< Amosa 3 >
1 Słuchajcie tego słowa, które PAN mówi przeciwko wam, synowie Izraela, przeciwko całemu pokoleniu, które wyprowadziłem z ziemi Egiptu:
Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2 Tylko was uznałem spośród wszystkich rodów ziemi, dlatego was ukarzę za wszystkie wasze nieprawości.
“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
3 Czy dwóch może chodzić razem, jeśli się nie zgadzają?
Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
4 Czy lew zaryczy w lesie, gdy nie ma łupu? [Czy] młody lew wyda swój głos ze swojego legowiska, jeśli nic nie złowił?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
5 Czy ptak wpadnie w sidła na ziemi, jeśli nie ma pułapki? Czy podniesie się sidła z ziemi, jeśli nic nie schwytały?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
6 Czy trąba zadmie w mieście, a lud się nie ulęknie? Czy w mieście zdarzy się nieszczęście, którego PAN by nie uczynił?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7 Doprawdy, Pan BÓG nic nie czyni, jeśli nie objawi swojej tajemnicy swym sługom, prorokom.
Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
8 Lew ryknął, któż się nie ulęknie? Pan BÓG przemówił, któż nie będzie prorokował?
Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
9 Głoście w pałacach w Aszdodzie i w pałacach ziemi Egiptu i mówcie: Zbierzcie się na górach Samarii i zobaczcie w niej wielkie zamieszanie oraz cierpiących w niej ucisk;
Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10 Nie umieją bowiem czynić tego, co jest prawe, mówi PAN. Zbierają w swoich pałacach skarby ze zdzierstwa i z grabieży.
“Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11 Dlatego tak mówi Pan BÓG: Wróg otoczy tę ziemię i pozbawi cię twojej siły, i twoje pałace zostaną ograbione.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12 Tak mówi PAN: Jak pasterz wyrywa z lwiej paszczy dwie nogi lub kawałek ucha, tak zostaną wyrwani synowie Izraela, którzy mieszkają w Samarii na rogu łoża i w Damaszku na posłaniach.
Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13 Słuchajcie i oświadczcie w domu Jakuba, mówi Pan BÓG, Bóg zastępów;
“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14 Bo w tym dniu, w którym ukarzę Izraela za jego przestępstwa, ukarzę też ołtarze w Betel. I rogi ołtarza zostaną odcięte i upadną na ziemię.
“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
15 I zburzę dom zimowy i dom letni, zginą domy z kości słoniowej i dla wielkich domów nastanie koniec, mówi PAN.
Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.