< Ezechiela 22 >
1 I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
Yehova anandiyankhula nati:
2 A ty, synu człowieczy, czy zechcesz sądzić, czy zechcesz sądzić to krwawe miasto? Uświadom mu więc wszystkie jego obrzydliwości.
“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
3 Powiedz: Tak mówi Pan BÓG: O miasto, które rozlewasz krew u siebie, aby przyszedł [twój] czas, i czynisz sobie bożki przeciwko sobie, aby się nimi plugawić.
ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
4 Przez krew, którąś przelało, jesteś winne, i przez swoje bożki, któreś robiło, jesteś skalane, i tyś sprawiło, że przybliżyły się twoje dni, tyś doszło do swoich lat. Dlatego wydam cię [na] pohańbienie narodom i na pośmiewisko wszystkim ziemiom.
wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
5 Ci, którzy są blisko, i ci, którzy są daleko od ciebie, będą się z ciebie naśmiewać, o [miasto] złej sławy i pełne zgiełku.
Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
6 Oto książęta Izraela, każdy był w tobie, po to, aby [całą] siłą krew rozlewać.
“‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
7 W tobie ojca i matkę znieważają, u ciebie czynią krzywdę przybyszowi, w tobie uciskają sierotę i wdowę.
Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
8 Wzgardzasz moimi świętymi rzeczami i zbezczeszczasz moje szabaty.
Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
9 W tobie są oszczercy w celu rozlania krwi, w tobie jadają na górach, u ciebie popełniają czyny haniebne.
Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
10 W tobie odkrywa się nagość ojca, w tobie hańbią oddaloną z powodu jej nieczystości.
Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
11 Jeden popełnia obrzydliwość z żoną swego bliźniego, drugi sprośnie plami swoją synową, inny zaś u ciebie hańbi swoją siostrę, córkę swego ojca.
Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
12 W tobie biorą dary za rozlanie krwi, pobierasz lichwę i odsetki, wyzyskujesz swego bliźniego przez ucisk i zapominasz o mnie, mówi Pan BÓG.
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
13 Dlatego oto ja klasnąłem w swą dłoń z powodu twego [nieuczciwego] zysku, któreś zdobyło, i z powodu krwi, którą u ciebie rozlano.
“‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
14 Czy twoje serce wytrzyma? Czy twoje ręce będą na tyle mocne w dniach, kiedy ja będę miał z tobą sprawę? Ja, PAN, to powiedziałem i uczynię.
Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
15 Rozproszę cię między poganami i rozrzucę cię po ziemiach, i usunę z ciebie twoją nieczystość.
Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
16 I będziesz splugawione na oczach pogan, i poznasz, że ja jestem PANEM.
Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
17 Potem doszło do mnie słowo PANA mówiące:
Yehova anandiyankhula nati:
18 Synu człowieczy, dom Izraela zamienił mi się w żużel; wszyscy [są] miedzią, cyną, żelazem i ołowiem w środku pieca; stali się żużlem srebra.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
19 Dlatego tak mówi Pan BÓG: Ponieważ wy wszyscy staliście się żużlem, oto zgromadzę was w środku Jerozolimy.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
20 [Jak] gromadzi się srebro, miedź, żelazo, ołów i cynę wewnątrz pieca, aby rozdmuchano na nie ogień, by je roztopić, tak was zgromadzę w swojej zapalczywości i w swoim gniewie, złożę was i roztopię.
Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
21 Tak, zgromadzę was i rozdmucham na was ogień swojej zapalczywości i zostaniecie roztopieni w jej środku.
Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
22 Jak topi się srebro w środku pieca, tak i wy zostaniecie roztopieni w jej środku; i poznacie, że ja, PAN, wylałem na was swoją zapalczywość.
Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
23 Ponadto doszło do mnie słowo PANA:
Yehova anandiyankhulanso nati,
24 Synu człowieczy, mów do niej: Ty jesteś ziemią nieoczyszczoną i nieobmytą deszczem w dniu mojej zapalczywości.
“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
25 W środku tej [ziemi znajduje się] spisek jej proroków, podobni są oni do ryczącego lwa, co rozdziera zdobycz. Pożerają dusze, zabierają bogactwa i kosztowności i mnożą wdowy pośród niej.
Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
26 Jej kapłani złamali moje prawo i plugawią moje święte rzeczy. Nie czynią różnicy między tym, co święte, a tym, co pospolite, nie rozsądzają między nieczystym a czystym. Ponadto zakrywają sobie oczy przed moimi szabatami, tak że doznaję zniewagi pośród nich.
Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
27 Jej książęta pośród niej są jak wilki rozdzierające zdobycz, rozlewające krew i tracące dusze, aby zdobyć nieuczciwy zysk.
Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
28 A jej prorocy tynkują słabym tynkiem, głosząc złudne widzenia i wróżąc im kłamstwo, mówiąc: Tak mówi Pan BÓG, choć PAN nie mówił.
Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
29 Lud tej ziemi dopuszcza się ucisku i dokonuje grabieży; krzywdzi ubogiego i nędznego i bezprawnie uciska cudzoziemca.
Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
30 I szukałem wśród nich męża, który by naprawił mur i stanął w wyłomie przede mną w obronie ziemi, abym jej nie zniszczył. Ale nie znalazłem żadnego.
“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
31 Wylałem więc na nich swój gniew, wyniszczyłem ich ogniem swojej zapalczywości. Złożyłem [im] na głowę ich własną drogę, mówi Pan BÓG.
Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”