< Izajasza 66 >
1 Tak mówi PAN: Niebo jest moim tronem, a ziemia podnóżkiem moich stóp. Gdzie więc będzie ten dom, który mi zbudujecie? Gdzie będzie miejsce mego odpoczynku?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Bo to wszystko moja ręka uczyniła i dzięki niej powstało to wszystko, mówi PAN. Lecz ja patrzę na tego, który jest ubogi i skruszony w duchu i który drży na moje słowo.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 Ten, kto zabija wołu [na] ofiarę, to jakby zabił człowieka; kto zabija na ofiarę barana, to jakby ściął psu [głowę]; kto przynosi ofiarę, to jakby ofiarował krew świni; kto pali kadzidło, to jakby błogosławił bożkowi. Lecz jak oni wybrali sobie swoje drogi i ich dusza ma upodobanie w obrzydliwościach;
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 Tak i ja wybiorę ich zmyślenia i sprowadzę na nich to, czego się boją, ponieważ gdy wołałem, nikt się nie odezwał, gdy mówiłem, nie słuchali, ale czynili to, co złe w moich oczach, i wybrali to, co mi się nie podobało.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Słuchajcie słowa PANA, wy, którzy drżycie na jego słowo. Wasi bracia, którzy was nienawidzą, którzy wypędzają was ze względu na moje imię, mówią: Niech PAN pokaże swoją chwałę. Ukaże się jednak dla waszej radości, a oni będą zawstydzeni.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Odgłos zgiełku z miasta, głos ze świątyni, głos PANA oddającego zapłatę swoim wrogom.
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Zanim odczuła bóle porodu, urodziła, zanim ogarnął ją ból, urodziła chłopca.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Kto słyszał o czymś takim? Kto widział coś podobnego? Czy ziemia może urodzić w jednym dniu? Czy naród rodzi się od razu? Ale Syjon ledwie zaczął odczuwać bóle, a już urodził swoich synów.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Czyżbym ja, który otwieram łono, nie doprowadził do rodzenia? – mówi PAN. Czyżbym ja, który doprowadzam do rodzenia, zamknął [łono]? – mówi twój Bóg.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Weselcie się z Jerozolimą i radujcie się z nią wszyscy, którzy ją miłujecie. Cieszcie się z nią wielce wszyscy, którzy nad nią płaczecie;
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Aby ssać do syta z piersi jej pociech; abyście ssali i rozkoszowali się pełnią jej chwały.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Tak bowiem mówi PAN: Oto skieruję do niej pokój jak rzekę i chwałę narodów jak strumień wezbrany. Wtedy będziecie ssać, będziecie noszeni na rękach i pieszczeni na kolanach.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Jak tego, którego pociesza matka, tak ja was będę pocieszał; i tak w Jerozolimie doznacie pociechy.
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Ujrzycie to i rozraduje się wasze serce, a wasze kości zakwitną jak trawa. I będzie rozpoznana ręka PANA wobec jego sług, a jego gniew – wobec jego wrogów.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Oto bowiem PAN przyjdzie w ogniu, a jego rydwany będą jak wicher, by wylać zapalczywość swego gniewu i [ukazać] swoją grozę w płomieniu ognia;
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Gdyż PAN będzie sądził ogniem i mieczem wszelkie ciało, a wielu będzie pobitych przez PANA.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 I ci, którzy się uświęcają i oczyszczają w środku ogrodów, jeden za drugim, którzy jedzą mięso wieprzowe oraz inną obrzydliwość, a także myszy, wszyscy razem zginą – mówi PAN.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 Ja znam bowiem ich uczynki i myśli. I przyjdzie czas, że zgromadzę wszystkie narody i języki, a one przyjdą i ujrzą moją chwałę.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 I ustanowię wśród nich znak i wyślę ocalałych spośród nich do narodów do Tarszisz, Pul i Lud, a tych, którzy naciągają łuk – do Tubala i Jawan, do wysp dalekich, które nic o mnie nie słyszały i nie widziały mojej chwały; i będą głosić moją chwałę wśród narodów.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 I przyprowadzą wszystkich waszych braci jako dar dla PANA ze wszystkich narodów, na koniach, na rydwanach, w lektykach, na mułach i na wielbłądach, na moją świętą górę, do Jerozolimy, mówi PAN, tak jak synowie Izraela przynoszą dar w czystym naczyniu do domu PANA.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 I z nich także wezmę sobie kapłanów i Lewitów, mówi PAN.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Jak bowiem to nowe niebo i ta nowa ziemia, które ja uczynię, będą trwać przede mną, mówi PAN, tak będzie trwać wasze potomstwo i wasze imię.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 I stanie się tak, że od nowiu do nowiu księżyca i od szabatu do szabatu przychodzić będzie wszelkie ciało, aby oddać pokłon przede mną, mówi PAN.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 I gdy wyjdą, zobaczą trupy ludzi, którzy wystąpili przeciwko mnie. Ich robak bowiem nie zdechnie i ich ogień nie zgaśnie, i będą obrzydliwością dla wszelkiego ciała.
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”