< Hioba 23 >
1 Wtedy Hiob odpowiedział:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Również dziś moja skarga jest gorzka, [choć] moje nieszczęście jest cięższe niż moje jęki.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 O gdybym wiedział, gdzie mógłbym go znaleźć, udałbym się aż do jego tronu.
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 Przedstawiłbym mu [swoją] sprawę, a moje usta napełniłbym dowodami;
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 Poznałbym słowa jego odpowiedzi i zrozumiałbym, co chce mi powiedzieć.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Czy w swojej wielkiej mocy będzie się spierał ze mną? Nie, raczej sam doda mi [siły].
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 Tam człowiek prawy rozprawiałby z nim, a ja na zawsze byłbym wolny od mojego sędziego.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 [Ale] oto idę prosto, a jego nie ma; cofam się, a nie dostrzegam go.
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 [Idę] w lewo, gdzie on działa, a nie oglądam go; idę na prawo, a nie widzę go.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 Gdyż on zna drogę, którą kroczę; kiedy mnie doświadczy, wyjdę jak złoto.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 Moja noga trzymała się jego śladu, przestrzegałem jego drogi i nie zbaczałem [z niej].
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 Od przykazania jego ust nie odchodziłem; ceniłem słowa jego ust bardziej niż mój własny [pokarm].
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 Lecz on jest [niezmienny], któż go odwróci? Czego bowiem jego dusza zapragnie, to uczyni;
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 Bo on wykona, co postanowił o mnie; u niego jest wiele takich [przykładów].
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Dlatego drżę przed jego obliczem; gdy to rozważam, lękam się go.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Bóg osłabił moje serce, Wszechmocny mnie zatrwożył.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 O mało bowiem nie zginąłem od ciemności, [nie] zakrył mroku przed moim obliczem.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.