< Jeremiasza 9 >

1 Oby moja głowa była wodą, a moje oczy źródłem łez, abym dniem i nocą opłakiwał pomordowanych córki mego ludu!
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Obym miał na pustyni schronisko dla podróżnych, abym mógł opuścić swój lud i oddalić się od nich! Wszyscy bowiem są cudzołożnikami, zgrają zdrajców;
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 I [jak] łuk napinają swój język do kłamstwa. Nie wzmocnili się prawdą na ziemi, bo od zła do zła przechodzą, a mnie nie znają, mówi PAN.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Niech się każdy strzeże swego bliźniego, a bratu nie ufa, bo każdy brat oszukuje podstępnie i każdy bliźni postępuje jak oszczerca.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 Każdy też oszukuje swego bliźniego i nie mówi prawdy. Przyuczyli swój język do mówienia kłamstwa, męczą się, aby popełnić nieprawość.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Twoje mieszkanie jest pośród ludu podstępnego; z powodu podstępu nie chcą mnie poznać, mówi PAN.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 Dlatego tak mówi PAN zastępów: Oto przetopię ich i wypróbuję; jak bowiem mam postąpić z córką mego ludu?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 Ich język [jest] śmiercionośną strzałą, wypowiada oszustwa. [Jeden] mówi ustami o pokoju ze swym przyjacielem, ale w sercu zastawia [na niego] sidła.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Czyż za to nie [powinienem] ich nawiedzić? – mówi PAN. Czyż nad takim narodem moja dusza nie powinna się zemścić?
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 Z powodu tych gór podniosę płacz i lament, z powodu pastwisk na pustkowiu – pieśń żałobną. Są bowiem spalone tak, że nikt tamtędy nie przechodzi ani odgłosu bydła nie słychać; ptactwo niebieskie i zwierzęta rozbiegły się i odeszły.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 I zamienię Jerozolimę w gruzy, w legowisko smoków, a miasta Judy – w pustkowie, [zostaną] bez mieszkańca.
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Któż jest tak mądry, aby [mógł] to zrozumieć? A do kogo mówiły usta PANA, aby [mógł] ogłosić, dlaczego ziemia ginie [i] jest spalona jak pustynia, tak że przez nią nikt nie przechodzi?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 PAN bowiem mówi: Dlatego że porzucili moje prawo, które im przedłożyłem, a nie słuchali mojego głosu ani nie szli za nim;
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 Ale postępowali według uporu swego serca i [szli] za Baalami, jak ich nauczyli ich ojcowie;
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 Dlatego tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Oto nakarmię ich, ten lud, piołunem i napoję ich wodą żółci.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 Rozproszę ich między narodami, których nie znali oni ani ich ojcowie, i poślę za nimi miecz, aż ich doszczętnie wytracę.
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 Tak mówi PAN zastępów: Zastanówcie się i wezwijcie płaczki, i niech przyjdą; poślijcie po te, które są wyćwiczone w tym, i niech przyjdą.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Niech się pospieszą, niech podniosą nad nami lament, aby łzami spływały nam oczy i powieki ociekały wodą.
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 Głos lamentu bowiem słychać z Syjonu: Jakże jesteśmy spustoszeni! Jesteśmy bardzo zawstydzeni, bo opuściliśmy ziemię, zburzono nasze mieszkania.
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Słuchajcie więc, kobiety, słowa PANA, niech wasze ucho przyjmie wyrok jego ust, abyście uczyły wasze córki lamentu, a jedna drugą – pieśni żałobnej.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 Śmierć bowiem wtargnęła przez nasze okna, weszła do naszych pałaców, aby wytracić dzieci na rynku i młodzieńców na ulicach.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Mów: Tak mówi PAN: Nawet trupy ludzkie padną jak gnój na polu i jak snopy za żniwiarzem, a nikt ich nie zbierze.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 Tak mówi PAN: Niech się nie chlubi mądry swoją mądrością, niech się nie chlubi mocarz swoją siłą i niech się nie chlubi bogaty swoim bogactwem;
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 Ale kto chce się chlubić, niech się chlubi tym, że rozumie i zna mnie, [wie], że ja [jestem] PAN, który okazuje miłosierdzie, sąd i sprawiedliwość na ziemi. To bowiem [mi] się podoba, mówi PAN.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Oto nadchodzą dni, mówi PAN, w których nawiedzę każdego obrzezanego i nieobrzezanego;
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 Egipt, Judę, Edom, Ammonitów, Moabitów i wszystkich, którzy są w najdalszych zakątkach i mieszkają na pustyni. Wszystkie te narody bowiem [są] nieobrzezane, a cały dom Izraela ma nieobrzezane serce.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< Jeremiasza 9 >