< Hioba 9 >
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 Doprawdy, wiem, że tak [jest]. Lecz jak człowiek miałby być usprawiedliwiony przed Bogiem?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Gdyby chciał się z nim spierać, nie odpowie mu ani raz na tysiąc.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Ma on mądre serce i potężną siłę. Kto mu się sprzeciwił i powodziło mu się?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 On przenosi góry, a [ludzie] nie zauważają, przewraca je w swoim gniewie.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 On wstrząsa ziemią z jej miejsca i trzęsą się jej filary.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 On rozkaże słońcu i ono nie wschodzi, zamyka też gwiazdy pieczęcią.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 On sam rozciąga niebiosa i kroczy po falach morza.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 On stworzył Niedźwiedzicę, Oriona, Plejady i gwiazdozbiory południa.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 On czyni rzeczy wielkie i niezbadane, cuda, których zliczyć nie można.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Oto przechodzi obok mnie, a nie widzę go; mija mnie, a ja go nie dostrzegam.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Oto gdy zabiera, któż go powstrzyma? Któż mu powie: Co czynisz?
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Gdyby Bóg nie odwrócił swego gniewu, zuchwali pomocnicy upadliby pod nim.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 Jakże ja mu odpowiem? [Jakie] słowa wybiorę, aby się z nim spierać?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Choćbym był sprawiedliwy, nie odpowiedziałbym mu, lecz błagałbym swojego sędziego.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Choćbym go wzywał, a on by się odezwał, jeszcze nie uwierzyłbym, że mnie wysłuchał;
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Kruszy mnie bowiem burzą i pomnaża moje rany bez powodu.
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 Nie pozwala mi odetchnąć, raczej napełnia mnie goryczą.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Jeśli [chodzi] o siłę, oto jest potężny, a jeśli chodzi o sąd, któż mnie przed nim przyprowadzi?
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Jeśli się usprawiedliwię, moje usta mnie potępią. Jeśli powiem, że jestem doskonały, to one wykażą, że jestem przewrotny.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 Choćbym był doskonały, przecież nie znałbym swojej duszy; gardziłbym swoim życiem.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Jedno jest [pewne], dlatego powiedziałem: On niszczy [zarówno] doskonałego, [jak] i niegodziwego;
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Jeśli bicz nagle zabija, śmieje się on z doświadczenia niewinnych.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 Ziemia została wydana w ręce niegodziwego. On zakrywa oblicze sędziów. A jeśli nie on, któż [to czyni]?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 Ale moje dni są szybsze niż goniec, uciekły i nie widziały nic dobrego.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 Przeminęły jak szybkie łodzie, jak orzeł, który rzuca się na żer.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Jeśli powiem: Zapomnę o swojej skardze, zaniecham swego gniewu i pocieszę się;
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 Wtedy przerażają mnie wszystkie moje cierpienia, bo wiem, że nie uznasz mnie za niewinnego.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Jeśli jestem niegodziwy, to czemu trudzę się na próżno?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 Choćbym się umył wodą ze śniegu i oczyścił mydłem swoje ręce;
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Ty i tak zanurzysz mnie w dole i moje szaty będą się mną brzydzić.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 On bowiem nie jest człowiekiem jak ja, abym śmiał mu odpowiedzieć i abyśmy razem stanęli przed sądem.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Nie ma między nami rozjemcy, który mógłby położyć rękę na nas obu.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Niech tylko zdejmie ze mnie swoją rózgę, a jego groza niech mnie już nie przeraża;
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Wtedy będę mówił i nie będę się go bać; ale tak nie jest ze mną.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.