< Rodzaju 43 >

1 A ciężki głód [panował] w tej ziemi.
Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
2 I gdy zużyli zboże, które przynieśli z Egiptu, ich ojciec powiedział do nich: Idźcie znowu [i] kupcie nam trochę żywności.
Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
3 Juda powiedział do niego: Ten człowiek uroczyście nam oświadczył: Nie zobaczycie mojej twarzy, jeśli nie będzie z wami waszego brata.
Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
4 Jeśli [więc] poślesz naszego brata z nami, pojedziemy i nakupimy ci żywności;
Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
5 Ale jeśli nie poślesz, nie pojedziemy, bo ten człowiek mówił do nas: Nie zobaczycie mojej twarzy, jeśli nie będzie z wami waszego brata.
Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
6 Izrael zapytał: Dlaczego sprawiliście mi ból, mówiąc temu człowiekowi, że macie jeszcze brata?
Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
7 Odpowiedzieli: Ten człowiek dokładnie się wypytał o nas i naszą rodzinę: Żyje jeszcze wasz ojciec? Macie [jeszcze jakiegoś] brata? I odpowiedzieliśmy mu na jego pytania. Skąd mogliśmy wiedzieć, że powie: Przyprowadźcie mi tu waszego brata?
Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
8 I Juda powiedział do swego ojca Izraela: Poślij chłopca ze mną. Powstaniemy i pojedziemy, abyśmy żyli, a nie pomarli [z głodu], tak my, jak i ty, i nasze dzieci.
Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
9 Ja biorę odpowiedzialność za niego, ode mnie się go domagaj. Jeśli nie przyprowadzę go do ciebie i nie stawię go przed tobą, na zawsze będę ponosił [za to] winę.
Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
10 Gdybyśmy bowiem nie zwlekali, wrócilibyśmy już dwa razy.
Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
11 Wtedy Izrael, ich ojciec, powiedział do nich: Jeśli tak [musi być], zróbcie w ten sposób: weźcie z najlepszych owoców ziemi w wasze naczynia i zanieście je temu człowiekowi w darze – trochę balsamu, trochę miodu, wonności, mirry, orzechów i migdałów.
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
12 Weźcie też ze sobą podwójną sumę pieniędzy, a pieniądze wrzucone na wierzch waszych worów zabierzcie ze sobą, bo może to była pomyłka.
Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
13 Weźcie także waszego brata, wstańcie i jedźcie znowu do tego człowieka;
Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
14 A niech Bóg Wszechmogący da wam miłosierdzie przed tym człowiekiem, aby wam wypuścił waszego drugiego brata i Beniamina. A jeśli mam stracić swoje dzieci, to je stracę.
Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
15 Mężczyźni wzięli więc ten dar, zabrali ze sobą podwójną sumę pieniędzy oraz Beniamina, wstali i pojechali do Egiptu, i stanęli przed Józefem.
Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
16 A gdy Józef zobaczył z nimi Beniamina, powiedział do zarządcy jego domu: Wprowadź tych ludzi do domu, zabij [bydlę] i przyrządź, bo ci ludzie w południe będą jedli ze mną.
Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
17 Człowiek ten zrobił, jak mu Józef rozkazał, i wprowadził tych ludzi do domu Józefa.
Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
18 Gdy zostali wprowadzeni do domu Józefa, bali się i mówili: Wprowadzono nas tu z powodu tych pieniędzy, które za pierwszym razem włożono do naszych worów, aby rzucić na nas [oszczerstwo], napaść na nas i wziąć w niewolę nas i nasze osły.
Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
19 Podeszli do zarządcy domu Józefa i rozmawiali z nim w drzwiach domu.
Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
20 I powiedzieli: [Pozwól], panie. Przyjechaliśmy za pierwszym razem kupić żywności.
“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
21 A gdy przyjechaliśmy do gospody i rozwiązaliśmy nasze wory, pieniądze każdego [były] na wierzchu jego wora, nasze pieniądze w pełnej wadze. Przywieźliśmy je więc ze sobą.
koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
22 Przywieźliśmy też inne pieniądze ze sobą, aby nakupić żywności. Nie wiemy, kto włożył nasze pieniądze do naszych worów.
Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
23 A [on] powiedział: Pokój wam, nie bójcie się. Bóg wasz, Bóg waszego ojca, dał wam skarb do waszych worów. Wasze pieniądze doszły do mnie. I wyprowadził do nich Symeona.
Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
24 Człowiek ten wprowadził tych ludzi do domu Józefa, dał im wody, aby umyli sobie nogi; dał też karmę ich osłom.
Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
25 Potem przygotowali dar, zanim Józef przyszedł w południe. Słyszeli bowiem, że tam mieli jeść chleb.
Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
26 A gdy Józef wszedł do domu, przynieśli mu dar, który [mieli] ze sobą w tym domu, i pokłonili mu się aż do ziemi.
Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
27 I dowiadywał się, jak się im powodzi, i zapytał: Czy wasz ojciec jest zdrowy, ten starzec, o którym mi opowiadaliście? Czy jeszcze żyje?
Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
28 A oni odpowiedzieli: Twój sługa, nasz ojciec, jest zdrowy, jeszcze żyje. I uklękli, i pokłonili mu się.
Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
29 Wtedy podniósł swe oczy i zobaczył swego brata Beniamina, syna swej matki, i zapytał: Czy to [jest] wasz najmłodszy brat, o którym mi opowiadaliście? I powiedział mu: Niech Bóg będzie ci miłosierny, miły synu.
Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
30 I nagle Józef [wyszedł], bo wzruszył się do głębi swym bratem, i szukał [miejsca], gdzie mógłby zapłakać. Wszedł więc do komnaty i tam płakał.
Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
31 Potem umył swoją twarz, wyszedł i gdy się opanował, powiedział: Kładźcie chleb.
Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
32 Położono jemu osobno, im osobno i osobno Egipcjanom, którzy z nim jedli. Egipcjanie bowiem nie mogą jeść chleba z Hebrajczykami, gdyż to budzi odrazę u Egipcjan.
Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
33 I usiedli przed nim, pierworodny według swego pierworództwa, a młodszy według swej młodości. I dziwili się ci mężczyźni, [patrząc] jeden na drugiego.
Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
34 Potem brał potrawy sprzed siebie i kazał im zanieść. A porcja Beniamina była pięciokrotnie większa od porcji ich wszystkich. Pili i podpili sobie z nim.
Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.

< Rodzaju 43 >