A kiedy lud usłyszał dźwięk trąb i wydał potężny okrzyk, runęły mury, a lud wszedł do miasta, każdy prosto przed siebie, i zdobyli miasto;
Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
21 I zniszczyli ostrzem miecza wszystko, co było w mieście: mężczyzn i kobiety, dzieci i starców, woły, owce i osły.
Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
22 Lecz dwóm mężczyznom, którzy wybadali tę ziemię, Jozue powiedział: Wejdźcie do domu nierządnicy i wyprowadźcie stamtąd tę kobietę oraz wszystko, co do niej należy, tak jak jej przysięgliście.
Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
23 Weszli więc młodzieńcy, zwiadowcy, i wyprowadzili Rachab, jej ojca, jej matkę i jej braci oraz wszystko, co do niej [należało]. Wyprowadzili całą jej rodzinę i zostawili ich poza obozem Izraela.
Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
24 A miasto i wszystko, co w nim było, spalili ogniem. Tylko srebro i złoto oraz przedmioty miedziane i żelazne złożyli do skarbca domu PANA.
Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
25 Jozue zostawił przy życiu nierządnicę Rachab, dom jej ojca i wszystko, co do niej należało; mieszka ona w Izraelu aż do dziś, ponieważ ukryła posłańców, których Jozue wysłał na wybadanie Jerycha.
Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
26 W tym czasie Jozue złożył przysięgę: Niech będzie przeklęty przed PANEM człowiek, który powstanie i odbuduje to miasto, Jerycho. Na swoim pierworodnym założy jego fundament, a na swoim najmłodszym postawi jego bramy.
Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
27 I PAN był z Jozuem, którego sława rozchodziła się po całej ziemi.
Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.