< Kaznodziei 2 >

1 Powiedziałem w sercu: Niech teraz doświadczę cię w radości, zażywaj więc przyjemności. Lecz to także jest marnością.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake.
2 O śmiechu powiedziałem: To szaleństwo, a o radości: Co to daje?
“Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?”
3 Postanowiłem w sercu, [że] poddam swoje ciało winu – serce jednak kierowałem mądrością – i że będę się trzymać głupoty, aż zobaczę, co dla synów ludzkich jest dobrem spośród tego, co mają czynić pod niebem, przez wszystkie dni ich życia.
Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.
4 Dokonałem wielkich dzieł, zbudowałem sobie domy, zasadziłem sobie winnice.
Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa.
5 Założyłem sobie ogrody i sady i posadziłem w nich wszelkiego rodzaju drzewa owocowe.
Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse.
6 Zbudowałem też sobie stawy na wodę, by nawadniać nią las rosnących drzew.
Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija.
7 Nabyłem sługi i służące, miałem też sługi urodzone w swoim domu. Posiadałem również stada wołów i trzody owiec większe niż wszyscy, którzy byli przede mną w Jerozolimie.
Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe.
8 Zgromadziłem sobie srebro i złoto, i klejnoty królów i prowincji. Przygotowałem sobie śpiewaków i śpiewaczki, i [inne] rozkosze synów ludzkich oraz liczne instrumenty muzyczne.
Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu.
9 I tak stałem się większy i możniejszy niż wszyscy, którzy byli przede mną w Jerozolimie. W dodatku moja mądrość pozostała przy mnie.
Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.
10 Nie wzbraniałem swoim oczom niczego, czego pragnęły, nie odmawiałem swemu sercu żadnej uciechy; moje serce bowiem radowało się z całego mojego trudu. A to był mój dział za cały mój trud.
Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna; mtima wanga sindinawumane zokondweretsa. Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse, ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.
11 Następnie przyjrzałem się wszystkim dziełom, jakich dokonały moje ręce, i trudowi, jaki podjąłem dla ich wykonania, a oto wszystko to marność i utrapienie ducha i nie ma żadnego pożytku pod słońcem.
Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga, ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze, zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe, palibe chomwe ndinapindula pansi pano.
12 Odwróciłem się więc, aby przyjrzeć się mądrości, szaleństwu i głupocie. Co bowiem może [uczynić] człowiek, który nastąpi po królu? To, co czynili już inni.
Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani, komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani. Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani choposa chimene chinachitidwa kale?
13 I zobaczyłem, że mądrość jest pożyteczniejsza od głupoty, tak jak światło jest pożyteczniejsze od ciemności.
Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru, monga momwe kuwala kumapambanira mdima.
14 Mądry ma oczy w swojej głowie, głupi zaś chodzi w ciemności. A poznałem, że ten sam los spotyka wszystkich.
Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo, pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli; koma ndinazindikira kuti chomwe chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.
15 Dlatego powiedziałem w sercu: Los, który spotyka głupiego, spotka również mnie. Po co więc przewyższyłem go mądrością? Wtedy powiedziałem w sercu, że to także jest marnością.
Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga, “Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine. Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?” Ndinati mu mtima mwanga, “Ichinso ndi chopandapake.”
16 Nie ma bowiem pamięci zarówno o mądrym, jak i o głupcu na wieki, gdyż to, co jest teraz, w najbliższych dniach pójdzie w niepamięć. A jak umiera mądry? Tak jak głupi.
Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali; mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika. Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!
17 Dlatego obrzydło mi życie, gdyż przykre mi są wszystkie sprawy dokonane pod słońcem. Wszystko bowiem jest marnością i utrapieniem ducha.
Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
18 Zbrzydł mi nawet cały mój trud, który podejmowałem pod słońcem, gdyż muszę go zostawić człowiekowi, który przyjdzie po mnie.
Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga.
19 A kto wie, czy będzie mądry, czy głupi? A jednak będzie władać całą moją pracą, w którą włożyłem swój trud i mądrość pod słońcem. Także i to jest marnością.
Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake.
20 Doszedłem więc do tego, że zwątpiłem w sercu w cały swój trud, jaki podjąłem pod słońcem.
Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano.
21 Gdyż niejeden człowiek pracuje mądrze, umiejętnie i sprawiedliwie, a swój dział pozostawia innemu, który się nim nie trudził. Także i to jest marnością i wielkim złem.
Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu.
22 Cóż bowiem ma człowiek z całej swojej pracy i z utrapienia swego serca, którymi się trudzi pod słońcem?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano?
23 Bo wszystkie jego dni są cierpieniem, a jego zajęcie – smutkiem; nawet w nocy jego serce nie zaznaje spokoju. Także i to jest marnością.
Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.
24 Nie ma nic lepszego dla człowieka, niż aby jadł i pił, i czynił dobrze swojej duszy przy swojej pracy. Zobaczyłem też, że pochodzi to z ręki Boga.
Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu,
25 Kto bowiem potrafi jeść i cieszyć się tym słuszniej niż ja?
pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo?
26 Bo człowiekowi, który mu się podoba, daje mądrość, wiedzę i radość. Ale grzesznikowi zadaje trud, aby zbierał i gromadził, i potem zostawił to temu, który się Bogu podoba. Także i to jest marnością i utrapieniem ducha.
Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

< Kaznodziei 2 >