< Hioba 26 >
1 A Hiob tak odpowiedział:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Jakże uratowałeś tego, który nie ma mocy? Jakże wybawiłeś ramię, które nie ma siły?
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 Jakże doradziłeś temu, który nie ma mądrości? Jakże dokładnie nauczyłeś tej sprawy?
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 Komu powiedziałeś te słowa? Czyj to duch wyszedł od ciebie?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 Rzeczy martwe rodzą się pod wodami oraz ich mieszkańcy.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 Piekło jest odkryte przed nim i zatracenie nie ma przykrycia. (Sheol )
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
7 Rozciągnął północ nad pustym miejscem [i] ziemię zawiesił na niczym.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 Zawiązuje wody w swoich obłokach, a obłok nie pęka pod nimi.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Zatrzymuje widok swego tronu, rozciąga nad nim swój obłok.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Wodom nakreślił granice, aż nastąpi koniec światłości i ciemności.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Filary niebios trzęsą się i zdumiewają się jego gromem.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 Swoją mocą dzieli morze, a swoją roztropnością uśmierza jego nawałnicę.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 Swoim duchem przyozdobił niebiosa, a jego ręka stworzyła pokrzywionego węża.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Oto tylko cząstka jego dróg, ale jakże mało o nim słyszymy! A kto pojmie grzmot jego wielkiej potęgi?
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”