< Hebrajczyków 3 >

1 Dlatego, bracia święci, uczestnicy niebieskiego powołania, zwróćcie uwagę na Apostoła i Najwyższego Kapłana naszego wyznania, Chrystusa Jezusa;
Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza.
2 Wiernego temu, który go ustanowił, podobnie jak Mojżesz [był] w całym jego domu.
Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu.
3 Tym większej bowiem chwały jest on godzien od Mojżesza, im większą cześć od domu ma jego budowniczy.
Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo.
4 Bo każdy dom jest przez kogoś zbudowany, lecz tym, który wszystko zbudował, jest Bóg.
Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu.
5 I Mojżesz wprawdzie był wierny w całym jego domu jako sługa, na świadectwo tego, co potem miało być powiedziane;
Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo.
6 Lecz Chrystus jako syn panuje nad swoim domem. Jego domem my jesteśmy, jeśli tylko ufność i chwalebną nadzieję aż do końca niewzruszenie zachowamy.
Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.
7 Dlatego, jak mówi Duch Święty: Dzisiaj, jeśli usłyszycie jego głos;
Tsono monga Mzimu Woyera akuti, “Lero mukamva mawu ake,
8 Nie zatwardzajcie waszych serc jak podczas rozdrażnienia, w dniu próby na pustyni;
musawumitse mitima yanu ngati munachitira pamene munawukira, pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.
9 Gdzie mnie wystawiali na próbę wasi ojcowie [i] doświadczali, i oglądali moje dzieła przez czterdzieści lat.
Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa, ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.
10 Dlatego się rozgniewałem na to pokolenie i powiedziałem: Oni zawsze błądzą sercem i nie poznali moich dróg;
Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo, ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera, ndipo iwo sadziwa njira zanga.’
11 Toteż przysiągłem w moim gniewie, że nie wejdą do mojego odpoczynku.
Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti, ‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’”
12 Uważajcie, bracia, żeby nie było czasem w kimś z was przewrotnego serca niewiary, które by odstępowało od Boga żywego;
Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo.
13 Lecz zachęcajcie się wzajemnie każdego dnia, dopóki nazywa się „Dzisiaj”, aby nikt z was nie popadł w zatwardziałość przez oszustwo grzechu.
Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo.
14 Staliśmy się bowiem uczestnikami Chrystusa, jeśli tylko nasze pierwotne przeświadczenie aż do końca niewzruszenie zachowamy.
Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi.
15 Dopóki jest powiedziane: Dzisiaj, jeśli usłyszycie jego głos, nie zatwardzajcie waszych serc jak w dniu rozdrażnienia.
Monga kunanenedwa kuti, “Lero ngati mumva mawu ake, musawumitse mitima yanu ngati momwe munachitira pamene munawukira.”
16 Niektórzy bowiem, usłyszawszy, rozdrażnili [Pana], ale nie wszyscy [z tych], którzy wyszli z Egiptu pod wodzą Mojżesza.
Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto?
17 A na kogo gniewał się przez czterdzieści lat? Czy nie na tych, którzy zgrzeszyli, a których ciała legły na pustyni?
Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja?
18 A którym przysiągł, że nie wejdą do jego odpoczynku, jeśli nie tym, którzy byli nieposłuszni?
Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja.
19 Widzimy więc, że nie mogli wejść z powodu niewiary.
Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

< Hebrajczyków 3 >