< Jozuego 17 >
1 Los przypadł też pokoleniu Manassesa, bo był on pierworodnym Józefa. [Przypadł] Makirowi, pierworodnemu Manassesa, ojcu Gileada, a ponieważ był wojownikiem, otrzymał Gilead i Baszan.
Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
2 [Dział] otrzymali też inni synowie Manassesa według ich rodzin: synowie Abiezera, synowie Cheleka, synowie Asriela, synowie Sychema, synowie Chefera i synowie Szemidy. Ci byli synami Manassesa, syna Józefa – mężczyźni według ich rodzin.
Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
3 Lecz Selofchad, syn Chefera, syna Gileada, syna Makira, syna Manassesa, nie miał synów, tylko córki. Oto imiona jego córek: Machla, Noa, Chogla, Milka i Tirsa.
Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
4 Przyszły one przed kapłana Eleazara, przed Jozuego, syna Nuna, oraz przed naczelników i powiedziały: PAN rozkazał Mojżeszowi, aby dał nam dziedzictwo pośród naszych braci; i [Jozue] dał im zgodnie z rozkazem PANA dziedzictwo pośród braci ich ojca.
Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
5 I przypadło Manassesowi dziesięć działów oprócz ziemi Gilead i Baszan, które były za Jordanem.
Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
6 Córki Manassesa otrzymały bowiem dziedzictwo pośród jego synów, a ziemia Gilead przypadła pozostałym synom Manassesa.
chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 I granica Manassesa ciągnęła się od Aszera do Michmetat, które leży naprzeciw Szechem, a dalej biegła na prawo do mieszkańców w En-Tappuach.
Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
8 Ziemia Tappuach należała do Manassesa, ale Tappuach na granicy Manassesa należało do synów Efraima.
(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
9 Granica ta biegła do potoku Kana, na południe od tego potoku. Te miasta Efraimitów [leżą] wśród miast Manassesa, ale granica Manassesa biegła od północy tego potoku, a kończyła się przy morzu.
Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
10 Na południu [był dział] Efraima, a na północy Manassesa, a jego granicą było morze. Z Aszerem graniczy na północy, a z Issacharem na wschodzie.
Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 I Manasses [posiadał] w działach Issachara i Aszera Bet-Szean i przyległe do niego miasteczka, Jibleam i przyległe do niego miasteczka, mieszkańców Dor i przyległe do niego miasteczka, mieszkańców Endor i przyległe do niego miasteczka, mieszkańców Tanaku i przyległe do niego miasteczka oraz mieszkańców Megiddo i przyległe do niego miasteczka – trzy okręgi.
Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
12 Lecz synowie Manassesa nie mogli wypędzić z tych miast [ich mieszkańców], dlatego Kananejczycy dalej mieszkali w tej ziemi.
Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
13 A gdy synowie Izraela wzmocnili się, kazali Kananejczykom płacić daninę, ale nie wypędzili ich całkowicie.
Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
14 Wtedy synowie Józefa powiedzieli do Jozuego: Dlaczego dałeś nam w dziedzictwo jeden los i jeden dział? Jesteśmy przecież ludem wielkim i PAN dotychczas nam błogosławił.
Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
15 I Jozue odpowiedział im: Jeśli jesteście ludem wielkim, idźcie do lasu i wykarczujcie tam sobie miejsce w ziemi Peryzzytów i Refaitów, skoro za ciasno jest wam na górze Efraim.
Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
16 Synowie Józefa odpowiedzieli: Góra nam nie wystarczy, a wszyscy Kananejczycy, którzy mieszkają w dolinach, mają żelazne rydwany, zarówno ci, którzy mieszkają w Bet-Szean i w przyległych do niego miasteczkach, jak i ci, [którzy mieszkają] w dolinie Jizreel.
Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
17 Wtedy Jozue powiedział do domu Józefa, do Efraima i Manassesa: Jesteś ludem wielkim i twoja moc jest wielka, nie będziesz miał [tylko] jednego losu;
Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
18 Lecz otrzymasz górę; a że tam [jest] las, to go wykarczujesz i będziesz miał jego granice. Wypędzisz bowiem Kananejczyków, choć mają żelazne rydwany [i] są potężni.
dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”