< Powtórzonego 18 >

1 Kapłani lewiccy oraz całe pokolenie Lewiego nie będą mieli działu ani dziedzictwa z Izraelem. Będą spożywać ofiary ogniowe PANA i jego dziedzictwo.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 Nie będą mieli dziedzictwa pośród swoich braci. PAN jest ich dziedzictwem, tak jak im powiedział.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 A taka będzie należność kapłanów od ludu, od tych, którzy składają ofiarę, czy to wołu, czy owcę: oddadzą kapłanowi łopatkę, obie szczęki i żołądek.
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 Oddasz mu pierwociny swego zboża, wina i oliwy oraz pierwociny wełny ze swoich owiec.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 Jego bowiem wybrał PAN, twój Bóg, ze wszystkich twoich pokoleń, aby stawał i służył w imię PANA, on i jego synowie, po wszystkie dni.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 A jeśli przyjdzie Lewita z jednego z twoich miast z całego Izraela, gdzie przebywa, a przyjdzie z całym pragnieniem swej duszy do miejsca, które PAN wybierze;
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 Wtedy będzie służyć w imię PANA, swego Boga, tak jak wszyscy jego bracia Lewici, którzy tam stoją przed PANEM.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 Będą jeść równą część oprócz tego, co mają ze sprzedaży ojcowizny.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 Gdy wejdziesz do ziemi, którą PAN, twój Bóg, ci daje, nie ucz się postępować według obrzydliwości tych narodów.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 Niech nie znajdzie się pośród was nikt, kto by przeprowadzał swego syna lub córkę przez ogień, ani wróżbita, ani wróżbiarz, ani jasnowidz, ani czarownik;
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 Ani zaklinacz, ani nikt, kto by wywoływał duchy, ani czarnoksiężnik, ani nekromanta.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 Każdy bowiem, kto czyni takie rzeczy, budzi odrazę w PANU. Z powodu tych obrzydliwości PAN, twój Bóg, wypędza przed tobą te [narody].
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 Będziesz doskonały przed PANEM, swoim Bogiem.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 Gdyż te narody, które opanujesz, słuchają wieszczbiarzy i wróżbitów, lecz tobie nie pozwala na to PAN, twój Bóg.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 PAN, twój Bóg, wzbudzi ci proroka podobnego do mnie spośród ciebie, spośród twoich braci. Jego będziecie słuchać;
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 Zgodnie z tym wszystkim, o co prosiłeś PANA, swego Boga, na Horebie, w dniu zgromadzenia: Niech już nie słucham głosu PANA, swego Boga, i niech już nie patrzę na ten wielki ogień, abym nie umarł.
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 Wtedy PAN powiedział do mnie: Słusznie powiedzieli.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 Wzbudzę im proroka podobnego do ciebie spośród ich braci i włożę moje słowa w jego usta, a on powie im wszystko, co mu rozkażę.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 I jeśli ktoś nie będzie posłuszny moim słowom, które będzie on mówić w moim imieniu, zażądam od niego [zdania sprawy].
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 Natomiast prorok, który odważy się mówić słowo w moim imieniu, którego mu nie nakazałem mówić, albo będzie mówił w imieniu obcych bogów, taki prorok poniesie śmierć.
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 A jeśli powiesz w swym sercu: Jak rozpoznamy to słowo, którego PAN nie wypowiedział?
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 Gdy prorok będzie coś mówił w imieniu PANA, a to się nie spełni ani nie nastąpi, to jest to słowo, którego PAN nie wypowiedział, lecz prorok mówił to z zuchwalstwa. Nie bój się go.
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Powtórzonego 18 >