< Amosa 5 >

1 Słuchajcie tego słowa, które jako lament podnoszę przeciwko wam, domu Izraela!
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 Upadła i już nie powstanie dziewica Izraela. Leży opuszczona w swej ziemi i nie ma nikogo, kto by ją podniósł.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Tak bowiem mówi Pan BÓG: W mieście, z którego wychodziło tysiąc, pozostanie sto, a w tym, z którego wychodziło sto, pozostanie domowi Izraela dziesięciu.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Tak bowiem mówi PAN do domu Izraela: Szukajcie mnie, a będziecie żyć;
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 A nie szukajcie Betel, nie chodźcie do Gilgal i do Beer-Szeby nie udawajcie się, gdyż Gilgal zostanie uprowadzony do niewoli, a Betel wniwecz się obróci.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Szukajcie PANA, a będziecie żyć, aby nie wybuchł jak ogień w domu Józefa i nie pochłonął go, a nie będzie nikogo w Betel, kto by go ugasił;
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 [Wy, którzy] zamieniacie sąd w piołun, a sprawiedliwość porzucacie na ziemi;
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 Szukajcie tego, który uczynił Plejady i Oriona, który przemienia cień śmierci w poranek i dzień w ciemności nocne; który przyzywa wody morskie i wylewa je na powierzchni ziemi, PAN jest jego imię;
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Który wzmacnia słabego przeciwko mocnemu, tak że [ten] osłabiony naciera na twierdzę.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Nienawidzą [tego], który upomina ich w bramie, i brzydzą się [tym], który mówi prawdę.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Ponieważ uciskacie ubogiego i zabieracie mu ciężar zboża, to chociaż pobudowaliście domy z kamienia ciosanego, nie będziecie w nich mieszkać; zasadzaliście rozkoszne winnice, ale nie będziecie pić z nich wina.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 Znam bowiem wasze wielkie przestępstwa i ogromne grzechy: uciskacie sprawiedliwego, bierzecie łapówkę i wypaczacie sprawy ubogich w bramie.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Dlatego roztropny milczy w tym czasie, bo jest to czas zły.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Szukajcie dobra, a nie zła, abyście żyli. A PAN, Bóg zastępów, będzie z wami, tak jak mówicie.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Nienawidźcie zła, a miłujcie dobro i ustanówcie sąd w bramie. Może wtedy PAN, Bóg zastępów, zlituje się nad resztką Józefa.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Dlatego tak mówi PAN, Bóg zastępów, Pan: Na wszystkich ulicach [będzie] zawodzenie, a na wszystkich drogach będą krzyczeć: Biada, biada! I zawołają oracza do płaczu, a tych, którzy umieją lamentować, do zawodzenia.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 I we wszystkich winnicach [będzie] zawodzenie, gdy przejdę pośród ciebie, mówi PAN.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Biada tym, którzy pragną dnia PANA! Cóż wam po tym dniu PANA? Jest on ciemnością, a nie światłością.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Jak gdyby ktoś uciekał przed lwem, a spotkał go niedźwiedź; albo jak gdyby wszedł do domu i oparł się ręką o ścianę, a ukąsiłby go wąż.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Czy dzień PANA nie jest ciemnością, a nie światłością? Mrokiem bez żadnej jasności?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Nienawidzę waszych uroczystych świąt [i] gardzę nimi, i woń na waszych zgromadzeniach nie jest mi miła.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Jeśli bowiem będziecie mi składać całopalenia i swoje ofiary pokarmowe, nie przyjmę [ich] ani nie wejrzę na ofiary pojednawcze z waszego tuczonego bydła.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Oddal ode mnie wrzask waszych pieśni, [bo] nie chcę słuchać dźwięku waszych cytr.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Niech raczej sąd tryska jak woda, a sprawiedliwość jak gwałtowny strumień.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Czy składaliście mi ofiary i dary na pustyni przez czterdzieści lat, domu Izraela?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Przecież nosiliście przybytek waszego Molocha i Kijuna, wasze bożki, gwiazdę waszych bogów, których sobie uczyniliście.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Dlatego uprowadzę was do niewoli poza Damaszek, mówi PAN, Bóg zastępów, [to] jego imię.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amosa 5 >