< Jeremiasza 8 >

1 W tym czasie, mówi PAN, wydobędą z ich grobów kości królów Judy, kości ich książąt, kości kapłanów, kości proroków i kości mieszkańców Jerozolimy;
Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
2 I rozrzucą je przed słońcem, przed księżycem i przed całym zastępem nieba, które oni kochali, którym służyli, za którymi szli, których szukali i którym oddawali pokłon. Nie będą zebrane ani pogrzebane, [lecz] staną się nawozem na powierzchni ziemi.
Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
3 I cała reszta ocalałych z tego przewrotnego rodu będzie wybierać [raczej] śmierć niż życie we wszystkich miejscach, gdzie zostali, kiedy ich wygnałem, mówi PAN zastępów.
Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
4 Dlatego powiesz do nich: Tak mówi PAN: Czy nie powstaje ten, który upadł? Czy nie zawraca ten, który zbłądził?
“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
5 Czemu więc odwrócił się ten lud Jerozolimy wiecznym odstępstwem? Trzymają się kłamstwa, nie chcą wrócić.
Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
6 Uważałem i słyszałem: nie mówią właściwie, nikt nie żałuje swej niegodziwości, mówiąc: Cóż uczyniłem? Każdy biegnie swoją drogą, jak koń pędzący do bitwy.
Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
7 Nawet bocian na niebiosach zna swoje ustalone pory; synogarlica, żuraw i jaskółka przestrzegają czasu swego przylotu. Lecz mój lud nie zna sądu PANA.
Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
8 Jakże [możecie] mówić: My jesteśmy mądrzy, a prawo PANA [jest] przy nas? Oto zaprawdę na próżno uczynił je; daremne jest pióro pisarzy.
“‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
9 Mędrcy się zawstydzili. Są przestraszeni i pojmani. Oto odrzucają słowo PANA, jaką więc mają mądrość?
Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
10 Dlatego ich żony dam innym, ich pola tym, którzy ich zdobędą, bo od najmniejszego aż do największego – wszyscy są oddani chciwości, od proroka aż do kapłana – wszyscy działają podstępnie.
Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
11 I leczą rany córki mego ludu [tylko] powierzchownie, mówiąc: Pokój, pokój! Ale nie ma pokoju.
Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
12 Czy zawstydzili się, że popełnili obrzydliwość? Bynajmniej, wcale się nie zawstydzili ani nie potrafili rumienić. Dlatego upadną wśród tych, co mają upaść. W czasie gdy ich nawiedzę, upadną, mówi PAN.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
13 Doszczętnie ich wykorzenię, mówi PAN. Nie będzie winogron na winorośli ani żadnych fig na drzewie figowym, nawet liść opadnie, a to, co im dałem, zostanie im zabrane.
“‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
14 Czemu [tu] siedzimy? Zbierzcie się, wejdźmy do miast warownych i tam będziemy milczeć. PAN bowiem, nasz Bóg, każe nam milczeć i daje nam do picia wodę żółci, gdyż zgrzeszyliśmy przeciwko PANU.
Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
15 Oczekiwaliśmy pokoju, ale nic dobrego [nie przyszło]; czasu uzdrowienia – a oto strach.
Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
16 Od Dan słychać parskanie jego koni, na odgłos rżenia jego mocarzy zadrżała cała ziemia. Nadciągają, aby pożreć ziemię i wszystko, co jest na niej, miasto i jego mieszkańców.
Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
17 Oto bowiem poślę na was najbardziej jadowite węże, których nie można zaklinać, i będą was kąsać, mówi PAN.
Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
18 Moje serce, które miało mnie posilać w smutku, mdleje we mnie.
Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
19 Oto głos krzyku córki mego ludu z dalekiej ziemi: Czy nie ma PANA na Syjonie? Czy nie ma na nim jego króla? Czemu pobudzili mnie do gniewu swoimi bożkami i obcymi próżnościami? – [odpowiada PAN].
Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
20 Przeminęło żniwo, skończyło się lato, a my nie jesteśmy wybawieni.
“Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
21 Z powodu rany córki mojego ludu jestem ranny, pogrążony w żałobie, ogarnęło mnie przerażenie.
Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
22 Czy nie ma balsamu w Gileadzie? Czy nie ma tam lekarza? Czemu więc nie jest uleczona córka mojego ludu?
Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?

< Jeremiasza 8 >