< Daniela 5 >
1 Król Belszazar urządził wielką ucztę dla tysiąca swoich książąt i przed [tym] tysiącem pił wino.
Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
2 A gdy Belszazar pił wino, rozkazał przynieść złote i srebrne naczynia, które jego ojciec, Nabuchodonozor, zabrał ze świątyni w Jerozolimie, aby pili z niego król, jego książęta, jego żony i jego nałożnice.
Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
3 Wtedy przyniesiono złote naczynia, które zabrano ze świątyni domu Bożego, który był w Jerozolimie, i pili z nich król, jego książęta, jego żony i jego nałożnice.
Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
4 Pili wino i chwalili bogów ze złota i srebra, z brązu i żelaza, z drewna i kamienia.
Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
5 W tej samej godzinie ukazały się palce ręki ludzkiej, które pisały naprzeciw świecznika na wapnie ściany pałacu króla, a król widział część ręki, która pisała.
Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
6 Wtedy oblicze króla zmieniło się, jego myśli zatrwożyły go, stawy jego bioder rozluźniły się i jego kolana uderzały jedno o drugie.
Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
7 I zawołał król ze wszystkich sił, aby przyprowadzono astrologów, Chaldejczyków i wróżbitów. Król powiedział do mędrców Babilonu: Ktokolwiek to pismo odczyta i oznajmi mi jego znaczenie, będzie odziany w purpurę, [dadzą] mu złoty łańcuch na szyję i będzie panował w królestwie jako trzeci.
Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
8 Weszli więc wszyscy mędrcy króla, ale nie mogli odczytać pisma ani oznajmić królowi jego znaczenia.
Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
9 Wtedy król Belszazar bardzo się zatrwożył i jego oblicze się zmieniło, a jego książęta struchleli.
Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
10 Wówczas królowa weszła do domu uczty z powodu słów króla i jego książąt. Odezwała się królowa i powiedziała: Królu, żyj na wieki! Niech cię nie trwożą twoje myśli i niech się nie zmienia twoje oblicze.
Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
11 Jest w twoim królestwie mężczyzna, w którym [jest] duch świętych bogów, w którym za dni twego ojca znalazły się światło, rozum i mądrość podobna do mądrości bogów i którego król Nabuchodonozor, twój ojciec, [mówię ci], twój ojciec, król, ustanowił przełożonym magów, astrologów, Chaldejczyków i wróżbitów;
Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
12 Dlatego że znalazły się [w nim] nadzwyczajny duch, wiedza, rozum, wykładanie snów, objawianie zagadek i rozwiązywanie rzeczy trudnych, w Danielu, któremu król nadał imię Belteszassar. Niech [więc] teraz wezwą Daniela, a on oznajmi znaczenie [pisma].
Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
13 Wtedy Daniel został przyprowadzony do króla. A król zapytał Daniela: Czy ty jesteś tym Danielem z synów uprowadzonych z Judy, którego król, mój ojciec, sprowadził z ziemi Judy?
Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
14 Słyszałem o tobie, że duch bogów [jest] w tobie, że światło, rozum i obfita mądrość znajdują się w tobie.
Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
15 Właśnie przyprowadzono przede mnie mędrców i astrologów, aby mi to pismo odczytali i oznajmili jego znaczenie. Oni jednak nie potrafili tego zrobić.
Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
16 A słyszałem o tobie, że możesz dawać wyjaśnienie i rozwiązywać trudności. Jeśli więc teraz możesz to pismo odczytać i oznajmić mi jego znaczenie, będziesz odziany w purpurę, [będzie włożony] złoty łańcuch na twoją szyję i będziesz panował w królestwie jako trzeci.
Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
17 Wtedy Daniel odpowiedział przed królem: Twoje upominki niech pozostaną przy tobie, a twoje dary daj innemu; pismo jednak odczytam królowi i oznajmię mu znaczenie.
Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
18 Ty, królu, [posłuchaj]. Bóg Najwyższy dał Nabuchodonozorowi, twemu ojcu, królestwo, majestat, sławę i cześć;
“Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
19 A z powodu wielkości, którą mu dał, wszyscy ludzie, narody i języki drżały przed nim i bały się [go]. Kogo chciał, zabijał, a kogo chciał, zostawiał przy życiu, kogo chciał, wywyższał, a kogo chciał, poniżał.
Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
20 Ale gdy jego serce stało się wyniosłe i jego duch utwierdził się w pysze, został strącony z tronu swego królestwa i odebrano mu sławę;
Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
21 Został wypędzony spośród synów ludzkich, jego serce stało się podobne do [serca] zwierzęcia i mieszkał z dzikimi osłami. Żywili go trawą jak woły i jego ciało było skrapiane rosą z nieba, aż poznał, że Bóg Najwyższy ma władzę nad królestwem ludzkim i ustanawia nad nim, kogo chce.
Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
22 Ty, też, Belszazarze, jego synu, nie ukorzyłeś swego serca, chociaż o tym wszystkim wiedziałeś.
“Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
23 Lecz uniosłeś się przeciwko Panu nieba i naczynia jego domu przyniesiono przed ciebie, a ty, twoi książęta, twoje żony i twoje nałożnice piliście wino z nich. Ponadto chwaliłeś bogów ze srebra, złota, brązu, żelaza, drewna i kamienia, które nie widzą ani nie słyszą i nic nie wiedzą. Bogu zaś, w którego ręku jest twoje tchnienie i u którego są wszystkie twoje drogi, nie oddałeś czci.
Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
24 Dlatego przez niego została posłana część ręki i pismo to zostało napisane.
Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
25 A to jest pismo, które zostało napisane: Mene, Mene, Tekel, Uparsin.
“Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
26 Takie jest znaczenie tych słów: Mene: Bóg policzył twoje królestwo i doprowadził je do końca.
“Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
27 Tekel: Zważono cię na wadze i okazałeś się lekki.
Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
28 Peres: Twoje królestwo zostało podzielone i oddane Medom i Persom.
Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
29 Wtedy Belszazar wydał rozkaz i odziano Daniela w purpurę, złoty łańcuch włożono mu na szyję i ogłoszono o nim, że będzie panował jako trzeci w królestwie.
Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
30 Tej samej nocy Belszazar, król Chaldejczyków, został zabity.
Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
31 A Dariusz, Med, przejął królestwo, mając około sześćdziesięciu dwóch lat.
ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.