< Hioba 15 >

1 Wtedy Elifaz z Temanu odpowiedział:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Czy mądry [człowiek] ma odpowiadać próżną wiedzą i napełniać swoje wnętrze wiatrem wschodnim?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Czy ma się spierać słowami bezużytecznymi i mową, która nie przynosi pożytku?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Ty nawet odrzucasz bojaźń i powstrzymujesz modlitwę przed Bogiem.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Twoje usta bowiem pokazują twą nieprawość, posługujesz się mową przebiegłych.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Twoje usta cię potępiają, a nie ja; twoje wargi świadczą przeciwko tobie.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Czy jesteś pierwszym człowiekiem, który się urodził? Czy zostałeś stworzony przed pagórkami?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Czy słuchałeś tajemnic Boga? Czy tylko w tobie jest mądrość?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Cóż ty wiesz, czego my nie wiemy? Cóż ty rozumiesz, czego my nie rozumiemy?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Wśród nas są i sędziwi, i starcy, starsi od twego ojca.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Czy lekceważysz pociechę Boga? Czy masz w sobie coś tajemnego?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Czemu cię tak uniosło twoje serce? Czemu swoimi oczami tak mrugasz;
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Że zwracasz przeciwko Bogu swego ducha i wypuszczasz ze swoich ust takie słowa?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Czym jest człowiek, aby miał być czysty, urodzony z kobiety, aby miał być sprawiedliwy?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Oto nawet swoim świętym on nie ufa i niebiosa nie są czyste w jego oczach.
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Tym bardziej obrzydły i nikczemny jest człowiek, [który] pije nieprawość jak wodę.
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Wykażę ci, [tylko] mnie posłuchaj; opowiem ci, co widziałem;
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Co mądrzy powiedzieli, a nie zataili, [co mieli] od przodków swoich;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 Im samym dana była ziemia i żaden obcy nie przeszedł wśród nich.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Niegodziwy żyje w udręce przez wszystkie [swoje] dni i niewiele lat wyznaczono ciemięzcy.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Głos przerażenia [brzmi] w jego uszach, że w czasie pokoju napadnie go niszczyciel.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Nie wierzy, że miałby wrócić z ciemności, obawia się [zewsząd] miecza.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Tuła się za chlebem, [pytając], gdzie [go znaleźć]. Wie, że dzień ciemności został dla niego przygotowany.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Przeraża go utrapienie i ucisk; wzmocnią się przeciwko niemu jak król gotowy do boju.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Wyciągnął bowiem swą rękę przeciw Bogu, przeciwko Wszechmocnemu się umocnił.
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Naciera na niego, na [jego] szyję, [która jest okryta] pod gęstymi grzbietami jego tarcz.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Swoją twarz kryje bowiem w tłuszczu, a jego tusza zaokrągliła się na lędźwiach.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 Mieszka w opustoszałych miastach i domach, w których nikt nie przebywa, które niebawem staną się ruiną.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Nie wzbogaci się i nie przetrwa jego majątek ani jego doskonałość nie rozszerzy się na ziemi.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Nie wyjdzie z ciemności, płomień ususzy jego latorośle, a zginie od tchnienia jego ust.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Niech złudzony nie ufa marności, gdyż marność będzie jego zapłatą.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Przed wypełnieniem jego dni nastąpi, a jego gałązka nie zakwitnie.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Jak winna latorośl utraci swoje niedojrzałe grona, jak oliwka zrzuci swój kwiat.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Zgromadzenie obłudników będzie bowiem spustoszone, a ogień strawi namioty przekupstwa.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Poczęli krzywdę i urodzili nieprawość, a ich łono przygotowuje oszustwo.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Hioba 15 >