< Aggeusza 2 >

1 W siódmym [miesiącu], dwudziestego pierwszego [dnia] tego miesiąca, słowo PANA doszło przez proroka Aggeusza mówiące:
Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
2 Mów teraz do Zorobabela, syna Szealtiela, namiestnika Judy, i do Jozuego, syna Josadaka, najwyższego kapłana, oraz do reszty ludu:
“Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
3 Któż pozostał pośród was, który widział ten dom w jego dawnej chwale? A jakim go teraz widzicie? Czy nie wydaje się wam, że jest niczym w porównaniu z tamtym?
‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
4 Teraz jednak umocnij się, Zorobabelu, mówi PAN; umocnij się, Jozue, synu Josadaka, najwyższy kapłanie; umocnij się też, cały ludu tej ziemi, mówi PAN, i pracujcie. Ja bowiem jestem z wami, mówi PAN zastępów.
Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
5 Zgodnie ze słowem, przez które zawarłem z wami przymierze, gdy wyszliście z Egiptu, mój Duch jest stale wśród was, nie bójcie się.
‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
6 Tak bowiem mówi PAN zastępów: Jeszcze raz, [po] krótkim [czasie], wstrząsnę niebem i ziemią, morzem i lądem;
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
7 Wstrząsnę wszystkimi narodami i przyjdzie Pożądany przez wszystkie narody. I napełnię ten dom chwałą, mówi PAN zastępów.
Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
8 Moje jest srebro i moje [jest] złoto, mówi PAN zastępów.
‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Chwała tego domu będzie większa od tej, jaką miał tamten dawny, mówi PAN zastępów; bo to miejsce obdarzę pokojem, mówi PAN.
‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
10 Dnia dwudziestego czwartego, dziewiątego [miesiąca], w drugim roku Dariusza, słowo PANA doszło przez proroka Aggeusza mówiące:
Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
11 Tak mówi PAN zastępów: Zapytaj teraz kapłanów o prawo:
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
12 Gdyby ktoś niósł poświęcone mięso [włożone] za połę swojej szaty, a połą dotknął chleba, potrawy, wina, oliwy lub jakiegokolwiek pokarmu, czy to stałoby się poświęcone? Odpowiedzieli kapłani: Nie.
Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
13 Wtedy Aggeusz zapytał: Jeśli ktoś, będąc nieczysty od zwłok, dotknie którejś z tych rzeczy, czy staje się ona nieczysta? Odpowiedzieli kapłani: Stanie się nieczysta.
Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
14 Wtedy Aggeusz odezwał się i powiedział: Taki jest ten lud, taki jest ten naród przede mną, mówi PAN; takie jest każde dzieło ich rąk; i wszystko, co tam składają w ofierze, jest nieczyste.
Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
15 Teraz więc, proszę, zastanówcie się, [jak się wam powodziło] od dzisiejszego dnia do minionych [dni], zanim ułożono kamień na kamieniu w świątyni PANA.
“‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
16 Dawniej, gdy ktoś przyszedł do stosu zboża z dwudziestu [miar], było [ich] tylko dziesięć; gdy przyszedł do prasy, aby naczerpać pięćdziesiąt wiader [wina], było [ich] tylko dwadzieścia.
Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
17 Karałem was suszą, pleśnią i gradem we wszystkich dziełach waszych rąk; lecz żaden z was nie [wrócił] do mnie, mówi PAN.
Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
18 Zastanówcie się teraz [nad okresem] od dzisiejszego dnia po [dni] minione, od dnia dwudziestego czwartego, dziewiątego [miesiąca, to znaczy] od dnia, w którym położono [fundament] świątyni PANA; zastanówcie się.
‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
19 Czy ziarno jeszcze [jest] w spichlerzu? I [owszem] ani winorośl, ani drzewo figowe, granatowe i oliwne nie wydały jeszcze owocu. Od tego dnia będę [wam] błogosławił.
Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
20 Potem słowo PANA doszło po raz drugi do Aggeusza dnia dwudziestego czwartego [tego] miesiąca mówiące:
Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
21 Mów do Zorobabela, namiestnika Judy: Ja wstrząsnę niebiosami i ziemią;
“Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
22 I przewrócę tron królestw, i zniszczę moc królestw pogan; przewrócę także rydwany i tych, którzy na nich jeżdżą; i upadną konie i ich jeźdźcy, każdy od miecza swego brata.
Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
23 W tym dniu, mówi PAN zastępów, wezmę cię, Zorobabelu, mój sługo, synu Szealtiela, mówi PAN, i uczynię cię niczym sygnet. Ja bowiem wybrałem ciebie, mówi PAN zastępów.
“‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

< Aggeusza 2 >