< Wyjścia 17 >

1 Całe zgromadzenie synów Izraela wyruszyło z pustyni Sin, robiąc postoje, według rozkazu PANA, i rozbili obóz w Refidim, gdzie nie było wody, aby lud mógł się napić.
Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
2 Dlatego lud spierał się z Mojżeszem, mówiąc: Dajcie nam wody, abyśmy się napili. Mojżesz odpowiedział im: Dlaczego kłócicie się ze mną? Czemu wystawiacie PANA na próbę?
Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
3 Lud zaś pragnął tam wody i szemrał przeciwko Mojżeszowi, mówiąc: Po co wyprowadziłeś nas z Egiptu, aby uśmiercić nas, nasze dzieci i nasze bydło pragnieniem?
Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
4 Wtedy Mojżesz zawołał do PANA: Cóż mam uczynić z tym ludem? Jeszcze trochę, a mnie ukamienują.
Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
5 I PAN powiedział do Mojżesza: Idź przed ludem i weź ze sobą [niektórych] ze starszych Izraela. Weź także w rękę swoją laskę, którą uderzyłeś w rzekę, i idź.
Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
6 Oto stanę przed tobą tam, na skale na Horebie, i uderzysz w skałę, a wypłynie z niej woda, którą lud będzie pił. I Mojżesz uczynił tak na oczach starszych Izraela.
Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
7 I nadał temu miejscu nazwę Massa i Meriba z powodu kłótni synów Izraela i dlatego, że wystawili na próbę PANA, mówiąc: Czy PAN jest wśród nas, czy nie?
Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
8 Tymczasem Amalek nadciągnął, aby walczyć z Izraelem w Refidim.
Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
9 I Mojżesz powiedział do Jozuego: Wybierz nam mężczyzn, wyrusz i stocz bitwę z Amalekiem. Ja zaś jutro stanę na szczycie wzgórza z laską Boga w ręku.
Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
10 Jozue uczynił więc, jak mu Mojżesz rozkazał, i stoczył bitwę z Amalekiem. A Mojżesz, Aaron i Chur weszli na szczyt wzgórza.
Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
11 Gdy Mojżesz podnosił rękę, przeważał Izrael, a gdy opuszczał rękę, przeważał Amalek.
Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
12 Ale ręce Mojżesza [były] ociężałe. Wzięli więc kamień i podłożyli pod niego, i usiadł na nim. A Aaron i Chur podpierali jego ręce, jeden z jednej, drugi z drugiej strony. I jego ręce były stale podniesione aż do zachodu słońca.
Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
13 Jozue rozgromił więc Amaleka i jego lud ostrzem miecza.
Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
14 Wtedy PAN powiedział do Mojżesza: Zapisz to na pamiątkę w księdze i powtórz do uszu Jozuego, że wymażę zupełnie pamięć o Amaleku pod niebem.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
15 Potem Mojżesz zbudował ołtarz i nadał mu nazwę: PAN moją chorągwią;
Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
16 Bo powiedział: Ręka tronu PANA i wojna PANA będzie przeciwko Amalekowi z pokolenia na pokolenie.
Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”

< Wyjścia 17 >