< Daniela 11 >

1 W pierwszym roku Dariusza Meda stanąłem, aby go pokrzepić i wzmocnić.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 A teraz oznajmię ci prawdę: Oto jeszcze trzej królowie będą panować w Persji, potem czwarty wzbogaci się o wiele bardziej niż wszyscy, a gdy się umocni w swoich bogactwach, podburzy wszystkich przeciw królestwu Grecji.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 I powstanie potężny król, który będzie sprawował wielką władzę, i będzie czynił według swojej woli.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 A gdy on się umocni, jego królestwo zostanie pokruszone i rozdzielone na cztery strony świata, ale nie między jego potomków i nie według władzy, jaką sprawował. Jego królestwo bowiem zostanie wykorzenione, a [dostanie się] innym, ale nie tym.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 Wtedy umocni się król południa oraz jeden z jego książąt. Ten będzie mocniejszy od niego i będzie panować, a jego władza będzie władzą rozległą.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Lecz po upływie kilku lat połączą się, bo córka króla południa przybędzie do króla północy, aby zawrzeć przymierze. Ona jednak nie otrzyma siły ramienia ani on nie ostoi się ze swoim ramieniem. Ale zostanie ona wydana, a [z nią] ci, którzy ją sprowadzili, jej syn oraz ten, co ją umacniał w tych czasach.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 Potem z latorośli jej korzenia powstanie [ktoś] na jego miejsce, kto nadciągnie ze swoim wojskiem, wkroczy do twierdzy króla północy, będzie rządził nimi i zwycięży.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Także ich bogów wraz z ich książętami i drogimi naczyniami ze srebra i złota uprowadzi do niewoli [do] Egiptu; i będzie bezpieczny [przez wiele] lat od króla północy.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 A król południa wtargnie do królestwa i wróci do swojej ziemi.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Ale jego synowie będą walczyć i zgromadzą mnóstwo wielkich wojsk. [Jeden z nich] nadciągnie z siłą jak powódź i przejdzie. Potem wróci i wojskiem będzie nacierać aż do jego twierdzy.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 Wtedy król południa, będąc rozjuszony, wyruszy i będzie walczył z nim, [to jest] z królem północy. Uszykuje wielkie mnóstwo, ale to mnóstwo zostanie wydane w jego rękę.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 A gdy to mnóstwo zostanie rozbite, jego serce się wywyższy, a choć powali dziesiątki tysięcy, nie umocni się.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Wróci bowiem król północy i uszykuje większe mnóstwo niż poprzednie, i po upływie kilku lat przyjdzie na pewno z wielkim wojskiem i mnóstwem bogactw.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 W tych czasach wielu powstanie przeciwko królowi południa. Synowie zbójców spośród twego ludu powstaną, aby utwierdzić widzenie, ale upadną.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Nadciągnie więc król północy, usypie wały i zdobędzie miasta warowne, a nie oprą się ramiona południa ani jego lud wybrany, i nie będą mieć siły, by stawić opór.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 [Ten], który nadciągnie przeciwko niemu, uczyni według swojej woli, i nie [będzie] nikogo, kto by mu się przeciwstawił; stanie też w pięknej ziemi, która zostanie zniszczona przez jego rękę.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Potem zwróci swoją twarz, aby przyjść z siłą całego swego królestwa, i będzie wyglądał, jakby [szukał zgody], i uczyni tak: da mu córkę piękną, aby doprowadził go przez nią do zguby. Ale ona nie [będzie] go wspierać ani nie będzie za nim.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Potem zwróci swoją twarz ku wyspom i zdobędzie [ich] wiele. Ale [pewien] wódz położy kres jego zniewadze, ponadto odpłaci mu za tę zniewagę.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 Dlatego zwróci swoją twarz ku twierdzom swojej ziemi, lecz potknie się i upadnie, i nie będzie [już] znaleziony.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 I powstanie na jego miejsce [taki], który roześle poborców w chwale królestwa. Ale po niewielu dniach zostanie zniszczony, lecz nie w gniewie ani nie w bitwie.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 Potem powstanie na jego miejsce [człowiek] godny pogardy, któremu nie dadzą godności królestwa. Przyjdzie jednak w pokoju i zdobędzie królestwo pochlebstwem.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 A ramionami, [jakby] powodzią, zostaną porwani sprzed jego oblicza i skruszeni, a także książę przymierza.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 Po zawarciu przymierza z nim będzie postępował zdradliwie. Nadciągnie bowiem i umocni się z niewielkim ludem.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 Nieoczekiwanie wkroczy nawet do najbogatszych miejsc prowincji i uczyni to, czego nie czynili jego ojcowie ani ojcowie jego ojców. Łup, zdobycz i bogactwo rozdzieli między nich. Uknuje plany przeciw warowniom, ale do czasu.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Potem pobudzi swoją moc i [swe] serce przeciw królowi południa z wielkim wojskiem. Król południa przygotuje się do walki z wielkim i potężnym wojskiem, ale się nie oprze, gdyż obmyślą przeciwko niemu zdradę.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Ci, którzy jedzą jego chleb, zniszczą go, gdy jego wojsko najedzie jak powódź, i padnie wielu zabitych.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Obaj królowie w swych sercach [będą mieli] złe zamiary i przy jednym stole będą mówić kłamstwa; ale to się [im] nie uda, gdyż koniec będzie w jeszcze [innym] wyznaczonym czasie.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Potem powróci do swojej ziemi z wielkim bogactwem, a jego serce zwróci się przeciwko świętemu przymierzu; tak będzie działał i wróci do swojej ziemi.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 W czasie wyznaczonym wróci i skieruje się na południe, ale nie powiedzie [mu] się tak [jak] za pierwszym i drugim [razem].
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Przeciwko niemu bowiem wyruszą okręty z Kittim, będzie przygnębiony, wróci i rozgniewa się na święte przymierze; tak będzie działał. I znowu wróci, i zawrze porozumienie z tymi, którzy opuścili święte przymierze.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 A powstaną przez niego wojska, które zbezczeszczą świątynię-twierdzę i [zniosą] codzienną [ofiarę], a postawią obrzydliwość spustoszenia.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 A tych, którzy będą postępować niegodziwie przeciwko przymierzu, splugawi pochlebstwem. Ale lud znający swego Boga umocni się i będzie działać.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 A rozumni wśród ludu będą nauczać wielu, ale będą padać od miecza, od ognia, od niewoli i od łupu przez wiele dni.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Gdy padną, będą mieli niewielką pomoc i wielu przyłączy się do nich pochlebstwem.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Spośród tych rozumnych niektórzy padną, aby byli doświadczeni, oczyszczeni i wybieleni aż do czasu ostatecznego, bo to jeszcze potrwa aż do czasu wyznaczonego.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 A król uczyni według swojej woli, wyniesie się i wywyższy się ponad każdego boga; będzie mówić dziwne rzeczy przeciwko Bogu bogów i poszczęści mu się, aż dokona się gniew. [To] bowiem, [co] zostało postanowione, dokona się.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 Nie będzie miał względu ani na boga swoich ojców, ani na pożądanie kobiet, ani na żadnego boga, gdyż wyniesie się ponad wszystko.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Zamiast tego będzie czcił boga twierdz; boga, którego nie znali jego ojcowie, będzie czcił złotem, srebrem i drogocennymi kamieniami, i kosztownościami.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Tak postąpi w twierdzach obcego boga, a którego uzna i obdarzy sławą. I sprawi, że będą panowali nad wieloma, i rozdzieli [im] ziemię jako zapłatę.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 A pod koniec czasu będzie z nim walczył król południa; ale król północy uderzy na niego jak burza z rydwanami, jeźdźcami i licznymi okrętami, wtargnie do krajów, zaleje [je] i przejdzie.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Potem wkroczy do pięknej ziemi i wiele [krajów] padnie. Te jednak ujdą z jego rąk: Edom, Moab i pierwsi z synów Ammona.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Wyciągnie swą rękę po kraje, a ziemia Egiptu nie zdoła mu ujść.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Opanuje skarby złota i srebra oraz wszystkie kosztowności Egiptu, a Libijczycy i Etiopczycy pójdą za nim.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Ale wieści ze wschodu i z północy przestraszą go. Dlatego wyruszy z wielkim gniewem, aby wielu wygubić i wytępić.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 I rozbije namioty swego pałacu między morzami na pięknej górze świętej; ale jego koniec przyjdzie na niego i nikt mu nie pomoże.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniela 11 >