< Izajasza 60 >

1 Powstań, zajaśniej, ponieważ przyszła twoja światłość i chwała PANA wzeszła nad tobą.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Oto bowiem ciemność okryje ziemię i mrok – ludy, ale nad tobą wzejdzie PAN i jego chwała pojawi się nad tobą.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 I pójdą narody do twojej światłości, a królowie do blasku twojego wschodu.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Podnieś wokoło swe oczy i spójrz: ci wszyscy, którzy się zgromadzili, przyjdą do ciebie. Twoi synowie przyjdą z daleka i twoje córki będą wychowane przy twoim boku.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Wtedy zobaczysz i rozweselisz się, twoje serce zadrży i rozszerzy się, gdyż nawróci się do ciebie tłum morski, a siły narodów przyjdą do ciebie.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Okryje cię mnóstwo wielbłądów, dromadery z Midianu i Efy. Przyjdą wszyscy z Szeby, przyniosą złoto i kadzidło i będą głosić chwałę PANA.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Wszystkie stada Kedaru zgromadzą się u ciebie, barany Nebajotu będą ci służyć: wstąpią na mój ołtarz, gdzie będą przyjęte; i tak ozdobię dom mego majestatu.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 I powiesz: Kim są ci, co nadciągają jak obłoki i jak gołębie do swoich okien?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Zaprawdę wyspy oczekują mnie, a na czele okręty Tarszisz, aby przyprowadzić twoich synów z daleka, a z nimi ich srebro i złoto, do imienia PANA, twego Boga, i do Świętego Izraela, bo cię uwielbił.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 Synowie cudzoziemców odbudują twoje mury i ich królowie będą ci służyć, gdyż w moim gniewie uderzyłem cię, a w mojej łaskawości zlitowałem się nad tobą.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 I twoje bramy będą nieustannie otwarte, nie będą zamknięte ani w dzień, ani w nocy, aby można było przyprowadzić do ciebie siły narodów, i aby ich królowie byli przyprowadzeni.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Ten naród i królestwo, które nie będą ci służyć, zginą. Takie narody właśnie zostaną do szczętu spustoszone.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 Chwała Libanu przyjdzie do ciebie: razem cyprys, sosna oraz bukszpan, na ozdobę miejsca mojej świątyni. I wsławię miejsce moich nóg.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Przyjdą też do ciebie w pokorze synowie tych, którzy cię trapili, i będą się kłaniać do twoich stóp wszyscy ci, którzy tobą wzgardzili. I nazwą cię Miastem PANA, Syjonem Świętego Izraela.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 Za to, że byłaś opuszczona i znienawidzona tak, że nie było nikogo, kto by przez ciebie przechodził, uczynię cię wiecznym dostojeństwem, radością z pokolenia na pokolenie.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Będziesz ssać mleko narodów i piersiami królów będziesz karmiona. I poznasz, że ja jestem PANEM, twoim Zbawicielem i twoim Odkupicielem, Mocarzem Jakuba.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Zamiast miedzi naniosę złota, a zamiast żelaza naniosę srebra, zamiast drewna – miedzi, a zamiast kamieni – żelazo. Ustanowię nad tobą spokojnych zwierzchników i urzędników sprawiedliwych.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Nie będzie więcej słychać o przemocy w twojej ziemi ani o spustoszeniu i zniszczeniu w twoich granicach; ale nazwiesz swoje mury Zbawieniem, a twoje bramy – Chwałą.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Słońce nie będzie już twoją światłością za dnia ani księżyc już nie zaświeci ci swoim blaskiem; ale PAN będzie twoją wieczną światłością, a twój Bóg – twoją chwałą.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Nie zajdzie już więcej twoje słońce, a twój księżyc nie ukryje się, bo PAN będzie twoją wieczną światłością i skończą się dni twojej żałoby.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Cały twój lud będzie sprawiedliwy. Odziedziczy ziemię na wieki, będzie latoroślą mego szczepu, dziełem moich rąk, abym był uwielbiony.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Najmniejszy rozmnoży się tysiąckrotnie, a malutki – w naród potężny. Ja, PAN, dokonam tego rychło, w swoim czasie.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< Izajasza 60 >