< Hioba 24 >
1 Czemu, [skoro] od Wszechmocnego nie są zakryte czasy, ci, którzy go znają, nie widzą jego dni?
“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
2 [Niektórzy] przesuwają granice, zabierają trzody i pasą je.
Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
3 Osła sierot pędzą i wołu wdowy biorą w zastaw.
Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
4 Spychają z drogi ubogich, biedni ziemi [muszą] się kryć razem.
Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
5 Oto jak dzikie osły na pustyni wychodzą oni do swojej pracy, wstając rano na łup. Pustynia [wydaje] chleb dla nich oraz ich dzieci.
Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
6 Na polu żną zboże i zbierają [grona] w winnicy niegodziwych.
Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
7 Nagich zmuszają nocować bez ubrania, tak że nie mają czym się nakryć w czasie chłodów;
Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
8 Przemoczeni ulewą górską, bez schronienia przytulają się do skały.
Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
9 Odrywają od piersi sieroty, od ubogiego biorą zastaw.
Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
10 Nagiego zmuszają do chodzenia bez ubrania, a głodnym zabierają snopy.
Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
11 [A ci, którzy] pośród ich murów wyciskają oliwę i tłoczą w prasach, są spragnieni.
Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
12 Ludzie w mieście wzdychają, dusze śmiertelnie rannych wołają, a Bóg im w tym nie przeszkadza.
Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
13 To są ci, którzy się sprzeciwiają światłości, nie znają jej dróg ani nie trwają na jej ścieżkach.
“Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
14 Morderca wstaje przed świtem i zabija ubogiego i potrzebującego, a w nocy jest jak złodziej.
Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
15 Oko cudzołożnika czeka na zmierzch, mówiąc: Nikt mnie nie zobaczy, i zakrywa on [swoje] oblicze.
Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
16 W ciemności podkopują domy, które sobie za dnia oznaczyli, nie znają światła.
Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
17 Dla nich bowiem poranek jest jak cień śmierci. Jeśli ktoś ich rozpozna, ogarnia ich strach cienia śmierci.
Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
18 Lekko unoszą się na wodach, przeklęty jest ich dział na ziemi, nie patrzą na drogę [do] winnic.
“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
19 [Jak] susza i upał trawią wody śniegu, [tak] grób [trawi] grzeszników. (Sheol )
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol )
20 Zapomni o nim łono [jego] matki, a robak będzie się nim karmić jak słodycz; nikt go więcej nie wspomni, a nieprawość zostanie połamana jak drzewo.
Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
21 Dręczy niepłodną, która nie rodziła, a wdowie nie czyni dobra.
Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
22 Pociąga też mocarzy swoją siłą; [gdy] powstaje, nikt nie jest pewien swego życia.
Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
23 Dano mu, że może oprzeć się bezpiecznie; jego oczy jednak [patrzą] na ich drogi.
Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
24 Na chwilę zostali wywyższeni, ale już [ich] nie ma; zostali poniżeni [i] ściśnieni jak wszyscy inni, a jak wierzch kłosa zostaną wycięci.
Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
25 A jeśli tak nie jest, kto mi udowodni kłamstwo i obróci wniwecz moje słowa?
“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”