< Rodzaju 22 >

1 Po tych wydarzeniach Bóg wystawił Abrahama na próbę i powiedział do niego: Abrahamie! A on odpowiedział: Oto jestem.
Nthawi ina zitatha izi, Mulungu anamuyesa Abrahamu. Iye anati, “Abrahamu!” Ndipo iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
2 I [Bóg] powiedział: Weź teraz swego syna, twego jedynego, którego miłujesz, Izaaka, idź do ziemi Moria i tam złóż go na ofiarę całopalną na jednej górze, o której ci powiem.
Ndipo Mulungu anati, “Tenga Isake, mwana wako yekhayo amene umamukonda ndi kupita naye ku dziko la Moriya. Ukamupereke iye ngati nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri a kumeneko limene ndidzakuwuza.”
3 Abraham wstał więc wcześnie rano, osiodłał swego osła i wziął ze sobą dwóch służących i swego syna Izaaka, narąbał drew na ofiarę całopalną, wstał i poszedł na miejsce, o którym mu Bóg powiedział.
Abrahamu anadzuka mmamawa wake namangirira chokhalira pa bulu. Atadula nkhuni zokwanira zowotchera nsembe yopsereza, Abrahamu, antchito ake awiri pamodzi ndi Isake ananyamuka kupita kumalo kumene Mulungu anamuwuza Abrahamu.
4 A trzeciego dnia Abraham podniósł swe oczy i zobaczył z daleka to miejsce.
Pa tsiku lachitatu, Abrahamu anakweza maso ake ndipo anaona malowo chapatali.
5 Wtedy Abraham powiedział do swoich służących: Zostańcie tu z osłem, a ja i chłopiec pójdziemy tam, oddamy cześć [Bogu] i wrócimy do was.
Ndipo Abrahamu anati kwa antchito ake aja, “Bakhalani pano ndi buluyu. Ine ndi mnyamatayu tipita uko kukapemphera, koma tibweranso.”
6 Wziął więc Abraham drwa na ofiarę całopalną i włożył je na swego syna Izaaka, [a sam] wziął do ręki ogień i nóż i poszli obaj razem.
Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza zija namusenzetsa mwana wake Isake, ndipo iye mwini anatenga moto ndi mpeni. Pamene awiriwo amayendera pamodzi,
7 I Izaak powiedział do swego ojca Abrahama: Mój ojcze! A [on] odpowiedział: Oto jestem, mój synu. I [Izaak] zapytał: Oto ogień i drwa, a gdzie jest baranek na ofiarę całopalną?
Isake anati kwa abambo ake Abrahamu, “Abambo?” Abrahamu anayankha, “Ee mwana wanga.” Isake anafunsa, “Moto ndi nkhuni zilipo, koma nanga mwana wankhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?”
8 Abraham odpowiedział: Bóg sobie upatrzy baranka na ofiarę całopalną, mój synu. I szli obaj razem.
Abrahamu anayankha, “Mwana wanga, Mulungu adzipezera yekha mwana wankhosa wa nsembe yopsereza.” Ndipo awiriwo anapitiriza ulendo.
9 A gdy przyszli na miejsce, o którym mu Bóg powiedział, Abraham zbudował tam ołtarz, ułożył na nim drwa, związał swego syna Izaaka i położył go na ołtarzu na drwach.
Atafika pamalo pamene Mulungu anamuwuza paja, Abrahamu anamangapo guwa lansembe nayika nkhuni pamwamba pa guwapo. Kenaka anamumanga mwana wake Isake namugoneka paguwapo, pamwamba pa nkhuni paja.
10 Potem Abraham wyciągnął rękę i wziął nóż, aby zabić swego syna.
Kenaka Abrahamu anatambasula dzanja lake natenga mpeni kuti aphe mwana wake.
11 Lecz Anioł PANA zawołał do niego z nieba: Abrahamie, Abrahamie! A [on] odpowiedział: Oto jestem.
Koma mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba nati, “Abrahamu! Abrahamu!” Iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
12 [Anioł] powiedział: Nie podnoś ręki na chłopca i nic mu nie czyń, bo teraz wiem, że boisz się Boga i nie odmówiłeś mi swego jedynego syna.
Mngeloyo anati, “Usatambasulire mwanayo dzanja lako kuti umuphe, pakuti tsopano ndadziwa kuti iwe umaopa Mulungu. Iwe sunandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”
13 A Abraham podniósł swe oczy i spojrzał, a oto za nim baran zaplątał się rogami w zaroślach. Abraham poszedł więc i wziął barana, i złożył go na ofiarę całopalną zamiast swego syna.
Abrahamu anatukula maso ake ndipo anaona nkhosa yamphongo itakoledwa ndi nyanga zake mu ziyangoyango. Iye anapita nakatenga nkhosa ija ndikuyipha ngati nsembe yopsereza mʼmalo mwa mwana wake.
14 I Abraham nadał temu miejscu nazwę: PAN upatrzy. Dlatego po dziś dzień mówią: Na górze PANA będzie upatrzony.
Choncho Abrahamu anatcha malo amenewa kuti Yehova-Yire (Wopereka). Ndipo mpaka lero amatchula malowo kuti ndi “Pa phiri la Yehova wopereka.”
15 Wtedy Anioł PANA ponownie zawołał z nieba na Abrahama:
Mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba kachiwiri
16 Przysiągłem na siebie samego, mówi PAN: Ponieważ to uczyniłeś i nie odmówiłeś mi swego syna, twego jedynego;
ndipo anati, “Ndikulumbira mwa Ine ndekha kuti popeza wachita zimenezi, wosandikaniza mwana wako mmodzi yekhayu,
17 Błogosławiąc, będę ci błogosławić, a rozmnażając, rozmnożę twoje potomstwo jak gwiazdy na niebie i jak piasek na brzegu morza; a twoje potomstwo odziedziczy bramy swoich nieprzyjaciół.
ndidzakudalitsa ndithu ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zamlengalenga komanso ngati mchenga wa mʼmphepete mwa nyanja. Zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo,
18 I w twoim potomstwie będą błogosławione wszystkie narody ziemi, dlatego że posłuchałeś mojego głosu.
ndipo kudzera mwa chidzukulu chako, mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi idzadalitsika, chifukwa iwe wandimvera.”
19 Abraham wrócił więc do swoich służących i wstali, i wspólnie udali się do Beer-Szeby. Abraham bowiem mieszkał w Beer-Szebie.
Kenaka Abrahamu anabwerera kumene anasiya antchito ake kuja nanyamukira nawo pamodzi kupita ku Beeriseba. Ndipo Abrahamu anakhala ku Beeriseba.
20 Po tych wydarzeniach doniesiono Abrahamowi: Oto Milka również urodziła dzieci twemu bratu Nachorowi;
Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana.
21 Usa, jego pierworodnego, Buza, jego brata, i Kemuela, ojca Arama;
Woyamba anali Huzi ndipo kenaka mʼbale wake Buzi. Anaberekanso Kemueli, amene anali abambo ake a Aramu.
22 I Keseda, Chazo, Pildasza, Jidlafa i Betuela.
Ana ena ndi Kesede Hazo, Pilidasi, Yidilafi ndi Betueli.”
23 Betuel zaś spłodził Rebekę. Tych ośmiu urodziła Milka Nachorowi, bratu Abrahama.
Betueli anabereka Rebeka. Milika anaberekera Nahori, mʼbale wake wa Abrahamu, ana aamuna asanu ndi atatu amenewa.
24 A jego nałożnica, której imię było Reuma, urodziła też Tebacha, Gachama, Tachasza i Maakę.
Mkazi wake wachiwiri, dzina lake Reuma, anamubaliranso Nahori ana awa: Teba, Gahamu, Tahasi ndi Maaka.

< Rodzaju 22 >