< Ezechiela 9 >
1 Potem zawołał donośnym głosem do moich uszu, mówiąc: Zbliżcie się straże miasta, każda z niszczycielską bronią w ręku.
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 A oto sześciu mężów przyszło drogą od górnej bramy, która jest zwrócona ku północy, i każdy z nich miał w ręku niszczycielską broń. Jeden mąż wśród nich był ubrany w lnianą szatę, z kałamarzem pisarskim u boku. Weszli i stanęli obok ołtarza z brązu.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 A chwała Boga Izraela uniosła się znad cherubina, na którym spoczywała, [i sięgnęła] do progu świątyni. Potem zawołał na tego męża ubranego w lnianą szatę, który miał kałamarz pisarski u boku;
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 PAN powiedział do niego: Przejdź przez środek miasta, przez środek Jerozolimy, i uczyń znak na czołach mężczyzn, którzy wzdychają i lamentują nad wszystkimi obrzydliwościami, jakie popełnia się pośród niej.
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 A słyszałem, że tamtym powiedział tak: Idźcie za nim przez miasto i zabijajcie. Niech wasze oko nie oszczędzi [nikogo] i nie zlituję się [nad nikim].
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Wybijcie do szczętu starców i młodzieńców, panny, dzieci i kobiety, ale nie przystępujcie do nikogo, na którym będzie ten znak. Rozpocznijcie od mojej świątyni. Zaczęli więc od starszych, którzy byli przed domem.
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 Powiedział im: Splugawcie ten dom i napełnijcie dziedziniec zabitymi. Idźcie. Wyszli więc i zabijali w mieście.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 A gdy ich zabijali, a ja pozostałem, wtedy padłem na twarz i zawołałem: Ach, Panie BOŻE! Czy wytracisz całą resztkę Izraela, wylewając swoją zapalczywość na Jerozolimę?
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 Odpowiedział mi: Nieprawość domu Izraela i Judy jest niezmiernie wielka, ziemia jest pełna krwi i miasto pełne przewrotności. Mówią bowiem: PAN opuścił tę ziemię, PAN nas nie widzi.
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 A więc ja [to uczynię], moje oko nie oszczędzi [nikogo] i nie zlituję się [nad nikim], złożę im na głowę ich własne postępowanie.
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 A oto ten mąż odziany w lnianą szatę, który miał kałamarz u boku, oznajmił: Uczyniłem tak, jak mi rozkazałeś.
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”