< Ozeasza 5 >
1 Słuchajcie tego, kapłani, zważ [na to], domu Izraela, i nakłoń ucha, domu króla. Przeciwko wam bowiem [jest] sąd, ponieważ byliście sidłem dla Mispy i siecią rozciągniętą na Taborze.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 Owszem, udają się podstępnie na rzeź, ale ja ukarzę każdego z nich.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 Znam Efraima i Izrael nie jest ukryty przede mną, bo teraz, Efraimie, uprawiasz nierząd, a Izrael się splugawił.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 Nie chcą zmienić swoich czynów, aby się nawrócić do swego Boga, dlatego że duch nierządu jest wśród nich i nie poznali PANA.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 Pycha Izraela świadczy przeciwko niemu. Dlatego Izrael i Efraim upadną z powodu swojej nieprawości, upadnie wraz z nimi też Juda.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 Ze swoimi trzodami i swoim bydłem pójdą szukać PANA, ale [go] nie znajdą, bo odstąpił od nich.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 Sprzeniewierzyli się PANU, bo napłodzili obcych synów, [a] teraz miesiąc pożre ich wraz z ich dziedzictwami.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Zadmijcie w trąbę w Gibea i w trąbę w Rama; krzyczcie w Bet-Awen: [Wróg] za tobą, Beniaminie!
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Efraim będzie spustoszony w dniu kary. Oznajmiłem wśród pokoleń Izraela to, co pewne.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 Książęta Judy stali się jak ci, którzy przesuwają granice. Wyleję na nich swój gniew jak wodę.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Efraim jest uciskany i pokruszony sądem, gdyż chętnie chodził za rozkazem [ludzkim].
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 Dlatego będę dla Efraima jak mól, a dla domu Judy jak próchnica.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 Gdy Efraim zauważył swoją chorobę, a Juda swoją ranę, uciekł Efraim do Asyryjczyka i posłał do króla Jareb. Ale on was nie będzie mógł uzdrowić ani uleczyć waszej rany.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 Będę bowiem dla Efraima jak srogi lew, a dla domu Judy jak młody lew. Ja, ja [sam] porwę i odejdę; wezmę, a nikt mi [go] nie wydrze.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 Pójdę i wrócę do swego miejsca, aż uznają swoją winę i zaczną szukać mojego oblicza. W swoim utrapieniu będą mnie pilnie szukać.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”