< Hioba 42 >
1 Wtedy Hiob odpowiedział PANU:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
2 Wiem, że ty wszystko możesz i że żaden twój zamysł nie może być powstrzymany.
“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
3 Kim jest ten, który zaciemnia radę bez wiedzy? Właśnie dlatego mówiłem to, czego nie rozumiałem; mówiłem o rzeczach zbyt cudownych, których nie mogłem pojąć.
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
4 Wysłuchaj, proszę, a będę mówił; będę cię pytał, a ty mnie pouczysz.
“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
5 [Dotąd] tylko [moje] ucho słyszało o tobie, lecz teraz moje oko cię ujrzało.
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
6 Dlatego żałuję i pokutuję w prochu i popiele.
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
7 A gdy PAN wypowiedział te słowa do Hioba, powiedział PAN do Elifaza z Temanu: Mój gniew zapłonął przeciw tobie i przeciw dwom twoim przyjaciołom, ponieważ nie mówiliście o mnie prawdy jak mój sługa Hiob.
Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
8 Teraz więc weźcie sobie siedem cielców i siedem baranów, idźcie do mego sługi Hioba i złóżcie całopalenie za siebie; a Hiob, mój sługa, będzie się modlił za was, bo jego przyjmę, abym nie uczynił z wami według waszej głupoty. Nie mówiliście bowiem o mnie prawdy jak mój sługa Hiob.
Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
9 Poszli więc Elifaz z Temanu, Bildad z Szuach i Sofar z Naamy i uczynili, jak PAN im rozkazał. PAN także przyjął Hioba.
Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
10 PAN przywrócił to, co zostało zabrane Hiobowi, gdy się modlił za swoich przyjaciół. PAN także pomnożył Hiobowi w dwójnasób wszystko, co miał.
Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
11 Wtedy zeszli się do niego wszyscy jego bracia, wszystkie jego siostry i wszyscy dawni znajomi i jedli z nim chleb w jego domu. Ubolewali nad nim i pocieszali go z powodu wszystkich nieszczęść, które PAN sprowadził na niego. Każdy dał mu po jednym srebrniku i każdy po jednym złotym kolczyku.
Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
12 I tak PAN błogosławił ostatnie [lata] Hioba bardziej niż początkowe. Miał bowiem czternaście tysięcy owiec, sześć tysięcy wielbłądów, tysiąc jarzm wołów i tysiąc oślic.
Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
13 Miał też siedmiu synów i trzy córki.
Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
14 I nadał pierwszej imię Jemima, drugiej Kecja i trzeciej Kerenhappuk.
Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
15 W całej ziemi nie można było znaleźć kobiet tak pięknych jak córki Hioba. Ich ojciec dał im dziedzictwo wśród ich braci.
Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
16 Potem Hiob żył jeszcze sto czterdzieści lat i oglądał swoich synów i synów swoich synów aż do czwartego pokolenia.
Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
17 I umarł Hiob stary i syty dni.
Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.