< Izajasza 56 >

1 Tak mówi PAN: Strzeżcie sądu i czyńcie sprawiedliwość, bo bliskie jest nadejście mojego zbawienia i objawienie się mojej sprawiedliwości.
Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
2 Błogosławiony człowiek, który to czyni, i syn człowieczy, który się tego trzyma, który przestrzega szabatu, aby go nie bezcześcić, który strzeże swej ręki, aby nie czyniła nic złego.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
3 Niech więc nie mówi cudzoziemiec, który przyłączył się do PANA: PAN na pewno odłączył mnie od swego ludu. Niech też eunuch nie mówi: Oto jestem suchym drzewem.
Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
4 Tak bowiem mówi PAN o eunuchach, którzy przestrzegają moich szabatów i wybierają to, co mi się podoba, i trzymają się mojego przymierza:
Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
5 Dam im miejsce w swoim domu i w swoich murach oraz imię lepsze od synów i córek; dam im imię wieczne, które nie będzie zgładzone.
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
6 A cudzoziemców, którzy przyłączyli się do PANA, aby mu służyć, miłować imię PANA i być jego sługami, wszystkich przestrzegających szabatu, by go nie bezcześcić, i trzymających się mojego przymierza;
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
7 Tych przyprowadzę na swoją świętą górę i rozraduję ich w swoim domu modlitwy. Ich całopalenia i ofiary będą przyjęte na moim ołtarzu, bo mój dom będzie nazywany domem modlitwy dla wszystkich narodów.
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
8 Tak mówi Pan BÓG, który gromadzi rozproszonych z Izraela: Jeszcze [innych] zgromadzę do niego i do jego zgromadzonych.
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
9 Wszystkie zwierzęta polne, przyjdźcie na żer, i [wy], wszystkie zwierzęta leśne.
Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Jego stróżowie są ślepi wszyscy, nic nie wiedzą, wszyscy są niemymi psami, nie mogą szczekać; są ospali, leżą, kochają drzemać.
Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
11 A są to psy żarłoczne i nienasycone; są to pasterze niezdolni do zrozumienia. Wszyscy udali się w swoją drogę, każdy w swoim miejscu [szuka] własnego zysku, mówiąc:
Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 Przyjdźcie, wezmę wino i upijemy się mocnym napojem; jutro będzie tak jak dziś i jeszcze bardziej obficie.
Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”

< Izajasza 56 >