< Efezjan 3 >
1 Dlatego ja, Paweł, więzień Chrystusa Jezusa dla was, pogan;
Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
2 Jeśli tylko słyszeliście o udzieleniu łaski Boga, która jest mi dana dla was;
Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
3 Że przez objawienie została mi oznajmiona tajemnica, jak to wam przedtem krótko napisałem.
ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
4 Dlatego czytając [to], możecie zrozumieć moje poznanie tajemnicy Chrystusa;
Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
5 Która w innych wiekach nie była znana synom ludzkim, jak teraz została objawiona jego świętym apostołom i prorokom przez Ducha;
chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
6 [Mianowicie], że poganie są współdziedzicami i [członkami] tego samego ciała, i współuczestnikami jego obietnicy w Chrystusie przez ewangelię.
Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
7 Stałem się jej sługą według daru łaski Boga danej mi przez działanie jego mocy.
Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
8 Mnie, najmniejszemu ze wszystkich świętych, została dana ta łaska, abym wśród pogan głosił te niezgłębione bogactwa Chrystusa;
Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
9 I żebym ujawnił wszystkim, jaka jest wspólnota tej tajemnicy ukrytej od wieków w Bogu, który wszystko stworzył przez Jezusa Chrystusa; (aiōn )
Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn )
10 Aby teraz wieloraka mądrość Boga poprzez kościół stała się jawna zwierzchnościom i władzom w [miejscach] niebiańskich;
Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
11 Zgodnie z wiecznym postanowieniem, które powziął w Chrystusie Jezusie, naszym Panu. (aiōn )
Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn )
12 W nim mamy śmiałość i przystęp z ufnością przez wiarę jego.
Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
13 Proszę zatem, abyście nie zniechęcali się z powodu moich utrapień, [jakie znoszę] dla was, bo to one są waszą chwałą.
Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
14 Dlatego zginam swoje kolana przed Ojcem naszego Pana Jezusa Chrystusa;
Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
15 Od którego cała rodzina na niebie i na ziemi bierze swoją nazwę;
amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
16 Aby według bogactwa swej chwały sprawił, żeby wasz wewnętrzny człowiek był utwierdzony mocą przez jego Ducha;
Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
17 Aby Chrystus przez wiarę mieszkał w waszych sercach, [abyście] zakorzenieni i ugruntowani w miłości;
kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
18 Mogli pojąć wraz ze wszystkimi świętymi, jaka jest szerokość, długość, głębokość i wysokość;
kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
19 I poznać miłość Chrystusa, która przewyższa wszelkie poznanie, abyście zostali napełnieni całą pełnią Boga.
Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
20 Temu zaś, który według mocy działającej w nas może uczynić o wiele obficiej ponad to wszystko, o co prosimy albo o czym myślimy;
Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
21 Jemu [niech będzie] chwała w kościele przez Chrystusa Jezusa po wszystkie pokolenia na wieki wieków. Amen. (aiōn )
Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )