< Rodzaju 48 >

1 Gdy to się stało, dano znać Józefowi: Oto twój ojciec zachorował. Wziął więc ze sobą swoich dwóch synów, Manassesa i Efraima.
Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
2 I powiedziano Jakubowi: Oto twój syn Józef idzie do ciebie. A Izrael zebrał siłę i usiadł na łożu.
Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
3 Wtedy Jakub powiedział do Józefa: Bóg Wszechmogący ukazał mi się w Luz, w ziemi Kanaan, i błogosławił mi.
Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
4 I powiedział do mnie: Oto ja uczynię cię płodnym i rozmnożę cię, i wywiodę z ciebie wielki lud. I dam tę ziemię twemu potomstwu po tobie w wieczne dziedzictwo.
nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
5 Dlatego teraz twoi dwaj synowie, Efraim i Manasses, którzy urodzili ci się w ziemi Egiptu, zanim przyszedłem tu do ciebie do Egiptu, są moimi. Będą moi jak Ruben i Symeon.
“Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
6 Ale twoje dzieci, które spłodzisz po nich, będą twoje; będą zwane w swych posiadłościach imieniem swoich braci.
Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
7 A gdy wracałem z Paddan, umarła mi Rachela w ziemi Kanaan, w drodze, gdy byłem jeszcze w niewielkiej odległości od Efraty, i pogrzebałem ją tam przy drodze do Efraty, czyli Betlejem.
Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
8 A gdy Izrael zobaczył synów Józefa, zapytał: Czyi oni są?
Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
9 Józef odpowiedział swemu ojcu: To są moi synowie, których Bóg dał mi tutaj. A [on] powiedział: Proszę, przyprowadź ich do mnie, abym im błogosławił.
Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
10 A oczy Izraela były tak słabe ze starości, że nie mógł widzieć. I przyprowadził ich do niego, a [Jakub] ich pocałował i uścisnął.
Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
11 Potem Izrael powiedział do Józefa: Nie spodziewałem się, że będę jeszcze oglądał twoją twarz, a oto Bóg dał mi widzieć nawet twoje potomstwo.
Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
12 Wtedy Józef odsunął ich od jego kolan i pokłonił się twarzą aż do ziemi.
Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
13 Potem Józef wziął obydwu i [postawił] Efraima po swojej prawej ręce, czyli po lewej stronie Izraela; a Manassesa po swojej lewej ręce, czyli po prawej stronie Izraela, i przyprowadził ich do niego.
Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
14 Izrael wyciągnął swoją prawą rękę, położył ją na głowę Efraima, który był młodszy, a swoją lewą rękę na głowę Manassesa, umyślnie pokładając swoje ręce, choć pierworodny był Manasses.
Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
15 I błogosławił Józefowi, mówiąc: Bóg, przed którego obliczem chodzili moi ojcowie, Abraham i Izaak, Bóg, który mnie żywił od mej młodości aż do dziś;
Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
16 Anioł, który wybawił mnie ze wszelkiego zła, niech błogosławi tym chłopcom i niech będą nazywani [od] mego imienia i od imienia moich ojców, Abrahama i Izaaka, i niech się rozmnożą na ziemi.
mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
17 A gdy Józef zobaczył, że jego ojciec położył swoją prawą rękę na głowę Efraima, nie podobało mu się to. Wziął więc rękę swego ojca, aby ją przenieść z głowy Efraima na głowę Manassesa.
Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
18 I Józef powiedział do swego ojca: Nie tak, mój ojcze. Ten bowiem [jest] pierworodny, połóż swoją prawą rękę na jego głowę.
nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
19 Ale jego ojciec wzbraniał się i powiedział: Wiem, mój synu, wiem. Ten też stanie się ludem i on też urośnie, ale jego młodszy brat go przewyższy, a z jego potomstwa wyjdzie mnóstwo narodów.
Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
20 Błogosławił im więc tego dnia, mówiąc: Przez ciebie Izrael będzie błogosławił, mówiąc: Niech Bóg cię uczyni jak Efraim i jak Manasses. Tak wyróżnił Efraima przed Manassesem.
Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
21 Potem Izrael powiedział do Józefa: Oto ja umieram, ale Bóg będzie z wami i przywróci was do ziemi waszych ojców.
Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
22 Oto daję ci jedną część więcej niż twoim braciom, którą nabyłem moim mieczem i moim łukiem z ręki Amorytów.
Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”

< Rodzaju 48 >