< Jeremiasza 14 >

1 Słowo PANA, które doszło do Jeremiasza w związku z suszą:
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 Ziemia Judy płacze, a jej bramy osłabły, w szacie żałobnej siedzą na ziemi, a krzyk Jerozolimy się podnosi.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 Ich szlachetni posyłają swoje sługi po wodę. A gdy przyszli do cystern, nie znaleźli wody i powrócili z pustymi naczyniami. Zapłonęli i zawstydzili się, i zakryli swoje głowy.
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 Z powodu spękanej ziemi – bo nie było deszczu na ziemi – oracze ze wstydu zakryli swoje głowy.
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 Nawet łania rodząca na polu porzuciła [młode], bo nie było trawy.
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 A dzikie osły, stojąc na wysokich miejscach, chwyciły wiatr jak smoki; ich oczy osłabły, bo nie było trawy.
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 PANIE, chociaż nasze nieprawości świadczą przeciwko nam, działaj przez wzgląd na twoje imię. Liczne są bowiem nasze odstępstwa, zgrzeszyliśmy przeciwko tobie.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 Nadziejo Izraela, jego Zbawicielu w czasie utrapienia, czemu jesteś jak przybysz w tej ziemi, jak podróżny, który zatrzymuje się na nocleg?
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 Czemu jesteś jak człowiek osłupiały [albo] jak mocarz, który nie może wybawić? Ty jednak jesteś pośród nas, PANIE, i twoje imię jest wzywane nad nami. Nie opuszczaj nas.
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 Tak mówi PAN o tym ludzie: Tak kochają błądzić, swoich nóg nie powstrzymają; dlatego PAN nie ma w nich upodobania, teraz wspomina ich nieprawość i nawiedza ich [za ich] grzechy.
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 Potem PAN powiedział do mnie: Nie módl się o dobro tego ludu.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 Gdy będą pościć, nie wysłucham ich wołania, a gdy będą składać całopalenia i ofiarę z pokarmów, nie przyjmę tego, ale wytracę ich mieczem, głodem i zarazą.
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 Wtedy powiedziałem: Ach, Panie BOŻE! Oto prorocy mówią im: Nie zobaczycie miecza ani nie dotknie was głód, ale dam wam trwały pokój na tym miejscu.
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 I PAN powiedział do mnie: Ci prorocy fałszywie prorokują w moje imię. Nie posłałem ich ani im [niczego] nie nakazywałem, ani nie mówiłem do nich. Prorokują wam kłamliwe widzenie i wróżbę, marność i urojenie swego serca.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 Dlatego tak mówi PAN o prorokach, którzy prorokują w moje imię, chociaż ich nie posłałem, i którzy mówią: Miecza i głodu nie będzie w tej ziemi. Ci sami prorocy od miecza i głodu zginą.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 A ten lud, któremu oni prorokują, będzie wyrzucony na ulice Jerozolimy z powodu głodu i miecza i nie będzie nikogo, kto by pogrzebał ich samych ani ich żon, ani ich synów i córek. Tak wyleję na nich ich niegodziwość.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 Dlatego powiesz im to słowo: Moje oczy wylewają łzy w nocy i we dnie, bez przerwy, bo dziewicza córka mego ludu została dotknięta wielką klęską, ciosem bardzo bolesnym.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 Jeśli wychodzę na pole – oto pobici mieczem, jeśli wchodzę do miasta – oto ginący od głodu. Tak, zarówno prorok, jak i kapłan kupczą ziemią, a [ludzie] tego nie zauważają.
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Czy całkowicie odrzucasz Judę? Czy twoja dusza obrzydziła sobie Syjon? Czemu nas bijesz, tak że już nie ma dla nas uzdrowienia? Oczekiwaliśmy pokoju, ale nie [ma] nic dobrego; [oczekiwaliśmy] czasu uleczenia, a oto trwoga.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Uznajemy, PANIE, swoją niegodziwość i nieprawość naszych ojców, bo zgrzeszyliśmy przeciw tobie.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Nie odrzucaj [nas] przez wzgląd na twoje imię, nie dopuść do znieważenia tronu swojej chwały. Pamiętaj o swoim przymierzu i nie zrywaj go z nami.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Czy wśród marności pogan są takie, co spuszczają deszcz? Czy niebiosa mogą [same] dawać deszcze? Czy to nie ty, PANIE, nasz Boże? Dlatego oczekujemy ciebie, bo ty czynisz to wszystko.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.

< Jeremiasza 14 >